< Jérémie 5 >

1 Parcourez les rues de Jérusalem, voyez et informez-vous, cherchez dans ses places si vous y trouverez un homme, s'il en est un seul qui fasse la justice et qui désire la foi; et je leur pardonnerai, dit le Seigneur.
“Pitani uku ndi uku mʼmisewu ya Yerusalemu, mudzionere nokha, funafunani mʼmabwalo ake. Ngati mungapeze munthu mmodzi amene amachita zachilungamo ndi kufunafuna choonadi, ndipo ndidzakhululukira mzinda uno.
2 Ils disent: Vive le Seigneur! et en cela ne font-ils pas un faux serment?
Ngakhale anthu akulumbira kuti, ‘Pali Yehova wamoyo,’ komabe akungolumbira mwachinyengo.”
3 Seigneur, vos yeux considèrent la foi; vous les avez flagellés, et ils ne l'ont point senti; vous les avez consumés, et ils n'ont point profité de la correction. Ils se sont fait un front plus dur que le roc, et n'ont point voulu se convertir.
Inu Yehova, kodi suja mumafuna anthu onena zoona? Inu munawakantha anthuwo, koma sanamve kupweteka; munawaphwanya anthuwo, koma sanatengepo phunziro. Anawumitsa mitima yawo ngati mwala ndipo anakaniratu kulapa.
4 Et j'ai dit: Peut-être sont-ils pauvres, et est-ce pour cela qu'ils sont faibles, et n'ont connu ni la voie du Seigneur ni le jugement de Dieu.
Ndiye ndinati, “Awa ndi amphawi chabe; anthu ochita zopusa. Sadziwa njira ya Yehova, sazindikira zimene Mulungu wawo amafuna.
5 J'irai donc vers les riches, et je leur parlerai; car ceux-là ont appris à connaître la voie du Seigneur et le jugement de Dieu; mais voilà qu'unanimement ils ont brisé le joug et mis en pièces les liens.
Tsono ndidzapita kwa atsogoleri ndi kukayankhula nawo; ndithu iwo amadziwa njira ya Yehova, amadziwa zomwe Mulungu wawo amafuna.” Koma ayi, iwonso anathyola goli la Yehova ndipo anadula msinga zawo.
6 C'est pourquoi, le lion sortant de la forêt les a blessés, et le loup les a détruits jusque dans leurs demeures, et la panthère s'est élevée contre leurs cités. Quiconque est issu d'eux sera poursuivi comme une proie, parce qu'ils ont multiplié leurs impiétés et se sont endurcis dans leurs rébellions.
Choncho mkango wochokera ku nkhalango udzawapha, mmbulu wochokera ku thengo udzawawononga, kambuku adzawabisalira pafupi ndi mizinda yawo kuti akhadzule aliyense amene adzayesera kutuluka mʼmizindamo pakuti kuwukira kwawo ndi kwakukulu ndipo abwerera mʼmbuyo kwambiri.
7 Comment puis-je leur être propice? Tes fils m'ont délaissé, et ils ont juré par ce qui n'est point Dieu; je les ai nourris en abondance, et ils ont commis des adultères, et ils ont logé dans les maisons des prostituées.
Yehova akuti, “Kodi ndingakukhululukireni bwanji ndi zimene mwachita? Ana anu andisiya Ine ndipo amapembedza milungu imene si milungu konse. Ine ndinawapatsa zonse zimene ankasowa, komabe iwo anachita chigololo namasonkhana ku nyumba za akazi achiwerewere.
8 Ils sont devenus comme des chevaux courant après des cavales; chacun; s'est mis à hennir auprès de la femme de son prochain:
Monga amachitira akavalo onenepa akamamemesa, aliyense wa iwo ankathamangira mkazi wa mnzake.
9 Est-ce que je ne les visiterai pas pour ces choses? dit le Seigneur; est- ce que mon âme ne tirera pas vengeance d'un tel peuple?
Tsono ndingaleke kuwalanga chifukwa cha zimenezi?” akutero Yehova. “Kodi nʼkuleka kuwulipsira mtundu woterewu?
