< Job 41 >

1 Prendras-tu le serpent à l'hameçon? passeras-tu dans ses dents une bride?
“Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
2 Attacheras-tu à son nez un anneau? perceras-tu ses lèvres d'un cercle?
Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
3 Te parlera-t-il, te priera-t-il, te fera-t-il entendre de douces supplications?
Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
4 S'engagera-t-il avec toi par un pacte? En feras-tu ton esclave dans les siècles des siècles?
Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
5 Te joueras-tu de lui comme d'un oisillon, le mettras-tu en cage comme un passereau pour ton petit enfant?
Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
6 Les nations s'en nourrissent; les peuples phéniciens se le partagent.
Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
7 Ils attachent de sa peau à leurs navires, et sa tête à leurs barques de pêcheurs.
Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
8 Tu le maîtriseras en te souvenant de la guerre qu'il a causée, et qu'elle ne se renouvelle plus.
Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
9 Ne l'as-tu pas vu? N'as-tu pas été surpris de ce qui a été dit?
Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
10 N'as-tu pas été effrayé parce que je l'avais préparé? car quel est celui qui s'était opposé à moi?
Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
11 Et qui donc après m'avoir contredit persistera, puisque tout ce que le ciel recouvre m'appartient?
Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
12 Je ne me tairai point à cause lui, et la puissance de mes paroles, justes à son regard, excitera sa compassion.
“Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
13 Qui découvrira la face que voile son vêtement? qui pénétrera jusqu'au fond de sa poitrine?
Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
14 Qui ouvrira les portes qui le cachent? Le grincement de ses dents inspire à l'entour la terreur.
Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
15 Ses entrailles sont des aspics d'airain; son ensemble est comme de la pierre d'émeri.
Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
16 Les aspérités de son corps sont tout d'une pièce; jamais l'esprit de l'a traversé.
Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
17 Tel un homme est uni à son frère, tels ces deux frères sont toujours inséparables.
Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
18 S'il éternue des étincelles jaillissent; ses yeux brillent comme l'étoile du matin.
Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
19 Sa bouche vomit comme des lampes, leur flamme se répand à l'entour, comme des brasiers pleins de feu.
Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
20 De ses narines sort une fumée semblable à celle d'une fournaise où brûle de l'anthracite.
Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
21 Son âme est de charbon embrasé; sa bouche exhale du feu.
Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
22 La force réside en son encolure; la perdition court devant lui.
Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
23 Les chairs de son corps forment un bloc; elles ont été coulées sur lui; rien ne peut les émouvoir.
Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
24 Son cœur est condensé comme une pierre; il est inflexible comme une enclume.
Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
25 S'il se retourne, il répand l'effroi, parmi les bêtes fauves qui bondissent sur la terre.
Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
26 Les javelines, les traits, les cuirasses ne peuvent rien contre lui.
Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
27 Il fait cas de l'airain comme du bois pourri, et du fer comme de la paille.
Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
28 La flèche ne le percera pas; la pierre d'une fronde lui fait l'effet d'un brin d'herbe.
Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
29 Les marteaux sont pour lui comme des joncs; il rit des tremblements de terre et des éruptions de flammes.
Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
30 Il a pour couche des obélisques aigus; l'or de la mer qu'il foule aux pieds lui semble une boue dont on ne dit rien.
Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
31 Il fait bouillir l'abîme comme une marmite; il prend la mer pour un vase à parfums,
Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
32 Le Tartare de l'abîme pour un captif, l'abîme pour un lieu de promenade.
Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
33 Il n'est rien sur la terre de semblable à lui qui a été créé pour être raillé par mes anges.
Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
34 Il voit tout ce qui s'élève; il est roi de tout ce que contiennent les eaux.
Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”

< Job 41 >