< Isaïe 19 >

1 Oracle sur l'Égypte. Voici que le Seigneur s'est assis sur une nuée légère, et il arrivera en Égypte, et les idoles de l'Égypte seront ébranlées devant sa face, et elle faiblira au fond de son cœur.
Uthenga onena za Igupto: Taonani, Yehova wakwera pa mtambo waliwiro, ndipo akupita ku Igupto. Mafano a ku Igupto akunjenjemera pamaso pake, ndipo mitima ya Aigupto yachokamo ndi mantha.
2 Et les Égyptiens s'élèveront contre les Égyptiens, et le frère combattra le frère, ami contre ami, ville contre ville, nom contre nom.
“Ine ndidzadzutsa Aigupto kuti amenyane okhaokha; mʼbale adzamenyana ndi mʼbale wake, mnansi ndi mnansi wake, mzinda ndi mzinda unzake, ndiponso ufumu ndi ufumu unzake.
3 Et l'esprit des Égyptiens sera troublé en eux-mêmes, et je dissiperai leurs conseils; et ils interrogeront leurs dieux, et leurs statues, et ceux qui font sortir leurs voix de la terre, et les magiciens.
Aigupto adzataya mtima popeza ndidzalepheretsa zolinga zawo; adzapempha nzeru kwa mafano awo ndiponso kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa, kwa amawula ndi kwa oyankhula ndi mizimu.
4 Et je livrerai l'Égypte aux mains de maîtres cruels, et des rois cruels y règneront: voilà ce que dit le Seigneur Dieu des armées.
Ndidzawapereka Aigupto kwa olamulira ankhanza, ndipo mfumu yoopsa idzawalamulira,” akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
5 Et les Égyptiens boiront de l'eau près de la mer; car leur fleuve tarira, et il sera desséché.
Madzi a mu mtsinje wa Nailo adzaphwa, ndipo mʼmbali mwa mtsinje mudzangʼaluka ndi kuwuma.
6 Et les fleuves tariront et les canaux du fleuve; et tout amas d'eau sera desséché, et tous les marais où croissent le roseau et le papyrus;
Ngalande zake zidzanunkha; ndipo mitsinje ya Igupto idzayamba kuchepa ndi kuwuma. Bango ndi dulu zidzafota,
7 Et le gazon verdoyant au bord du fleuve; et tout ce qui est semé le long du fleuve sera flétri et desséché par le vent.
ndiponso zomera za mʼmphepete mwa Nailo ndi ku mathiriro a mtsinjewo. Zonse zodzalidwa mʼmbali mwa Nailo zidzawuma, zidzawuluzika ndipo sizidzaonekanso.
8 Et les pêcheurs gémiront; et ils gémiront tous ceux qui jettent l'hameçon dans le fleuve; et ceux qui jettent des seines et des filets pleureront.
Asodzi adzabuwula ndi kudandaula, onse amene amaponya mbedza mu Nailo; onse amene amaponya makoka mʼmadzi adzalira.
9 Et ceux qui travaillent le lin et le byssus, ou qui font des robes, seront confondus.
Amene amagwira ntchito yopota thonje adzataya mtima, anthu oluka nsalu zofewa zabafuta adzataya chiyembekezo.
10 Et tous les artisans seront dans la douleur, et ceux Qui font la bière seront attristés, et ils souffriront en leur âme
Akatswiri opanga nsalu adzangoti kakasi, ndipo anthu onse ogwira ntchito yolipidwa adzatheratu mphamvu.
11 Et les princes de Tanis, sages conseillers du roi, deviendront fous; leur conseil sera folie. Comment pourrez-vous dire au roi: Nous sommes les fils des sages, les fils des anciens rois?
Akuluakulu a ku Zowani ndi zitsiru; aphungu a nzeru a Farao amalangiza zopusa. Kodi mungathe kunena bwanji kwa Farao kuti, “Ine ndine mmodzi mwa anthu anzeru, wophunzira wa mafumu akale?”
12 Où sont maintenant tes sages? Qu'ils prophétisent, et qu'ils disent: Qu'a résolu contre l'Égypte le Seigneur Dieu des armées?
Iwe Farao, anthu ako anzeru ali kuti? Abweretu kuti akuwuze ndi kukudziwitsa zimene Yehova Wamphamvuzonse wakonza kuchitira dziko la Igupto.
13 Les princes de Tanis ont défailli; ceux de Memphis se sont enorgueillis, et ils ont égaré l'Égypte en toutes ses tribus.
Akuluakulu a ku Zowani asanduka zitsiru, atsogoleri a ku Mefisi anamizidwa; atsogoleri a dziko la Igupto asocheretsa anthu a dzikolo.
14 Car le Seigneur a répandu sur eux un esprit d'erreur, et ils ont égaré l'Égypte en toutes ses œuvres, et ils l'ont fait marcher comme un homme ivre qui vomit.
