< Esdras 8 >

1 Et voici les noms des chefs de familles, qui sont venus avec moi sous le règne d'Arthasastha, roi de Babylone
Nawa mayina a atsogoleri a mabanja amene anabwera nane kuchokera ku Babuloni nthawi ya ulamuliro wa mfumu Aritasasita:
2 Des fils de Phinéès, Gerson; des fils d'Ithamar, Daniel; des fils de David, Attus.
Geresomu wa fuko la Finehasi; Danieli wa fuko la Itamara; Hatusi
3 Des fils de Sachanie et des fils de Phoros, Zacharie, et avec lui ses compagnons, cent cinquante hommes.
mwana wa Sekaniya wa fuko la Davide; Zekariya wa fuko la Parosi. Pamodzi ndi iyeyu panalembedwa anthu ena 150;
4 Des fils de Phaath-Moab, Eliana, fils de Saraïa, et avec lui deux cents hommes.
Elihunai mwana wa Zerahiya, wa fuko la Pahati-Mowabu. Pamodzi ndi iyeyu panalinso anthu ena 400.
5 Et des fils de Zathoé, Sechénias, fils d'Aziel, et avec lui trois cents hommes.
Sekaniya, mwana wa Yahazieli wa fuko la Zatu. Pamodzi ndi iyeyu panalembedwanso anthu 300.
6 Et des fils d'Adin, Obed, fils de Jonathas, et avec lui cinquante hommes.
Ebedi, mwana wa Yonatani wa fuko la Adini. Pamodzi naye analembedwanso anthu ena makumi asanu.
7 Et des fils d'Elam, Isaïe, fils d'Athélie, et avec lui soixante-dix hommes.
Yesaiya, mwana wa Ataliya wa fuko la Elamu. Pamodzi naye panali anthu ena 70.
8 Et des fils de Saphatie, Zabadie, fils de Michel, et avec lui quatre-vingts mâles.
Zebadiya, mwana wa Mikayeli wa fuko la Sefatiya. Pamodzi naye panalinso anthu 80.
9 Et des fils de Joab, Abadie, fils de Jehiel, et avec lui deux cent dix-huit hommes.
Obadiya, mwana wa Yehieli wa fuko la Yowabu. Pamodzi naye panalinso anthu 218.
10 Et des fils de Baani, Selimuth, fils de Joséphie, et avec lui cent soixante hommes.
Selomiti mwana wa Yosifiya wa fuko la Bani. Pamodzi ndi iyeyu panalinso anthu 160.
11 Et des fils de Babi, Zacharie, fils de Babi, et avec lui vingt-huit mâles.
Zekariya, mwana wa Bebai wa fuko la Babai. Pamodzi naye analembedwanso anthu 28.
12 Et des fils d'Asgad, Johanan, fils d'Accatan, et avec lui cent dix mâles.
Yohanani, mwana wa Hakatani wa fuko la Azigadi. Pamodzi naye panalinso anthu 110.
13 Et des fils d'Adonicam, les derniers, et voici leurs noms: Eliphalat, Jehel et Samaia, et avec eux soixante mâles.
Atsogoleri a fuko la Adonikamu, anthu amene anabwera pambuyo pake mayina awo anali Elifeleti, Yeiyeli ndi Semaya. Pamodzi ndi iwowa panalinso anthu 60.
14 Et des fils de Baguai, Uthaï et Zabud, et avec eux soixante-dix mâles.
Atsogoleri a fuko la Bigivai anali Utai ndi Zakuri. Pamodzi ndi iwowa panali anthu 70.
15 Je les réunis vers le fleuve qui se rend à Evi, et nous y restâmes campés trois jours; et je m'informai du peuple et des prêtres, et je ne trouvai là pas un fils de Lévi.
Anthu onse ndinawasonkhanitsa ku mtsinje umene umapita mpaka ku Ahava, ndipo kumeneko tinagona mʼmisasa masiku atatu. Nditayangʼana pakati pa anthu ndi ansembe, ndinapeza kuti panalibe Alevi.
16 Ensuite, je donnai mes ordres à Eléazar, à Ariel, à Sémeïas et à Alonam, à Jarib, à Elnatham, à Nathan, à Zacharie, à Mesollam, à Joarim et à Elthanan, hommes doués de sagesse.