10 Montez sur ses créneaux et renversez-les; mais ne la détruisez pas de fond en comble; laissez-en les fondations, parce qu'elles appartiennent au Seigneur.
“Pitani ku minda yake ya mipesa ndi kukayiwononga, koma musakayiwononge kotheratu. Sadzani nthambi zake pakuti anthu amenewa si a Yehova.
11 Parce que la maison d'Israël et la maison de Juda ont gravement prévariqué contre moi, dit le Seigneur.
Nyumba ya Israeli ndi nyumba ya Yuda onse akhala osakhulupirika kotheratu kwa Ine.”
12 Elles ont menti au Seigneur, disant: Les choses ne sont pas ainsi, les maux ne viendront pas sur nous, et nous ne verrons ni le glaive ni la famine.
Iwowa ankanama ponena za Yehova kuti, “Yehova sangachite zimenezi! Choyipa sichidzatigwera; sitidzaona nkhondo kapena njala.
13 Nos prophètes ont parlé en l'air, et la parole du Seigneur n'était pas en eux.
Mawu a aneneri azidzangopita ngati mphepo; ndipo mwa iwo mulibe uthenga wa Yehova. Choncho zimene amanena zidzawachitikira okha.”
14 A cause de cela, voici ce que dit le Seigneur tout-puissant: En punition de ce que vous avez ainsi parlé, voilà que je fais de mes paroles un feu dans ta bouche, et le peuple sera le bois, et le feu consumera le peuple.
Chifukwa chake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse akuti, “Popeza kuti anthu awa ayankhula mawu amenewa, tsono mawu anga ndidzawasandutsa moto mʼkamwa mwako ndipo anthu awa ndidzawasandutsa nkhuni zimene moto udzapserezeretu.
15 Je vais amener de loin une nation sur vous, ô maison d'Israël, dit le Seigneur, une nation dont vous n'entendrez pas le langage.
Inu Aisraeli,” Yehova akuti, “Ndikukubweretserani mtundu wa anthu ochokera kutali, ndi mtundu umene sunagonjetsedwepo, mtundu wakalekale umene chiyankhulo chawo inu simuchidziwa, zimene akunena inu simungazimvetse.
16 Ce sont tous des hommes forts.
Zida zawo za nkhondo zapha anthu ambirimbiri; onsewo ndi ankhondo amphamvu okhaokha.
17 Et ils mangeront votre moisson et votre pain; ils dévoreront vos fils et vos filles, ils dévoreront vos brebis et vos bœufs, ils dévoreront vos vignes, vos figuiers et vos oliviers, et ils détruiront de fond en comble, par le glaive, vos places fortes, en qui vous aviez mis votre confiance.
Adzakudyerani zokolola zanu ndi chakudya chanu, adzapha ana anu aamuna ndi aakazi; adzakupherani nkhosa zanu ndi ngʼombe zanu, adzawononga mpesa wanu ndi mikuyu yanu. Ndi malupanga awo adzagwetsa mizinda yanu yotetezedwa imene mumayidalira.
18 En ces jours-là, dit le Seigneur votre Dieu, je ne vous exterminerai pas entièrement.
“Komabe pa masiku amenewo sindidzakuwonongani kotheratu,” akutero Yehova.
19 Et lorsque vous direz: Pourquoi le Seigneur, notre Dieu, nous a-t-il fait ces choses? tu leur diras; En punition de ce que vous avez servi, dans votre terre, des dieux étrangers, vous aussi vous servirez des étrangers en une terre qui ne sera pas la vôtre.
Ndipo pamene anthu adzafunsa Yehova kuti, “Chifukwa chiyani Yehova Mulungu wathu wachita zimenezi?” Iwe udzawawuze kuti, “Monga momwe mwasiyira Ine ndi kutumikira milungu yachilendo mʼdziko mwanu, momwemonso mudzatumikira anthu a mʼdzikonso lachilendo.”
