< Isaïe 65 >

1 Je me suis manifesté à ceux qui ne me demandaient point; j'ai été trouvé par ceux qui ne me cherchaient pas; j'ai dit à un peuple qui n'avait point invoqué mon nom: Me voici.
“Ndinali wokonzeka kumva mapemphero a amene sankandipempha kanthu; ndipo ndinalola kuti anthu amene ankandifunafuna kuti andipeze. Kwa mtundu wa anthu umene sunkapempha chithandizo kwa Ine, ndinati, ‘Ine ndili pano, Ine ndili pano.’
2 Durant tout le jour j'ai tendu les mains à un peuple désobéissant et contradicteur, à des hommes qui marchaient non dans la bonne voie, mais à la suite de leurs péchés.
Tsiku lonse ndatambasulira manja anga anthu owukira aja, amene amachita zoyipa, natsatira zokhumba zawo.
3 Ce peuple est celui qui ne cesse pas de m'irriter en face; ils sacrifient dans leurs jardins, et ils brûlent de l'encens sur des briques, pour des divinités qui n'existent pas.
Ndatambasulira manja anga anthu aja amene nthawi zonse amandikwiyitsa mopanda manyazi. Iwo amapereka nsembe mʼminda ndi kufukiza lubani pa maguwa ansembe a njerwa.
4 Ils se couchent sur des sépulcres ou des cavernes, à propos de leurs songes; et ils mangent de la chair de porc avec le jus de leurs victimes; et tous leurs vases sont souillés.
Amakatandala ku manda ndipo amakachezera usiku wonse kumalo obisika. Amadya nyama ya nkhumba, ndipo mʼmiphika mwawo muli msunzi wa nyama yodetsedwa.
5 Ce sont eux qui disent: Loin de moi, ne m'approche pas; car je suis pur. Mon courroux les réduira en fumée, et en eux brûlera un feu éternel.
Amawuza ena kuti, ‘Khala patali usandiyandikire, chifukwa ungatengere kupatulika kwanga!’ Ukali wanga pa anthu otere uli ngati utsi mphuno zanga, ngati moto umene umayaka tsiku lonse.
6 Voilà qu'il est écrit devant mes yeux: Je ne garderai point le silence jusqu'à ce que j'aie puni dans leur sein
“Taonani, ndatsimikiza kale mlandu ndi chilango chawo; sindidzakhala chete koma ndidzawalanga kwathunthu chifukwa cha machimo awo
7 Leurs péchés et ceux de leurs pères, dit le Seigneur. Ceux qui ont sacrifié sur les montagnes, ceux qui m'ont outragé sur les collines, recevront dans leur sein la punition de leurs œuvres.
ndi a makolo awo,” akutero Yehova. “Chifukwa anapereka nsembe zopsereza pa mapiri ndi kundinyoza Ine pa zitunda zawo, Ine ndidzawalanga kwathunthu potsata zimene anachita kale.”
8 Ainsi dit le Seigneur: De même que s'il se trouve un grain mûr dans un verjus, on dit: Ne le gâtez point, parce que la bénédiction est en lui; ainsi ferai-je pour l'amour d'un seul qui me sert; pour l'amour de celui-là je ne les détruirai pas tous.
Yehova akuti, “Pamene madzi akanapezeka mu phava la mphesa ndipo anthu amati, ‘Musawononge phavalo, popeza madzi ena abwino akanalimobe mʼphavalo,’ Inenso chifukwa cha mtumiki wanga; sindidzawononga onse.
9 Et je délivrerai la postérité de Jacob et de Juda; elle aura pour héritage ma montagne sainte; mes élus et mes serviteurs l'auront pour héritage, et ils y demeureront.
Ndidzatulutsa zidzukulu mʼbanja la Yakobo, ndipo a banja la Yuda adzalandira mapiri anga ngati cholowa chawo. Anthu anga osankhidwa adzalandira zimenezi, ndipo atumiki anga adzakhala kumeneko.
10 Et il y aura dans la forêt des bergeries pour les menus troupeaux; et dans la vallée d'Achor se reposeront les bœufs de mon peuple, de ceux qui m'auront cherché.
Chigwa cha Saroni chidzakhala kodyetserako nkhosa, ndipo chigwa cha Akori chidzakhala malo opumirako ngʼombe kwa anthu anga ondifunafuna Ine.
11 Et vous qui m'abandonnez et qui oubliez ma montagne sainte, qui dressez une table pour le démon et qui mêlez le vin pour faire des libations à la fortune,
“Koma inu amene mumasiya Yehova ndi kuyiwala phiri langa lopatulika, amene munamukonzera Gadi chakudya ndi kuthirira Meni chakumwa,
12 Je vous livrerai au glaive, vous tomberez sous le couteau; car je vous ai appelés, et vous ne m'avez point obéi; j'ai parlé, et vous n'avez pas entendu, et devant moi vous avez fait le mal, et ce que je rejetais, vous l'avez choisi.
ndidzakuperekani ku lupanga ngati nsembe, ndipo nonse mudzaphedwa; chifukwa simunayankhe pamene ndinakuyitanani, ndinayankhula koma simunamvere. Munachita zoyipa pamaso panga ndipo munasankha kuchita zoyipa zomwe sindikondwera nazo.”