Choncho ndinayitana atsogoleri awa: Eliezara, Arieli, Semaiya, Elinatani, Yaribu, Elinatani, Natani, Zekariya ndi Mesulamu, pamodzi ndi aphunzitsi awiri, Yoyaribu ndi Elinatani,
17 Et je les envoyai aux chefs, avec l'argent recueilli dans la contrée, et je leur mis sur les lèvres les paroles qu'ils avaient à dire à leurs frères les Athinéens, en leur remettant l'argent recueilli dans la contrée, afin qu'ils nous amenassent des chantres pour le temple de notre Dieu.
ndipo ndinawatuma kwa Ido, mtsogoleri wa malo otchedwa Kasifiya. Ine ndinawawuza zoti akanene kwa Ido ndi kwa abale ake, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu ku Kasifiyako, kuti atitumizire anthu odzatumikira ku Nyumba ya Mulungu.
18 Et comme la main de Dieu nous était favorable, ils nous amenèrent un homme: Sachon, des fils de Mooli, fils de Lévi, fils d'Israël, et d'abord arrivèrent ses fils et ses frères, en tout dix-huit;
Chifukwa cha kutikomera mtima kwa Mulungu wathu, Ido anatitumizira munthu wanzeru, Serabiya, wa fuko la Mahili, mwana wa Levi, mwana wa Israeli, pamodzi ndi ana ake aamuna ndi abale ake, anthu 18.
19 Ils nous amenèrent aussi Asebie et Isaïe, des fils de Mérari, et ses frères et ses fils, vingt personnes.
Anatitumiziranso Hasabiya ndi Yesaiya wa fuko la Merari pamodzi ndi abale ake ndi adzukulu ake, anthu makumi awiri.
20 Et des Nathinéens que David et les chefs avaient donnés pour serviteurs aux lévites, deux cent vingt, tous désignés par leurs noms.
Panalinso anthu ena 220 mwa anthu ogwira ntchito mʼNyumba ya Mulungu amene Davide ndi nduna zake anawasankha kuti azitumikira Alevi. Anthu onsewa analembedwa potsata mayina awo.
21 Et là, sur le fleuve Ahua je proclamai un jeûne, pour nous humilier devant notre Dieu, et chercher par lui le droit chemin, pour nous et nos enfants, et tout notre bétail.
Ku mtsinje wa Ahava, ndinalengeza kuti anthu onse asale zakudya, adzichepetse pamaso pa Mulungu wathu ndi kupempha kuti atiyendetse bwino ife ndi ana athu, ndi kuteteza katundu wathu yense.
22 En effet, j'aurais eu honte de demander au roi des troupes et de la cavalerie, pour nous protéger en route contre tout ennemi, car nous avions dit au roi: La main de notre Dieu est sur tous ceux qui le cherchent pour le bien; mais sa puissance et sa colère sont sur tous ceux qui l'abandonnent.
Ine ndinali ndi manyazi kupempha mfumu kuti atipatse asilikali oyenda pansi ndi ena okwera pa akavalo kuti atiteteze kwa adani athu pa ulendo wathuwu popeza tinali titawuza kale mfumu kuti “Yehova amateteza aliyense amene amamudalira, koma amakwiyira onse amene amamukana.”
23 Et nous jeûnâmes, nous fîmes à ce sujet notre prière au Seigneur, et il nous exauça.
Choncho tinasala zakudya ndi kupemphera kwa Mulungu wathu kuti atiteteze ndipo Iye anamva pemphero lathu.
24 Et je donnai mes ordres à douze des chefs des prêtres: à Sardias, Asabie, et dix de leurs frères.
Tsono ndinasankha atsogoleri a ansembe khumi ndi awiri awa, Serebiya, Hasabiya ndi abale awo khumi
25 Et je pesai pour eux l'argent, l'or et les vases des prémices consacrées dans le temple de notre Dieu, que le roi, ses conseillers, ses princes, et tous ceux d'Israël, qu'on avait trouvés, avaient offerts,
ndipo ndinawayezera siliva ndi golide, ndiponso ziwiya ndi zopereka za ku Nyumba ya Mulungu wathu zimene mfumu ndi alangizi ake, nduna zake ndi Aisraeli onse amene anali kumeneko anazipereka.
26 Je pesai ainsi entre leurs mains six cent cinquante talents d'argent, cent vases d'argent et cent talents d'or;
Nditayeza zonse, ndinapereka mʼmanja mwawo, matani 22 asiliva, ziwiya zasiliva zolemera makilogalamu 70, ndiponso makilogalamu 3,400 a golide,
27 Et vingt tasses d'or du poids d'environ mille drachmes, et des vases de grand prix, en bel airain brillant, aussi précieux que s'ils eussent été d'or.
mbale zagolide makumi awiri zolemera makilogalamu asanu ndi atatu ndi theka ndiponso ziwiya ziwiri zamkuwa wosalala, wonyezimira bwino ngati golide wamtengowapatali.
