< Job 8 >

1 Et Baldad de Sauchée répondant dit:
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 Jusqu'à quand parleras-tu de la sorte? Quel esprit verbeux s'exprime par ta bouche?
“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
3 Dieu est-il un juge prévaricateur? Le créateur de toutes choses torture-t- il l'équité?
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 Si tes fils ont péché devant lui, il leur a, de sa main, fait expier leurs fautes.
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
5 Commence donc dès l'aurore à prier le Seigneur tout-puissant.
Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 Si tu es pur et sincère, il t'exaucera et il te traitera selon sa justice.
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
7 Ce que tu possédais d'abord te semblera médiocre; ce que tu posséderas finalement sera inexprimable.
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
8 Remonte jusqu'à la première génération; suit à la trace les générations de nos pères.
“Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 Car nous sommes d'hier et nous ne savons rien; notre vie sur la terre est une ombre.
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 N'est-ce donc pas à nos pères de t'instruire, de t'éclairer, et de tirer de leur cœur les paroles que je vais dire?
Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 Le papyrus croît-il sans eau? L'herbe des prairies pousse-t-elle si elle n'est pas arrosée?
Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 La fauche-t-on quand elle est encore près de la racine? Et la plante que rien n'abreuve ne dessèche-t-elle pas?
Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 Ainsi finissent ceux que le Seigneur oublie, car l'espérance de l'impie est vaine.
Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 Sa maison sera déserte; sa tente disparaîtra comme une toile d'araignée.
Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 Il aura beau l'étayer, elle ne sera pas solide; dès qu'il en sera enlevé, elle s'écroulera.
Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 Il y a de l'humidité sous le soleil, une tige sort de la moisissure qu'elle engendre.
Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 Elle s'élève sur un tas de pierres; elle subsiste au milieu des cailloux.
mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 Et s'ils viennent à la dévorer, le lieu même se prêtera à nier son existence. N'as-tu pas vu pareille chose?
Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 N'est-ce pas comme cette tige que succombe l'impie? Une autre plante hors de terre germera.
Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 Jamais le Seigneur ne rejettera l'innocence; il n'acceptera pas les dons des pervers.
“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 Il mettra le sourire sur les lèvres des hommes sincères, et leur bouche sera pleine de ses louanges.
Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 Leurs ennemis seront couverts de honte; et il n'y aura pas de vie heureuse pour les méchants.
Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

< Job 8 >