< Genèse 12 >

1 Le Seigneur dit alors à Abram: Sors de ta terre, de ta famille, et de la maison de ton père, pour te rendre en la terre que je te montrerai.
Tsiku lina Yehova anamuwuza Abramu kuti, “Tuluka mʼdziko lako. Siya abale ako ndi banja la abambo ako ndipo pita ku dziko limene ndidzakusonyeza.
2 Je ferai sortir de toi un grand peuple; je te bénirai, je glorifierai ton nom, et il sera béni.
“Ndidzakusandutsa kholo la mtundu waukulu wa anthu ndipo ndidzakudalitsa; ndi kukusandutsa wotchuka kotero kuti udzakhala dalitso kwa anthu ambiri.
3 Je bénirai ceux qui te béniront; ceux qui je maudiront, je les maudirai, et en toi seront bénies toutes les tribus de la terre.
Ndidzadalitsa amene adzadalitsa iwe, ndi kutemberera amene adzatemberera iwe; ndipo mafuko onse a pa dziko lapansi adzadalitsika kudzera mwa iwe.”
4 Et Abram s'en alla, comme avait dit le Seigneur, et Lot partit avec lui. Or, Abram avait soixante-quinze ans lorsqu'il sortit de Haran.
Choncho Abramu ananyamuka monga momwe Yehova anamuwuzira, napita pamodzi ndi Loti. Pamene Abramu amachoka ku Harani nʼkuti ali ndi zaka 75.
5 Abram prit donc Sara, sa femme, Lot, fils de son frère, tout ce qui leur appartenait, tout ce qu'ils avaient acquis, toutes les âmes qu'ils avaient acquises dans Haran; et ils partirent pour passer en la terre de Chanaan.
Abramu anatenga mkazi wake Sarai, Loti, mwana wamngʼono wake, pamodzi ndi chuma chawo chimene anapeza ndi antchito amene anali nawo ku Harani. Iwo ananyamuka ulendo mpaka kukafika ku dziko la Kanaani.
6 Abram traversa cette terre dans toute sa longueur jusqu'au territoire de Sichem, vers le grand chêne. Or, les Chananéens habitaient alors cette terre.
Abramu anadutsa mʼdzikomo mpaka kukafika ku Sekemu pa mtengo wa thundu wa ku More. Nthawi imeneyo Akanaani analipobe mʼdzikomo.
7 Et le Seigneur apparut à Abram, et il lui dit: À ta face je donnerai cette terre; c'est pourquoi Abram bâtit là un autel au Seigneur qui lui était apparu.
Yehova anadza kwa Abramu nati, “Kwa zidzukulu zako ndidzapereka dziko limeneli.” Choncho Abramu anamangira Yehova amene anadza kwa iye, guwa lansembe.
8 Et il alla de ce lieu vers la montagne, à l'orient de Béthel, il y dressa ses tentes, ayant Béthel à l'occident, et Angaï à l'orient; puis il éleva là un autel au Seigneur, et il invoqua le nom du Seigneur.
Atachoka pamenepo analowera cha ku mapiri a kummawa kwa Beteli namangako tenti yake pakati pa Beteli chakumadzulo ndi Ai chakummawa. Kumeneko anamangira Yehova guwa lansembe napemphera mʼdzina la Yehovayo.
9 Ensuite Abram partit, et, ayant marché, il campa dans le désert.
Kenaka Abramu ananyamuka kumalowera cha ku Negevi.
10 Il y eut alors une famine en la contrée, et Abram descendit en Égypte pour y séjourner, parce que la famine avait prévalu dans le pays.
Kunagwa njala yayikulu mʼdzikomo, ndipo Abramu anapita ku Igupto kukakhala ngati mlendo kwa kanthawi kochepa popeza njalayo inakula kwambiri.
11 Or, il arriva qu'Abram, près d'entrer en Égypte, dit à Sara, sa femme: Je sais que tu es une femme très belle;
Atatsala pangʼono kulowa mu Igupto, Abramu anamuwuza mkazi wake Sarai kuti, “Ndimadziwa kuti ndiwe mkazi wokongola kwambiri.
12 Il adviendra donc, quand les Égyptiens t'auront vue, qu'ils diront: C'est sa femme; alors ils me tueront, et ils s'empareront de toi.
Tsono Aigupto akakuona adzanena kuti ‘Ameneyu ndi mkazi wake.’ Tsono adzandipha ine nakusiya iwe ndi moyo.
13 Dis donc: Je suis sa sœur, afin qu'à cause de toi je sois mieux traité, et qu'en ta considération j'aie la vie sauve.
Tsono udzikawawuza kuti iwe ndiwe mlongo wanga. Ukatero zidzandiyendera bwino ndipo ndidzapulumuka chifukwa cha iwe.”
14 Et lorsque Abram fut entré en Égypte, les Égyptiens virent que sa femme était très belle.
Pamene Abramu anafika ku Igupto, Aigupto aja anaona kuti Sarai anali mkazi wokongoladi.
15 Les officiers du Pharaon la virent aussi; ils la vantèrent devant le Pharaon, et ils la conduisirent en sa demeure.
Pamene akuluakulu a ku nyumba ya Farao anamuona, anakamuyamikira pamaso pa Farao ndipo ananka naye ku nyumba ya Farao.
16 À cause d'elle, ils traitèrent bien Abram, et il eut des brebis, des bœufs, des ânes, des serviteurs, des servantes, des mulets et des chameaux.
Abramu naye zinthu zinkamuyendera bwino chifukwa cha Sarai. Farao anamupatsa nkhosa, ngʼombe, abulu aamuna ndi abulu aakazi, antchito aakazi pamodzi ndi ngamira.
17 Mais Dieu envoya au Pharaon et à sa famille de grandes et cruelles afflictions, à cause de Sara, femme d'Abram.
Koma Yehova anabweretsa matenda owopsa pa Farao pamodzi ndi banja lake lonse chifukwa cha Sarai mkazi wa Abramu.
18 Et le Pharaon ayant appelé Abram, lui dit: Pourquoi as-tu fait cela, et ne m'as-tu pas dit: C'est ma femme?
Choncho Farao anayitanitsa Abramu namufunsa kuti, “Nʼchiyani wandichitirachi? Nʼchifukwa chiyani sunandiwuze kuti ameneyu ndi mkazi wako?
19 Pourquoi as-tu dit: C'est ma sœur? Alors je l'ai prise pour qu'elle fût ma femme; or, maintenant voici ta femme devant toi; reprends-la, et pars aussitôt.
Nʼchifukwa chiyani unati ndi mlongo wako, mpaka ine ndinamutenga kukhala mkazi wanga? Eko mkazi wako. Mutenge uzipita!”
20 Le Pharaon prescrivit à des hommes d'escorter Abram, sa femme, et tout ce qui lui appartenait.
Farao analamula asilikali ake ndipo iwo anamutulutsa Abramu pamodzi ndi mkazi wake ndi zonse anali nazo.

< Genèse 12 >