28 Puis, je leur dis: Vous êtes saints aux yeux du Seigneur; les vases sont saints, l'argent et l'or ont été volontairement donnés pour le Seigneur Dieu de nos pères.
Kenaka ndinawawuza kuti, “Inu ndi opatulika a Yehova, ndiponso mphatso zonsezi ndi zopatulika. Siliva ndi golideyu ndi zopereka zaufulu kwa Yehova, Mulungu wa makolo anu.
29 Veillez sur eux et gardez-les jusqu'à ce que vous les pesiez devant les princes des prêtres, devant les lévites et devant les chefs de familles de Jérusalem, dans le tabernacle du temple du Seigneur.
Muzisamale bwino mpaka mutaziyeza pamaso pa atsogoleri a ansembe ndi Alevi ndi akulu a mabanja a Israeli mʼzipinda za mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu.”
30 Cet or et cet argent pesés de cette manière, les prêtres et les lévites les reçurent pour les porter à Jérusalem, dans le temple du Seigneur notre Dieu.
Choncho ansembe ndi Alevi analandira zonse zoyezedwa zija, siliva, golide pamodzi ndi ziwiya kuti apite nazo ku Nyumba ya Yehova ku Yerusalemu.
31 Alors, je levai mon camp du fleuve Ahua, le douzième jour du premier mois, pour aller à Jérusalem. Et la main du Seigneur notre Dieu était sur nous, et il nous préserva en route de tout ennemi, de toute attaque ou de toute hostilité.
Pa tsiku la khumi ndi chiwiri la mwezi woyamba, tinachoka ku mtsinje wa Ahava kupita ku Yerusalemu. Ndipo Mulungu wathu anali nafe, ndipo anatiteteza kwa adani athu makamaka otibisalira pa njira.
32 Nous arrivâmes à Jérusalem, et nous y demeurâmes trois jours.
Tinafika ku Yerusalemu, komwe tinapumula masiku atatu.
33 Le quatrième jour, nous pesâmes l'argent, l'or et les vases, dans le temple du Seigneur, entre les mains de Merimoth, fils d'Urie, le prêtre, en présence d'Eléazar, fils de Phinéès; il y avait avec eux les lévites Josabad, fils de Josué, et Noadia, fils de Banaïa.
Pa tsiku la chinayi lake, mʼNyumba ya Mulungu wathu, tinayeza siliva ndi golide ndi ziwiya zija nʼkuzipereka mʼmanja mwa Meremoti mwana wa wansembe Uriya. Pamodzi ndi iyeyo panali Eliezara mwana wa Finehasi ndiponso Alevi awa: Yozabadi mwana wa Yesuwa ndi Nowadiya mwana wa Binuyi.
34 On en fit le compte, on en prit le poids, et le poids total fut écrit. En ce temps-là,
Zonsezi anaziwerenga ndi kuziyeza ndipo analemba kulemera kwa chinthu chilichonse.
35 Les fils de l'exil revenus de la captivité offrirent en holocauste, au Dieu d'Israël, douze bœufs pour tout Israël, quatre-vingt-onze béliers, soixante-dix-sept agneaux, et douze boucs pour le péché; tout cela fut offert en holocauste au Seigneur.
Pamenepo anthu amene anatengedwa ukapolo aja anabwerera, anapereka nsembe zopsereza kwa Mulungu wa Israeli: ngʼombe zazimuna khumi ndi ziwiri, kuperekera Aisraeli onse, nkhosa zazimuna 96, ana ankhosa 77, ndiponso mbuzi zazimuna khumi ndi ziwiri ngati nsembe yopepesera machimo. Zonsezi zinali nsembe yopsereza zopereka kwa Yehova.
36 Et les édits du roi furent donnés à ses intendants et à ses gouverneurs, d'en deçà du fleuve, qui glorifièrent le peuple et le temple de Dieu.
Iwo anaperekanso chidziwitso cha mfumu chija kwa akuluakulu a mfumu ndi kwa akazembe a mʼdera la Patsidya pa Yufurate. Pamenepo iwo anathandiza Ayuda ndiponso ntchito za pa Nyumba ya Mulungu.

< Esdras 8 >