13 C'est pourquoi, voici ce que dit le Seigneur: Ceux qui me servent mangeront; et vous, vous aurez faim; ceux qui me servent boiront, et vous, vous aurez soif.
Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, “Atumiki anga adzadya, koma inu mudzakhala ndi njala; atumiki anga adzamwa, koma inu mudzakhala ndi ludzu; atumiki anga adzakondwa, koma inu mudzakhala ndi manyazi.
14 Ceux qui me servent vivront dans la joie, et vous, vous serez confondus; ceux qui me servent tressailliront d'allégresse, et vous, vous crierez dans la tristesse de votre cœur, et vous hurlerez dans le déchirement de votre esprit.
Atumiki anga adzayimba mosangalala, koma inu mudzalira kwambiri chifukwa chovutika mu mtima ndipo mudzalira mofuwula chifukwa mudzamva kuwawa mu mtima.
15 Et vous laisserez votre nom comme un objet de dégoût à mes élus, et le Seigneur vous détruira, et un nom nouveau sera donné à ceux qui le servent.
Anthu anga osankhidwa adzatchula dzina lanu potemberera. Ambuye Yehova adzakuphani, koma atumiki ake adzawapatsa dzina lina.
16 Et ce nom sera béni sur la terre; car ils béniront le Dieu véritable; et ceux qui jureront sur la terre jureront par le Dieu véritable; ils oublieront leur ancienne affliction, qui ne reviendra plus en leur cœur.
Aliyense wopempha dalitso mʼdzikomo adzachita zimenezo kwa Mulungu woona; ndipo aliyense wochita malumbiro mʼdzikomo adzalumbira mwa Mulungu woona. Pakuti mavuto akale adzayiwalika ndipo adzachotsedwa pamaso panga.
17 Car il y aura un ciel nouveau et une terre nouvelle; on ne se souviendra plus des choses d'autrefois, et le souvenir n'en reviendra plus en leur cœur.
“Taonani, ndikulenga mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano. Zinthu zakale sizidzakumbukika, zidzayiwalika kotheratu.
18 Mais ils y trouveront la joie et l'allégresse; car moi-même je ferai de Jérusalem l'allégresse, et de mon peuple la joie.
Koma inu mukhale osangalala ndi okondwa mpaka muyaya chifukwa cha zimene ndikulenga, pakuti ndikulenga Yerusalemu kukhala malo wosangalatsa ndipo anthu ake adzakhala achimwemwe.
19 Et à mon tour je ferai de Jérusalem mes délices, et de mon peuple ma joie; et l'on n'y entendra plus la voix des pleurs, ni celle des gémissements.
Ine ndidzakondwa chifuwa cha Yerusalemu ndipo ndidzasangalala chifukwa cha anthu anga. Kumeneko sikudzamvekanso kulira ndi mfuwu wodandaula.
20 Il n'y aura plus là ni enfant qui meure avant l'âge, ni vieillard qui ne remplisse son temps. Le jeune homme vivra cent ans, et le pécheur à sa mort aura aussi cent ans; mais celui-là sera maudit.
“Ana sadzafa ali akhanda ndipo nkhalamba zonse zidzakwaniritsa zaka zawo zonse. Wamngʼono mwa iwo adzafa ali ndi zaka 100. Amene adzalephere kufika zaka 100 adzatengedwa kukhala wotembereredwa.
21 Et ils bâtiront des maisons, et ils y demeureront, et ils y planteront des vignes, et ils en mangeront les fruits.
Anthu adzamanga nyumba ndi kukhalamo, adzadzala mpesa ndipo adzadya zipatso zake.
22 Et ils ne bâtiront plus pour autrui, et ils ne planteront plus pour que d'autres mangent. Les jours de mon peuple seront comme les jours de l'arbre de vie, et les travaux où ils auront pris de la peine atteindront la vieillesse.
Sadzamanganso nyumba anthu ena nʼkukhalamo, kapena kudzala ndi ena nʼkudya. Pakuti anthu anga adzakhala ndi moyo wautali ngati mitengo. Osankhidwa anga adzakondwera ndi ntchito ya manja awo nthawi yayitali.
23 Mes élus ne se fatigueront pas en vain; ils n'auront point d'enfants pour leur malédiction, car c'est une race bénie de Dieu; et leurs petits enfants comme eux seront bénis.
Sadzagwira ntchito pachabe kapena kubereka ana kuti aone tsoka; chifukwa adzakhala anthu odalitsidwa ndi Yehova, iwowo pamodzi ndi adzukulu awo omwe.
24 Et avant qu'ils aient crié je les aurai exaucés; pendant qu'ils parleront encore, je dirai: Qu'y a-t-il?
Ndidzawayankha ngakhale asanathe nʼkupempha komwe. Pamene akuyankhula kumene Ine ndidzakhala nditamva kale.
25 Alors les loups et les agneaux viendront paître ensemble; le lion mangera de la paille comme le bœuf, et le serpent mangera la terre comme du pain. Ils ne nuiront à personne; ils ne détruiront rien sur ma montagne sainte, dit le Seigneur.
Mʼmbulu ndi mwana wankhosa wamkazi zidzadyera pamodzi. Mkango udzadya udzu monga ngʼombe, koma fumbi ndiye chidzakhale chakudya cha njoka. Pa phiri langa lopatulika sipadzakhala chinthu chopweteka kapena chowononga,” akutero Yehova.

< Isaïe 65 >