< Genèse 10 >

1 Voici les générations des fils de Noé: Sem, Cham et Japhet; des fils leur naquirent après le déluge.
Nayi mbiri ya ana a Nowa, Semu, Hamu ndi Yafeti. Ana atatuwa anabereka ana awo chitatha chigumula.
2 Fils de Japhet: Gomer, Magog, Madaï, Javan, Elisa, Thubal, Mosoch et Thiras.
Ana aamuna a Yafeti anali: Gomeri, Magogi, Madai, Yavani, Tubala, Mesaki ndi Tirasi.
3 Fils de Gomer: Ascenez, Riphat, et Thogorma.
Ana aamuna a Gomeri anali: Asikenazi, Rifati ndi Togarima.
4 Fils de Javan: Elisa, Tharsis, Cettim et Dodanim.
Ana aamuna a Yavani anali: Elisa, Tarisisi, Kitimu ndi Rodanimu.
5 Ceux-ci sont les pères des gentils, qui se partagèrent les îles et les eurent pour territoire, chacun selon sa langue, par tribus, par nations.
(Amenewa ndiwo makolo a anthu okhala mʼmphepete mwa nyanja. Awa ndi ana a Yafeti monga mwa mafuko a mu mitundu yawo, uliwonse ndi chiyankhulo chake).
6 Fils de Cham: Chus, Mesraïm, Phuth et Chanaan.
Ana aamuna a Hamu anali: Kusi, Miziraimu, Puti ndi Kanaani.
7 Fils de Chus: Saba, Hevila, Sabatha, Regma et Sabathaca. Fils de Regma: Saba et Dadan.
Ana aamuna a Kusi anali: Seba, Havila, Sabita, Raama ndi Sabiteka. Ana aamuna a Raama anali: Seba ndi Dedani.
8 Et Chus engendra Nemrod: celui-ci commença à être puissant sur la terre.
Kusi anabereka Nimurodi amene anali wankhondo wamphamvu kwambiri pa dziko lapansi.
9 Il était grand chasseur devant le Seigneur; c'est pourquoi l'on dit: Grand chasseur comme Nemrod devant le Seigneur.
Iye anali mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova; nʼchifukwa chake anthu ali ndi chisudzo, chakuti, “Ndiwe mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova monga Nimurodi.”
10 Le commencement de son royaume fut Babylone, puis il eut Arach, Archad, Chalané, et la terre de Sennaar.
Malo oyambirira a ufumu wake anali Babeli, Ereki, Akadi ndi Kaline. Malo onsewa anali mʼdziko la Sinara.
11 De cette terre sortit Assur, qui bâtit Ninive, et la ville de Rhooboth et Chalé,
Atachoka mʼdziko limeneli anapita ku Asiriya kumene anakamanga Ninive, Rehoboti-Iri, Kala,
12 Et Ressen, grande ville, entre Ninive et Chalé.
ndi Reseni, mzinda waukulu umene uli pakati pa Ninive ndi Kala.
13 Mesraïm engendra les Ludim, les Ananim, les Laabim, les Nephtuïm,
Igupto ndiye kholo la Aludi, Aanami, Alehabu, Anafutu,
14 Les Phétrusim, les Chasluïm (d'où est sorti Philistin) et les Caphtorins.
Apaturusi, Akasilu ndi Akafitori (kumene kunachokera Afilisti).
15 Chanaan engendra Sidon son premier-né, puis le Hétéen,
Kanaani anabereka mwana wake wachisamba, Sidoni, ndipo anaberekanso Ahiti;
16 Le Jebuséen, l'Amorrhéen, le Gergéséen,
Ayebusi, Aamori, Agirigasi;
17 L'Evéen, l'Arucéen, l'Asennéen,
Ahivi, Aariki, Asini,
18 L'Aradien, le Samaréen et l'Amathéen. Après cela, les tribus des Chananéens se dispersèrent.
Aaravadi, Azemari ndi Ahamati. Pambuyo pake, mafuko a Akanaani anafalikira ponseponse,
19 Les limites des Chananéens étaient la côte depuis Sidon jusqu'à Gérara et Gaza; puis elles s'étendirent jusqu'à Sodome et Gomorrhe, et passèrent par Adama et Séboïm jusqu'à Léba.
mpaka ku malire a Kanaani. Malirewo anachokera ku Sidoni kulowa cha ku Gerari mpaka ku Gaza, ndi kulowa ku Sodomu, Gomora, Adima ndi Zeboimu mpaka ku Lasa.
20 Tels furent les fils de Cham et leurs tribus, selon leurs langues, par contrées, et par nations.
Amenewa ndiwo ana aamuna a Hamu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe amakhala ndi mitundu yawo.
21 Sem fut père aussi, et eut Héber de l'un de ses fils, frère de Japhet le plus grand.
Semu amene anali mkulu wake wa Yafeti nayenso anabereka nakhala kholo la Eberi.
22 Fils de Sem: Elam, Assur, Arphaxad, Lud, Aran et Caïnan.
Ana aamuna a Semu anali: Elamu, Asuri, Aripakisadi, Ludi ndi Aramu.
23 Fils d'Aram: Hus, Hul, Gether et Mosoch.
Ana aamuna a Aramu anali: Uzi, Huri, Geteri ndi Mesaki.
24 Arphaxad engendra Salé, et Salé engendra Héber.
Aripakisadi anabereka Sela, ndipo Selayo anabereka Eberi.
25 D'Héber naquirent deux fils, nommés, l'un Phaleg, parce que de son temps la terre fut partagée, et l'autre Jectan.
A Eberi anabereka ana aamuna awiri: Wina anamutcha Pelegi chifukwa pa nthawiyo anthu a pa dziko lapansi anagawikana. Dzina la mʼbale wake linali Yokitani.
26 Or, Jectan engendra Elmodad, Saleph, Asarmoth Jaré,
Yokitani anabereka Alimodadi, Selefi, Hazari-Maveti, Yera,
27 Aduram, Uzal, Décla,
Hadoramu, Uzali, Dikila,
28 Abimaël, Saba,
Obali, Abimaeli, Seba,
29 Ophir, Hévila et Jobab: tels furent les fils de Jectan.
Ofiri, Havila ndi Yobabu. Onsewa anali ana aamuna a Yokitani.
30 Ils habitèrent depuis Messa jusqu'à Séphar, montagne de l'Orient.
Chigawo chimene ankakhala chinayambira ku Mesa mpaka ku Seferi, ku dera la mapiri chakummawa.
31 Tels furent les fils de Sem et leurs tribus, selon leurs langues, par contrées et par nations.
Amenewa ndiwo ana a Semu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe ankakhala ndi mitundu yawo.
32 Telles furent les tribus des fils de Noé, par familles et nations; et c'est ainsi que les fils de Noé peuplèrent les pays des nations, sur la terre, après le déluge.
Amenewa ndiwo mafuko a ana aamuna a Nowa monga mwa mibado ya mitundu yawo. Mitundu yonse ya anthu inatuluka mwa iwowa ndi kufalikira pa dziko lonse lapansi chitatha chigumula chija.

< Genèse 10 >