< Ézéchiel 5 >

1 Et toi, fils de l'homme, prends avec toi un glaive plus tranchant que le rasoir d'un barbier; achète-le pour toi, et passe-le sur ta tête et sur ton menton; tu prendras ensuite des poids et une balance; puis tu sépareras ta barbe et tes cheveux.
Tsiku lina Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tsopano tenga lupanga lakuthwa ndipo uligwiritse ntchito ngati lumo lometera. Umete tsitsi ndi ndevu zako. Kenaka utenge sikelo ndipo ugawe tsitsilo patatu.
2 Tu en brûleras dans le feu un quart, au milieu de la ville, pendant que s'accompliront les jours du siège; tu en prendras un autre quart pour le brûler dans son enceinte; puis, avec le glaive, tu couperas le troisième quart autour de ses murailles; enfin tu jetteras au vent le dernier quart, que je poursuivrai à coups d'épée nue.
Kuzinga mzinda kuja kukatha, chimodzi cha zigawo zitatu za tsitsilo uchitenthe pakati pa mzinda. Chigawo chachiwiri uchiduledule ndi lupanga, poyenda muzungulire mzinda wonsewo. Chigawo chachitatu uchimwazire ku mphepo, ndidzachitsata nditasolola lupanga.
3 Et tu prendras quelque peu de poils, et tu les attacheras au bord de ton manteau.
Koma utengeko tsitsi pangʼono, ulimange mu mpindiro wa mkanjo wako.
4 Et tu en prendras encore, et tu les jetteras au milieu du feu, et tu les brilleras dans le feu; il en sortira une flamme, et tu diras à toute la maison d'Israël:
Pa tsitsi limeneli utapepo lina, uliponye pa moto ndi kulitentha. Moto udzayambira pamenepo mpaka ku nyumba yonse ya Israeli.”
5 Voici ce que dit le Seigneur: C'est là Jérusalem; je l'ai placée, elle et son territoire, au milieu des nations.
Ambuye Yehova akunena kuti, “Uyu ndi Yerusalemu amene ndamuyika pakati pa mitundu ya anthu, ndipo mayiko onse amuzungulira.
6 Et tu diras mes ordonnances à cette ville coupable entre toutes les nations, et mes préceptes aux peuples de son territoire; car ils ont répudié mes ordonnances, et ils n'ont point marché selon mes voies;
Koma anthu a Yerusalemu aphwanya malamulo anga pochita zoyipa kuposa anthu a mitundu ina. Iwo anandipandukira kupambana anthu ena amene awazungulira. Iwo anakana malamulo anga ndipo sanasunge malangizo anga.
7 À cause de cela, voici ce que dit le Seigneur: En punition de ce que les nations qui vous entourent ont été pour vous une occasion de péché; de ce que vous n'avez point cheminé selon mes préceptes, que vous n'avez point exécuté mes lois, mais que vous avez suivi celles des nations qui vous entourent;
“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Popeza mwakhala osamvera kupambana anthu a mitundu ina amene akuzungulirani, popeza simunatsate malamulo anga kapena kusunga malangizo anga, mʼmalo mwake mwakhala mukutsata makhalidwe a anthu a mitundu ina amene akuzungulirani.
8 À cause de cela, ainsi parle le Seigneur: Voilà que je suis contre toi, et au milieu de toi j'exécuterai mon jugement devant les nations.
“Tsono Ambuye Yehova akuti: Ine mwini ndikutsutsana nawe, Yerusalemu, choncho Ine ndidzakulangani. Ine ndidzakulangani anthu a mitundu ina akuona.
9 Et je ferai en toi des choses que je n'ai jamais faites, et telles que je n'en ferai jamais de semblables pour punir toutes tes abominations.
Chifukwa cha ntchito zanu zonyansa ndidzakulangani ndi chilango chimene sindinakulangeni nacho nʼkale lomwe ndipo sindidzakulangani ndi chofanana nacho mʼtsogolomo.
10 À cause de cela, les pères mangeront leurs enfants au milieu de toi, et les enfants mangeront leurs pères; et j'exécuterai en toi mon jugement, et je disperserai tes restes à tous les vents.
Tsono pakati panu makolo adzadya ana awo, ndipo ana adzadya makolo awo. Ndidzakulanga ndipo otsala onse ndidzawabalalitsa ku mphepo zonse zinayi.
11 À cause de cela, par ma vie, dit le Seigneur, en punition de ce que par toutes tes abominations tu as souillé mes choses saintes, je te répudierai; et mon œil sera sans pitié, et moi je serai sans miséricorde.
Ndithu, pali Ine, akutero Ambuye Yehova Wamoyo, pakuti mwayipitsa Nyumba yanga ndi mafano ano oyipa ndi miyambo yanu yonyansa, Inenso ndidzakulangani. Sindidzakulekererani kapena kukumverani chisoni.
12 Le quart des tiens périra par la peste; le quart périra par la famine au milieu de toi; le quart sera jeté par moi à tous les vents; le quart périra autour de toi par le glaive; et je les poursuivrai à coups d'épée nue.
Chimodzi mwa zigawo zitatu za anthu ako chidzafa ndi mliri, kapena chidzawonongeka ndi njala; chigawo china chidzaphedwa ndi lupanga kunja kwa mzinda, ndipo chigawo china ndidzachibalalitsira ku mphepo zonse zinayi pochita kuchithamangitsa.
13 Et ma colère et ma fureur s'assouvira contre eux, et tu connaîtras que moi, le Seigneur, j'ai parlé dans ma jalousie, pendant que j'assouvissais ma colère contre eux.
“Ndi mmene udzachitire mkwiyo wanga. Ndikadzatsiriza kuwalanga, pamenepo mtima wanga udzakhala pansi. Adzadziwa kuti Ine Yehova ndinawayankhula mwa nsanje ndikadzawalanga.
14 Et à la vue de tous les passants, je ferai un désert de toi et de tes filles qui entourent ton enceinte.
“Ndidzakusandutsa iwe bwinja ndi chinthu chonyozeka pakati pa anthu a mitundu ina amene akuzungulira, ndi kwa onse odutsapo
15 Et tu seras gémissante et digne de pitié au milieu des nations qui t'entourent, pendant que j'exécuterai sur toi mon jugement en me vengeant de toi selon ma colère.
Udzakhala chinthu chonyozeka ndi chonyogodoledwa. Udzakhala chenjezo ndi chinthu choopsa kwa anthu a mitundu ina amene akuzungulira ndikadzakulanga mokwiya ndi mwaukali ndi kugamula mlandu wako mokwiya. Ine Yehova ndayankhula.
16 Moi, le Seigneur, j'ai parlé, et quand je lancerai contre eux les traits de la faim, ils seront en défaillance, et je briserai le soutien de leur pain;
Pamene ndidzakulasa ndi njala yolasa ngati mivi yoopsa ndi yosakaza ndidzatero nʼcholinga choti ndikuwonongeni. Ndidzagwetsa njalayo pa iwe mowirikiza pochepetsa chakudya chako cha tsiku ndi tsiku.
17 Et j'enverrai contre toi la famine et les bêtes farouches, et je me vengerai de toi, et la peste et le sang passeront sur toi, et je promènerai sur toi le glaive autour de ton enceinte. Moi, le Seigneur, j'ai parlé.
Ndidzatumiza njala ndi zirombo za kuthengo, ndipo zidzakulanda ana ako. Mliri ndi kuphana zidzakhala pakati pako, ndipo ndidzakubweretsera nkhondo. Ine Yehova ndayankhula.”

< Ézéchiel 5 >