< Isaïe 7 >

1 Et dans les jours d'Achaz, fils de Joatham, fils d'Ozias, roi de Juda, il arriva que Rasin, roi d'Aram, et Phacée, fils de Romélie, roi d'Israël, marchèrent contre Jérusalem pour lui faire la guerre; mais ils ne purent la tenir assiégée.
Pamene Ahazi mwana wa Yotamu, mdzukulu wa Uziya anali mfumu ya Yuda, Rezini mfumu ya Siriya ndi Peka mwana wa Remaliya, mfumu ya Israeli anabwera kudzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu, koma sanathe kuwugonjetsa.
2 Et un message fut apporté en la maison de David, disant: Aram est coalisé avec Éphraïm. Et l'âme du roi fut saisie de stupeur, ainsi que l'âme de son peuple; comme dans une forêt les feuilles sont agitées par le vent.
Tsono nyumba ya Davide inawuzidwa kuti, “Dziko la Siriya lagwirizana ndi Efereimu.” Choncho mfumu Ahazi ndi anthu ake ananjenjemera, monga momwe mitengo ya mʼnkhalango imagwedezekera ndi mphepo.
3 Et le Seigneur dit à Isaïe: Va à la rencontre d'Achaz, toi et ton fils Jasub qui te reste; prends le chemin d'en haut dans le champ du Foulon près la piscine;
Pamenepo Yehova anawuza Yesaya kuti, “Tuluka, iwe ndi mwana wako Seariyasubu, mupite mukakumane ndi Ahazi kumapeto kwa ngalande yamadzi yochokera ku Dziwe Lakumtunda, pa msewu wopita ku Munda wa mmisiri wochapa nsalu.
4 Et dis au roi: Tiens-toi en repos, et sois sans crainte; que ton âme ne soit pas abattue par ces deux bouts de tison qui fument; car, lorsque le transport de ma colère éclatera, je te guérirai encore une fois.
Ukamuwuze kuti, ‘Chenjera, khala phee ndipo usaope. Usataye mtima chifukwa cha zitsa ziwiri zomwe zikufuka, chifukwa cha ukali woopsa wa Rezini ndi Siriya, ndiponso wa Peka mwana wa Remaliya.
5 Quant au fils d'Aram et au fils de Romélie, parce qu'ils ont conçu un mauvais dessein, disant:
Mfumu ya Siriya, Efereimu ndi mwana wa Remaliya apangana kuti akuchitire choyipa. Akunena kuti,
6 Montons en Judée, et, nous liguant contre eux, soumettons-les à nous, et donnons-leur pour roi le fils de Tabéel;
‘Tiyeni tikalimbane ndi Yuda. Tiyeni tiliwononge ndi kuligawa; tiligawane pakati pathu, ndipo tilonge ufumu mwana wa Tabeeli kumeneko.’
7 Voici ce que dit le Seigneur des armées: Ce complot ne subsistera pas, il ne s'accomplira point.
Komabe zimene akunena Ambuye Yehova ndi izi: “‘Zimenezo sizidzatheka, sizidzachitika konse,
8 Mais Damas restera la capitale de Syrie, et Rasin, roi de Damas. Et soixante-cinq ans encore, le royaume d'Éphraïm cessera d'être un peuple,
pakuti Siriya amadalira Damasiko, ndipo Damasiko amadalira mfumu Rezini basi. Zisanathe zaka 65 Efereimu adzawonongedwa kotheratu, sadzakhalanso mtundu wa anthu.
9 Et Samarie, la capitale d'Éphraïm, et le fils de Romélie, la capitale de Samarie. Et si vous ne me croyez point, c'est que vous manquerez d'intelligence.
Dziko la Efereimu limadalira Samariya ndipo Samariya amadalira mwana wa Remaliya basi. Mukapanda kulimbika pa chikhulupiriro chanu, ndithu simudzalimba konse.’”
10 Et le Seigneur continua de parler à Achaz, disant:
Yehova anayankhulanso ndi Ahazi,
11 Demande un signe au Seigneur ton Dieu, soit dans le ciel, soit dans l'abîme. (Sheol h7585)
“Pempha chizindikiro kwa Yehova Mulungu wako, chikhale chozama ngati manda kapena chachitali ngati mlengalenga.” (Sheol h7585)
12 Et Achaz dit: Non, je ne demanderai rien, et je ne tenterai point le Seigneur.
Koma Ahazi anati, “Ine sindipempha; sindikufuna kuyesa Yehova.”
13 Et le Seigneur reprit: Écoutez donc, maison de David. Est-ce pour vous si peu de chose que de soutenir une lutte contre des hommes? Et comment soutiendrez-vous une lutte contre Dieu?
