< Isaïe 24 >

1 Voilà que le Seigneur va dévaster la terre; il va la rendre déserte; il va dévoiler sa face et disperser ceux qui habitent en elle.
Taonani, Yehova adzawononga dziko lapansi ndi kulisandutsa chipululu; Iye adzasakaza maonekedwe ake ndi kumwaza anthu ake onse.
2 Et le peuple sera comme le prêtre, le serviteur comme le maître, et la servante comme la maîtresse; le marchand sera comme l'acheteur, le préteur comme l'emprunteur, et le débiteur comme le créancier.
Aliyense zidzamuchitikira mofanana: wansembe chimodzimodzi munthu wamba, antchito aamuna mofanananso ndi ambuye awo aamuna, antchito aakazi chimodzimodzi ambuye awo aakazi, wogula chimodzimodzi wogulitsa, wobwereka chimodzimodzi wobwereketsa, okongola chimodzimodzi okongoza.
3 La terre sera entièrement détruite, la terre sera entièrement dépouillée; car la bouche du Seigneur a dit ces choses:
Dziko lapansi lidzawonongedwa kwathunthu ndi kusakazikiratu. Yehova wanena mawu awa.
4 La terre est dans le deuil, le monde est désolé, les grands de la terre ont pleuré.
Dziko lapansi likulira ndipo likufota, dziko lonse likuvutika ndipo likuwuma, anthu omveka a dziko lapansi akuvutika.
5 Elle a péché par ceux qui l'habitent, parce qu'ils ont transgressé la loi et altéré les commandements de l'éternelle alliance.
Anthu ayipitsa dziko lapansi; posamvera malangizo ake; pophwanya mawu ake ndi pangano lake lamuyaya.
6 C'est pourquoi une malédiction consumera cette terre en punition du péché de ceux qui l'habitent. C'est pourquoi ses habitants seront pauvres, et il n'y restera qu'un petit nombre d'hommes.
Nʼchifukwa chake matemberero akuwononga dziko lapansi; anthu a mʼdzikomo akuzunzika chifukwa cha kulakwa kwawo, iwo asakazika ndipo atsala ochepa okha.
7 Le vin pleurera, la vigne pleurera; et ils gémiront, tous ceux qui avaient l'âme en joie;
Vinyo watsopano watha ndipo mphesa zikufota; onse okonda zosangalatsa ali ndi chisoni.
8 Il a cessé, le bruit joyeux des tambours; elle a cessé, la voix de la cithare.
Kulira kokometsera kwa matambolini kwatha, phokoso la anthu osangalala latha, zeze wosangalatsa wati zii.
9 Les hommes sont confondus; ils ne boivent plus de vin, et la bière est pleine d'amertume pour ceux qui en boivent.
Anthu sadzayimbanso akumwa vinyo; akadzamwa zaukali zidzakhala zowawa mʼkamwa mwawo.
10 Toute la ville est déserte; elle ferme ses maisons pour qu'on n'y puisse entrer.
Mzinda wachisokonezo uja wawonongeka; nyumba iliyonse yatsekedwa.
11 Partout elle crie pour avoir du vin; toute joie sur la terre a cessé, toute joie est partie de la terre,
Anthu akulira mʼmisewu kufuna vinyo; chimwemwe chonse chatheratu, palibenso chisangalalo pa dziko lapansi.
12 Et les villes seront inhabitées, et les maisons vides crouleront.
Mzinda wasanduka bwinja zipata zake zagumuka.
13 Toutes ces choses arriveront sur la terre au milieu des nations. Et de même que l'on secoue un olivier, ainsi seront-elles secouées. Et si la vendange s'arrête,
Zimenezi ndizo zidzachitikire mitundu yonse ya dziko lapansi ndiponso pakati pa mitundu ya anthu. Zidzakhala ngati pamene mitengo ya olivi yayoyoledwa, kapena ngati nthawi ya kunkha la mphesa atatsiriza kukolola.
14 Ils pousseront de grandes clameurs; mais ceux qui auront été épargnés sur la terre se réjouiront tous ensemble de la gloire du Seigneur, et la mer en sera troublée dans ses eaux.
Koma otsala onse akufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe; anthu akumadzulo akutamanda ukulu wa Yehova.
15 C'est pourquoi la gloire du Seigneur ira jusqu'aux îles de la mer, le nom du Seigneur y sera glorifié.
Nʼchifukwa chake inu akummawa, tamandani Yehova; ndi inu okhala mʼmphepete mwa nyanja kwezani dzina la Yehova, Mulungu wa Israeli.
16 Seigneur Dieu d'Israël, des extrémités de la terre nous avons appris vos prodiges, vous, espérance de l'homme pieux. Et l'on dira: Malheur aux prévaricateurs qui transgressent la loi!
Kuchokera kumalekezero a dziko lapansi tikumva kuyimba kotamanda “Wolungamayo.” Koma ine ndinati, “Ndatheratu, ndatheratu! Tsoka kwa ine! Anthu achinyengo akupitirizabe kuchita zachinyengo, inde chinyengo chawo chikunkerankera mʼtsogolo.”
17 La peur, l'abîme et les pièges sont pour vous qui habitez la terre.
Inu anthu adziko lapansi, zoopsa, dzenje ndi msampha zikukudikirani.
18 Et voici ce qui arrivera: celui qui fuira de peur tombera dans l'abîme; et celui qui sortira de l'abîme sera pris au piège; car les cataractes du ciel seront ouvertes, et les fondements de la terre en seront ébranlés.
Aliyense wothawa phokoso la zoopsa adzagwa mʼdzenje; ndipo aliyense wotuluka mʼdzenjemo adzakodwa ndi msampha. Zitseko zakumwamba zatsekulidwa, ndipo maziko a dziko lapansi agwedezeka.
19 La terre sera pleine de trouble, la terre sera pleine d'angoisse.
Dziko lapansi lathyokathyoka, ndipo lagawika pakati, dziko lapansi lagwedezeka kotheratu.
20 Elle s'est détournée de sa voie comme un homme ivre et débauché; elle sera chancelante comme la cabane du gardien des vergers; et parce que l'iniquité a prévalu en elle, elle tombera et ne pourra se relever.
Dziko lapansi likudzandira ngati munthu woledzera likugwedezeka ndi mphepo ngati chisimba; lalemedwa ndi machimo ake. Lidzagwa ndipo silidzadzukanso.
21 Et le Seigneur étendra sa main sur l'armée du ciel et sur les rois de la terre.
Tsiku limenelo Yehova adzalanga amphamvu a kumwamba ndiponso mafumu apansi pano.
22 Et la grande Synagogue de la terre sera réunie et jetée en prison; et la forteresse sera fermée; et après plusieurs générations ils seront visités.
Mulungu adzawasonkhanitsa pamodzi ngati amʼndende amene ali mʼdzenje. Adzawatsekera mʼndende ndipo adzalangidwa patapita nthawi yayitali.
23 Et la brique sera liquéfiée, et le mur croulera; parce que le Seigneur règnera du haut de Sion et de Jérusalem, et en présence des anciens il sera glorifié.
Mwezi udzanyazitsidwa, dzuwa lidzachita manyazi; pakuti Yehova Wamphamvuzonse adzakhala mfumu ndipo adzalamulira; pa Phiri la Ziyoni ndi ku Yerusalemu, ndipo adzaonetsa ulemerero wake pamaso pa akuluakulu.

< Isaïe 24 >