20 Publiez ces choses dans la maison de Jacob, et qu'elles soient entendues dans la maison de Juda.
“Lengeza izi kwa ana a Yakobo ndipo mulalikire kwa anthu a ku Yuda kuti,
21 Écoutez donc ces choses, peuplé insensé et sans cœur: qui avez des yeux, et ne voyez pas; qui avez des oreilles, et n'entendez pas.
Imvani izi, inu anthu opusa ndi opanda nzeru, inu amene maso muli nawo koma simupenya, amene makutu muli nawo koma simumva.
22 Ne me craindrez-vous point? dit le Seigneur; n'aurez-vous point de respect pour moi qui ai donné à la mer les sables pour limites? C'est un commandement éternel; et elle ne l'enfreindra point; elle s'agitera, mais elle ne prévaudra point; et ses flots bruiront, mais ils ne me désobéiront pas.
Kodi simuyenera kuchita nane mantha?” Akutero Yehova. “Kodi simuyenera kunjenjemera pamaso panga? Ine ndinayika mchenga kuti ukhale malire a nyanja, malire a muyaya amene nyanjayo singadutsepo. Mafunde angawombe motani, koma sangathe kupitirira malirewo; mafunde angakokome motani, koma sangadutse malirewo.
23 Le cœur de ce peuple est indocile et incrédule; ils se sont détournés et éloignés de moi.
Koma anthu awa ndi nkhutukumve ndiponso a mitima yowukira; andifulatira ndipo andisiyiratu.
24 Et ils n'ont point dit en leur âme: Craignons maintenant le Seigneur notre Dieu, qui nous a donné la pluie du printemps et cellede l'automne, comme il convient pour l'achèvement de la moisson au temps prescrit, et qui a veillé sur nous.
Sananenepo mʼmitima mwawo kuti, ‘Tiyeni tizipembedza Yehova Mulungu wathu. Kodi suja amatipatsa pa nthawi yake mvula yachizimalupsa ndi yamasika. Iye salephera konse kutipatsa nyengo ya kholola.’
25 Vos iniquités ont troublé ce cours des choses, et vos péchés ont éloigné de vous mes biens.
Koma zolakwa zanu zalepheretsa zonsezi; ndipo machimo anu akumanitsani zabwino.
26 Parce que, parmi mon peuple, il s'est trouvé des impies, et ils ont placé des pièges pour perdre les hommes, et ils les ont surpris.
“Pakati pa anthu anga pali anthu ena oyipa amene amabisalira anzawo monga amachitira mlenje mbalame ndiponso ngati amene amatchera misampha kuti akole anthu anzawo.
27 Tel un filet tendu est plein d'oiseaux, telle leur maison est pleine de fraude. Et c'est ainsi qu'ils sont devenus grands et se sont enrichis.
Nyumba zawo zadzaza ndi chuma chochipeza mwa chinyengo ngati zikwere zodzaza ndi mbalame. Nʼchifukwa chake asanduka otchuka ndi olemera.
28 Et ils ont transgressé la justice, et ils n'ont point jugé la cause de l'orphelin ni jugé celle de la veuve.
Ndipo ananenepa ndi kukhala ndi matupi osalala. Ntchito zawo zoyipa nʼzopanda malire; saweruza mwachilungamo nkhani ya ana amasiye kuti iyende bwino, sateteza ufulu wa anthu osauka.
29 Et pour tout cela est-ce que je ne les visiterai pas? dit le Seigneur; est-ce que mon âme ne tirera pas vengeance d'un tel peuple?
Kodi Ine ndingaleke kuwalanga chifukwa cha zimenezi? Kodi ndisawulipsire mtundu woterewu? Akutero Yehova.
30 La stupeur et l'horreur ont régné sur la terre.
“Chinthu chothetsa nzeru ndi choopsa kwambiri chachitika mʼdzikomo:
31 Les prophètes prophétisent l'iniquité; les prêtres applaudissent des mains, et mon peuple les aime pour avoir fait ainsi. Que pouvez-vous faire de plus après cela?
Aneneri akunenera zabodza, ndipo ansembe akuvomerezana nawo, ndipo anthu anga akukonda zimenezi. Koma mudzatani potsiriza?

< Jérémie 5 >