Apo Yesaya anati, “Imva tsopano, iwe nyumba ya Davide! Kodi sikokwanira kutopetsa anthu? Kodi mudzayeseranso kutopetsa Mulungu wanga?
14 C'est pourquoi le Seigneur lui-même vous donnera un signe. Voilà que la Vierge concevra dans son sein, et elle enfantera un fils, et tu lui donneras le nom d'Emmanuel.
Nʼchifukwa chake Ambuye mwini adzakupatsani chizindikiro: Onani, namwali adzakhala woyembekezera ndipo adzabala mwana wamwamuna, ndipo mwanayo adzamutcha Imanueli.
15 Il mangera du beurre et du miel, avant de savoir discerner le mal ou choisir le bien.
Azidzadya chambiko ndi uchi, mpaka atadziwa kukana choyipa ndi kusankha chabwino.
16 Aussi même avant de connaître le bien et le mal, cet enfant rejettera le mal, pour choisir le bien. Et cette terre, que tu crains, elle sera abandonnée de la présence de ces deux rois.
Koma nthawi yokana choyipa ndi kusankha chabwino kwa mwanayo isanafike, mayiko a mafumu awiri amene amakuopsaniwo adzakhala atasanduka bwinja.
17 Et le Seigneur enverra sur toi, et sur ton peuple, et sur la maison de ton père, des jours tels qu'il n'en est point venu depuis le jour où Éphraïm a repoussé de Juda le roi des Assyriens.
Yehova adzabweretsa pa inu, pa anthu anu ndiponso pa nyumba ya bambo wanu masiku a mavuto woti sanakhalepo kuyambira tsiku limene Efereimu anapatukana ndi Yuda. Yehova adzabweretsa mfumu ya ku Asiriya.”
18 Et voici ce qui arrivera: en ce jour le Seigneur sifflera pour appeler les mouches qui dominent sur une partie du fleuve d'Égypte, et les abeilles qui sont dans la région d'Assyrie.
Tsiku limenelo Yehova adzalizira likhweru ntchentche zochokera ku mitsinje yakutali ku Igupto, ndiponso njuchi zochokera ku dziko la Asiriya.
19 Et elles viendront toutes dans les vallons de la terre, et dans les creux des rochers, et dans les cavernes, et dans tous les ravins.
Onsewo adzafika ndi kudzakhazikika mu zigwa zozama, mʼmingʼalu ya matanthwe ndi mʼzitsamba zonse zaminga ndiponso ponse pamene pali malo omwetsera ziweto.
20 Ce jour-là, avec un rasoir loué sur les rives du fleuve du roi assyrien, le Seigneur rasera la tête de son peuple, et lui ôtera les poils de ses pieds et de sa barbe.
Tsiku limenelo Ambuye adzalemba ganyu ometa ochokera kutsidya kwa Mtsinje, ndiye mfumu ya ku Asiriya, kudzameta tsitsi lanu la ku mutu ndi la mʼmiyendo ndi ndevu zomwe.
21 Et en ce jour un homme à peine nourrira une vache et deux brebis.
Tsiku limenelo adzangosunga ngʼombe yayikazi yayingʼono ndi mbuzi ziwiri.
22 Et, au lieu de boire du lait en abondance, tout homme resté dans la contrée à peine y mangera du beurre et du miel.
Ndipo chifukwa cha kuchuluka kwa mkaka umene ziwetozi zidzapereka, munthuyo azidzadya chambiko. Aliyense amene adzatsalire mʼdzikomo azidzadya chambiko ndi uchi.
23 Et en ce jour il arrivera que tout lieu où il y aura eu des milliers de vignes, estimées des milliers de sicles, sera aride et couvert de ronces.
Tsiku limenelo, paliponse pamene panali mitengo ya mpesa 1,000 ndipo mtengo wake ndi wokwana masekeli asiliva 1,000, padzamera mkandankhuku ndi minga.
24 On y entrera avec l'arc et la flèche, parce que toute la terre sera aride et couverte de ronces;
Anthu adzapita kumeneko kukachita uzimba ali ndi uta ndi mivi, popeza kuti mʼdziko monsemo mudzakhala mkandankhuku ndi minga.
25 Et toute montagne jadis labourée sera inculte. Et la crainte ne l'envahira plus; car, à cause de son aridité et de ses ronces, ce ne sera plus qu'un pâturage pour les brebis et un passage pour les bœufs.
Ndipo mʼmapiri monse mʼmene kale munkalimidwa ndi khasu, simudzapitamo kuopa mkandankhuku ndi minga; malowo adzasanduka odyetserako ngʼombe ndi nkhosa.

< Isaïe 7 >