< Ézéchiel 34 >

1 Et la parole du Seigneur me vint, disant:
Yehova anandiyankhula kuti:
2 Fils de l'homme, prophétise contre les pasteurs d'Israël; prophétise, et dis aux pasteurs: Voici ce que dit le Seigneur Maître: Malheur aux pasteurs d'Israël! Est-ce que les pasteurs se paissent eux-mêmes? Est-ce que les pasteurs ne doivent pas paître les brebis?
“Iwe mwana wa munthu, yankhula mawu oyimba mlandu abusa a Israeli. Lengeza ndipo uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Tsoka kwa abusa a Israeli amene mumangodzisamala nokha! Kodi abusa sayenera kusamalira nkhosa?
3 Voilà que vous mangez le laitage; vous vous faites des vêtements avec la laine; vous égorgez les bêtes les plus grasses; vous ne paissez point mes brebis.
Mumadya chambiko, mumadziveka zovala zaubweya, ndi kupha nyama zonenepa, koma simusamalira nkhosazo.
4 Vous n'avez point fortifié les faibles, vous n'avez point guéri les malades, vous n'avez point entouré de bandes les blessées, vous n'avez point ramené les égarées; vous n'avez point cherché ce qui était perdu; et ce qui était plein de force, vous l'avez accablé de labeurs.
Simunalimbitse nkhosa zofowoka, kapena kuchiritsa zodwala, kapena kumanga mabala a nkhosa zopweteka. Simunabweze zosochera kapena kufunafuna zotayika. Munaziweta mozunza ndi mwankhanza.
5 Aussi mes brebis ont été dispersées, parce qu'elles n'avaient pas de pasteurs; et elles ont été la pâture des bêtes fauves des champs.
Kotero zinabalalika chifukwa zinalibe mʼbusa, ndipo pamene zinabalalika zinakhala chakudya cha zirombo zonse zakuthengo.
6 Et mes brebis ont été dispersées dans toutes les montagnes et sur toutes les hautes collines; elles ont été dispersées sur toute la face de la terre; et il n'y avait personne pour les chercher et les ramener.
Nkhosa zanga zinayendayenda mʼmapiri onse ndi mʼzitunda zonse zazitali. Zinabalalika pa dziko lonse lapansi, ndipo palibe amene anazilondola kapena kuzifunafuna.
7 À cause de cela, pasteurs, écoutez la parole du Seigneur:
“‘Choncho Inu abusa, tamvani zimene Ine Yehova ndikukuwuzani.
8 Par ma vie, dit le Seigneur Maître, en punition de ce que mes brebis ont été une proie, de ce que mes brebis ont été dévorées par toutes les bêtes fauves des champs, parce qu'elles n'avaient pas de pasteurs, et que les pasteurs ne cherchaient pas mes brebis, et que les pasteurs se paissaient eux-mêmes et ne paissaient pas mes brebis;
Pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Wamphamvuzonse, ndithu, nkhosa zanga zinajiwa ndi zirombo zakuthengo, zinasanduka chakudya cha zirombo chifukwa panalibe abusa. Abusa anga sanafunefune nkhosa zanga. Iwo ankangosamala za iwo okha mʼmalo mosamala nkhosa zanga.
9 En punition de cela, pasteurs,
Chifukwa chake, inu abusa, tamvani zimene Ine Yehova ndikukuwuzani.
10 Ainsi dit le Seigneur Maître: Voilà que je suis contre les pasteurs, et je réclamerai mes brebis de leurs mains, et je les empêcherai de paître mes brebis, et les pasteurs ne les feront plus paître; je retirerai mes brebis de leur bouche, et ils ne s'en nourriront plus.
Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndayipidwa nanu, inu abusa. Ndidzakulandani nkhosa zanga ndipo simudzazidyetsanso. Ndidzakuchotsani pa ntchito ya ubusa kuti musamangodzidyetsa nokha. Ndidzalanditsa nkhosa zanga kukamwa kwanu ndipo simudzazidyanso.