Yehova wasocheretsa anthu a ku Igupto. Iwo akuchita kudzandira pa zonse zimene akuchita, ngati chidakwa choterereka pa masanzi ake.
15 Et les Égyptiens ne feront plus rien qui ait une tête et une queue, un commencement et une fin.
Palibe chimene munthu wa mu Igupto angachite, mtsogoleri kapena wotsatira, nthambi ya kanjedza kapena bango.
16 Et, en ce jour, les Égyptiens seront comme des femmes effrayées et tremblantes sous la main du Seigneur des armées, qu'il fera tomber sur eux.
Tsiku limenelo Aigupto adzakhala ngati amayi. Adzanjenjemera ndi kuchita mantha akadzaona Yehova Wamphamvuzonse, atakweza dzanja lake kufuna kuwalanga.
17 Et la terre de la Judée sera pour les Égyptiens un objet de terreur; et quiconque prononcera son nom devant eux les frappera de crainte, à cause des desseins que le Seigneur des armées a formés sur eux-mêmes.
Ndipo dziko la Yuda lidzaopsa dziko la Aigupto. Aliyense amene adzamve dzina la Yuda adzaopsedwa chifukwa cha zimene Yehova Wamphamvuzonse wakonzekera kuchitira dziko la Igupto.
18 Ce jour-là, il y aura cinq villes d'Égypte qui parleront la langue de Chanaan, et jureront par le Seigneur Dieu des armées. L'une de ces villes s'appellera Asédec.
Tsiku limenelo ku dziko la Igupto kudzakhala mizinda isanu yoyankhula chiyankhulo cha Akanaani, ndipo anthu ake adzalumbira kwa Yehova Wamphamvuzonse kuti adzamutumikira. Umodzi mwa mizindayo udzatchedwa Mzinda Wachilungamo.
19 Ce jour-là, il y aura sur le territoire d'Égypte un autel du Seigneur, et à sa frontière une colonne élevée au Seigneur.
Tsiku limenelo mʼkati mwa dziko la Igupto mudzakhala guwa lansembe la Yehova, ndipo mʼmalire mwake adzayikira Yehova mwala wachikumbutso.
20 Et ce sera un signe éternel au Seigneur en la terre d'Égypte. Dès lors ils crieront au Seigneur dans leurs tribulations, et il leur enverra un homme pour les sauver; et il les sauvera en les jugeant.
Zimenezo zidzakhala umboni wozindikiritsa kuti Yehova Wamphamvuzonse alimo mʼdziko la Igupto. Pamene Aigupto adzalirira Yehova chifukwa cha owapondereza, Iye adzawatumizira mpulumutsi ndi mtetezi ndipo adzawalanditsa.
21 Et le Seigneur sera connu des Égyptiens. Et les Égyptiens en ce jour connaîtront le Seigneur, et ils lui sacrifieront des victimes, et ils lui feront des vœux, et ils les accompliront.
Kotero Yehova adzadziulula yekha kwa Aigupto, ndipo tsiku limenelo adzadziwa Yehova. Adzapembedza Yehova popereka nsembe ndi popereka zopereka zachakudya; Adzalumbira kwa Yehova ndipo adzachita zimene alumbirazo.
22 Et le Seigneur frappera d'une plaie les Égyptiens, puis il la guérira; et ils se convertiront au Seigneur, et il les exaucera, et il leur enverra une entière guérison.
Yehova adzakantha Aigupto ndi mliri. Iye adzawakanthadi ndipo kenaka adzawachiritsa. Aigupto adzatembenukira kwa Yehova ndipo Iye adzamva madandawulo awo ndi kuwachiritsa.
23 En ce jour, il y aura une voie de l'Égypte à l'Assyrie; et les Assyriens entreront en Égypte; et les Égyptiens iront en Assyrie, et ils seront asservis aux Assyriens.
Tsiku limenelo kudzakhala msewu waukulu wochoka ku Igupto kupita ku Asiriya. Aasiriya adzapita ku Igupto ndi Aigupto ku Asiriya. Aigupto ndi Aasiriya adzapembedza pamodzi.
24 En ce jour, Israël sera la troisième avec les Égyptiens et les Assyriens, et il sera béni sur la terre
Tsiku limenelo Israeli adzakhala pamodzi ndi Igupto ndi Asiriya, mayiko atatuwa adzakhala dalitso pa dziko lapansi.
25 Que le Seigneur des armées a bénie, disant: Béni soit mon peuple qui est en Égypte et qui est en Assyrie; et béni soit Israël mon héritage!
Yehova Wamphamvuzonse adzawadalitsa, ndi mawu awa, “Adalitsike anthu anga Aigupto, Aasiriya, ntchito ya manja anga, ndi Aisraeli osankhidwa anga.”

< Isaïe 19 >