< Aggée 1 >

1 En la sixième année du règne de Darius, le sixième mois, le premier jour du mois, la parole du Seigneur vint à Aggée, le prophète, disant: Parle à Zorobabel, fils de Salathiel, de la tribu de Juda, et à Jésus, fils de Josédec, le grand prêtre, et dis:
Chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo, tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chimodzi, Yehova anapatsa mneneri Hagai uthenga wopita kwa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, ndiponso kwa mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki:
2 Voici ce que dit le Seigneur Tout-Puissant. Ils disent que le temps n'est pas venu de réédifier la maison du Seigneur.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu awa amanena kuti, ‘Nthawi sinafike yoti nʼkumanga Nyumba ya Yehova.’”
3 Or la parole du Seigneur est venue à Aggée, le prophète, disant:
Tsono Yehova anayankhula ndi mneneri Hagai kuti,
4 Le temps est-il venu pour vous de demeurer en vos maisons lambrissées en voûte, quand Notre temple est désert?
“Kodi ino ndi nthawi yoti inuyo muzikhala mʼnyumba zomanga bwino, pamene Nyumba yangayi ikanali bwinja?”
5 Et maintenant, voici ce que dit le Seigneur tout-puissant. Dirigez vos cœurs en vos voies.
Tsono zimene Yehova Wamphamvuzonse akunena ndi izi, “Ganizirani bwino njira zanu.
6 Vous avez semé beaucoup, et peu recueilli; vous avez mangé, mais pas à satiété; vous avez bu, mais point jusqu'à l'ivresse; vous vous êtes vêtus, et vous n'avez pas été réchauffés; et celui qui a thésaurisé ses salaires, les a déposés dans un sac troué.
Mwadzala zambiri, koma mwakolola zochepa. Mumadya, koma simukhuta. Mumamwa, koma ludzu lanu silitha. Mumavala, koma simumva kutentha. Mumalandira malipiro, koma ndalama zanu zimatha ngati mwaziyika mʼthumba lobowoka.”
7 Or voici ce que dit le Seigneur tout-puissant. Dirigez vos cœurs en vos voies;
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ganizirani bwino njira zanu.
8 montez sur la montagne; abattez des arbres, et réédifiez le temple; et Je M'y complairai, et Je serai glorifié, dit le Seigneur.
Pitani ku mapiri ndipo mukatenge matabwa oti mudzamangire Nyumba yanga, kuti ndikondwere nayo ndi kulandiramo ulemu,” akutero Yehova.
9 Vous avez convoité beaucoup, et peu vous est venu; et ce peu vous l'avez emporté en vos maisons, et d'un souffle Je l'en ai fait sortir; c'est pourquoi voici ce que dit le Seigneur tout-puissant: En punition de ce que Ma demeure est déserte, et que chacun de vous court à sa demeure,
“Mumayembekezera zambiri, koma taonani mwapeza pangʼono pokha. Zimene munazibweretsa ku nyumba, Ine ndinazimwaza. Nʼchifukwa chiyani?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Chifukwa Nyumba yanga ikanali bwinja, pamene aliyense wa inu watanganidwa kumanga nyumba yake.
10 le ciel vous refusera sa rosée, et la terre vous retirera ses fruits.
Choncho, chifukwa cha inu, mitambo yaleka kugwetsa mvula ndipo dziko lapansi laleka kutulutsa zomera.
11 Et Je ferai passer un glaive sur la terre et sur les montagnes, sur le blé et sur le vin, sur l'huile et sur les fruits de la terre, sur les hommes, leur bétail et tous les travaux de leurs mains.
Ndabweretsa chilala pa minda ndi pa mapiri, chilala chawumitsa tirigu, mphesa, mafuta a olivi ndi chilichonse chimene chimamera pa nthaka, pa anthu ndi pa ngʼombe, ndi pa ntchito zonse za manja anu.”
12 Et Zorobabel, fils de Salathiel, de la tribu de Juda, et Jésus, fils de Josédec, le grand prêtre, et tout le reste du peuple entendirent la voix du Seigneur leur Dieu, et les paroles d'Aggée, le prophète, telles que par lui le Seigneur, leur Dieu, les leur avait envoyées. Et le peuple révéra la face du Seigneur.
Pamenepo Zerubabeli mwana wa Sealatieli, mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki, ndi anthu onse otsala anamvera mawu a Yehova Mulungu wawo ndi uthenga wa Hagai, chifukwa anatumidwa ndi Yehova Mulungu wawo. Ndipo anthuwo anaopa Yehova.
13 Et Aggée, le messager du Seigneur, rapporta au peuple le message du Seigneur, disant: Je suis avec vous, dit le Seigneur.
Tsono Hagai, mthenga wa Yehova, anapereka kwa anthuwo uthenga uwu wa Yehova: “Ine ndili nanu,” akutero Yehova.
14 Et le Seigneur suscita l'esprit de Zorobabel, fils de Salathiel, de la tribu de Juda, et l'esprit de Jésus, fils de Josédec, le grand prêtre, et l'esprit du reste du peuple; et ils entrèrent dans le temple du Seigneur, leur Dieu tout-puissant, et ils y firent des travaux.
Kotero Yehova anakhudza mtima wa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, mtima wa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndiponso mitima ya anthu onse otsala. Iwo anabwera ndi kuyamba ntchito yomanga Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wawo,
15 Le vingt-quatrième jour du sixième mois, la seconde année du règne de Darius;
pa tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chimodzi, wa chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo.

< Aggée 1 >