11 Car ainsi dit le Seigneur Maître: Voilà que je vais moi-même chercher mes brebis, et je les visiterai.
“‘Tsono Ine Ambuye Yehova ndikuti, mwini wakene ndidzazifunafuna nkhosa zanga ndi kuzisamalira.
12 Tel le pâtre cherche ses troupeaux le jour où il y a des nuages et des ténèbres, au milieu des brebis dispersées, tel je chercherai mes brebis, et je les ramènerai de tous les lieux où elles auront été dispersées dans les jours de ténèbres et de nuages.
Monga mʼbusa amanka nafunafuna nkhosa zake pamene zina zabalalikira kutali, moteronso Ine ndidzafunafuna nkhosa zanga. Ndidzazipulumutsa kuchoka kumalo onse kumene zinabalalikira pa nthawi yankhungu ndi mdima.
13 Et je les retirerai d'entre les nations, et je les réunirai de toutes les contrées, et je les ferai rentrer dans leur terre, et je les ferai paître sur la montagne d'Israël, et dans tous les vallons et dans tous les lieux habités de leur héritage.
Ndidzazitulutsa pakati pa mitundu ya anthu ndi kuzisonkhanitsa kuchokera ku mayiko ena, ndipo ndidzazibwezera ku dziko lawo. Ndidzaziwetera ku mapiri a Israeli, mʼmbali mwa mitsinje ndi kumalo kumene kumakhala anthu.
14 Je les ferai paître en un bon pâturage, sur la haute montagne d'Israël; et c'est là que seront leurs bergeries; et elles y dormiront, et elles s'y reposeront dans les délices, et elles iront paître en un gras pâturage, sur les montagnes d'Israël.
Ndidzaziwetera kumalo a msipu wabwino. Mapiri okwera a Israeli adzakhala malo azidyetserako. Kumeneko zidzapumula ku abusa abwino a msipu ndipo zizidzadyadi msipu wonenepetsa pa mapiri a Israeli.
15 Moi-même je ferai paître mes brebis; je leur donnerai moi-même le repos; et elles sauront que je suis le Seigneur Maître. Voici ce que dit le Seigneur Maître:
Ine mwini wake ndidzaziweta nkhosa zanga ndi kuzilola kuti zipumule. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
16 Je chercherai celle qui sera perdue; je ramènerai celle qui sera égarée; j'entourerai de bandes celle qui sera blessée; je fortifierai les faibles; je veillerai sur les fortes, et je les ferai paître selon la justice.
Ndidzafunafuna zotayika ndi kubweza zosochera. Ndidzamanga mabala a zopweteka ndi kulimbikitsa zofowoka. Koma zonenepa ndi zamphamvu ndidzaziwononga. Ndidzaweta nkhosazo mwachilungamo.
17 Et vous, brebis, dit le Seigneur Maître, voilà que je distinguerai entre brebis et brebis, entre boucs et béliers.
“‘Kunena za inu, nkhosa zanga, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzaweruza pakati pa nkhosa ndi nkhosa, pakati pa nkhosa zazimuna ndi mbuzi zazimuna.
18 Ne vous suffisait-il pas de brouter un bon pâturage? Pourquoi fouler aux pieds le reste de votre pâturage? Ne vous suffisait-il pas de boire de l'eau paisible? Pourquoi troubler encore de vos pieds ce que vous n'aviez pas bu?
Kodi sikukukwanirani kudya msipu wabwino kuti muzichita kuponderezanso msipu umene simunadyewo? Kodi simukhutira ndi kumwa madzi abwino kuti muzinka mudetsanso madzi otsalawo ndi mapazi anu?
19 Mes autres brebis n'ont-elles pas brouté l'herbe que vos pieds avaient foulée? N'ont-elles pas bu l'eau que vous aviez troublée?
Kodi nkhosa zanga zidye zimene mwazipondaponda ndi kumwa madzi amene mwawadetsa ndi mapazi anu?
20 À cause de cela, voici ce que dit le Seigneur Maître: Je distinguerai entre les brebis fortes et les brebis faibles.
“‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Taonani, Ine mwini wake ndidzaweruza pakati pa nkhosa zonenepa ndi nkhosa zowonda.
21 Vous heurtiez de vos flancs et de vos épaules, vous frappiez de vos cornes, vous opprimiez toute brebis faible.
Popeza zofowoka mumaziwomba ndi kuzikankhira kumbali, ndipo mumazigunda ndi nyanga zanu nʼkuzimwazira kutali,
22 Et moi je sauverai mes brebis, et elles ne seront plus une proie, et je jugerai entre bélier et bélier.
tsono Ine ndidzapulumutsa nkhosa zanga, ndipo sindidzalolanso kuti zijiwe. Ndidzaweruza pakati pa nkhosa ina ndi nkhosa inanso.
23 Et je susciterai pour eux un seul pasteur, et il les fera paître; je susciterai mon serviteur David, et il sera leur pasteur.
Ndidzaziyikira mʼbusa mmodzi, mtumiki wanga Davide. Iyeyo ndiye azidzazisamala. Adzakhala mʼbusa wawo.
24 Et moi, le Seigneur, je serai leur Dieu, et David, au milieu d'eux, sera leur roi. Moi, le Seigneur, j'ai parlé.
Ine Yehova ndidzakhala Mulungu wake ndipo mtumiki wanga Davide adzakhala mfumu pakati pa nkhosazo. Ine Yehova ndayankhula.
25 Et je ferai avec David une alliance de paix, et je ferai disparaître de la terre les bêtes malfaisantes, et l'on habitera le désert, et l'on dormira dans les forêts.
“‘Ndidzapangana nazo pangano la mtendere. Ndidzachotsa mʼdzikomo zirombo zolusa. Choncho nkhosa zanga zidzakhala mu mtendere mu chipululu ngakhalenso mʼthengo.
26 Et je donnerai à mes brebis tout le contour de ma montagne; et je leur donnerai de la pluie, une pluie de bénédiction.
Ndidzakhazika anthu anga pafupi ndi phiri langa loyera ndipo ndidzawadalitsa. Ndidzawagwetsera mvula pa nthawi yake ndipo idzakhala mvula ya madalitso.
27 Et les terres des champs produiront leurs fruits; et la terre aura toute sa fertilité; et mes brebis habiteront leur héritage dans l'espérance de la paix; et elles sauront que je suis le Seigneur quand j'aurai brisé leur joug, et que je les aurai retirées des mains de ceux qui les ont asservies.
Mitengo ya mʼminda idzabereka zipatso zake, ndipo nthaka idzakhala ndi zokolola zake. Anthu adzakhala mwamtendere mʼdziko lawo. Iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene ndidzathyola magoli awo ndi kuwapulumutsa kuchoka mʼmanja mwa amene anawagwira ukapolo.
28 Et elles ne seront plus livrées en proie aux nations; et les bêtes fauves ne les dévoreront plus, et elles habiteront leur héritage dans l'espérance, et nul ne les épouvantera plus.
Anthu amitundu ina sadzawafunkhanso ndipo sadzadyedwa ndi zirombo zakuthengo. Adzakhala mwamtendere ndipo palibe amene adzawaopseze.
29 Et je ferai naître pour elles une plante de paix, et elles ne périront plus par la famine sur la terre, et elles ne subiront plus les outrages des nations.
Ndidzawapatsa zokolola zochuluka motero kuti sadzavutikanso ndi njala. Anthu a mitundu ina sadzawanyozanso.
30 Et elles sauront que je suis le Seigneur leur Dieu, et qu'elles sont mon peuple. Maison d'Israël, dit le Seigneur Maître,
Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wawo ndili nawo pamodzi, ndipo kuti iwo, Aisraeli, ndi anthu anga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
31 Vous êtes mes brebis, les brebis de mon troupeau; et je suis votre Dieu, dit le Seigneur Maître.
Inu ndinu nkhosa zanga, nkhosa zimene ndimazidyetsa. Ine ndine Mulungu wanu. Ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse.’”

< Ézéchiel 34 >