< Ézéchiel 26 >

1 Et en l'année onzième, le premier jour du mois, la parole du Seigneur me vint, disant:
Pa chaka cha khumi ndi chimodzi, tsiku loyamba la mwezi, Yehova anandiyankhula kuti:
2 Fils de l'homme, en punition de ce que Tyr a dit de Jérusalem: C'est bien! elle est brisée, son peuple a péri, son trafic est revenu à moi; elle qui était remplie, la voilà vide;
“Iwe mwana wa munthu, anthu a ku Turo ananyogodola Yerusalemu kuti ‘Hii! Uja amene anali chipata choloweramo anthu a mitundu ina wawonongeka. Zitseko zake zatsekukira ife. Tidzalemera popeza wasanduka bwinja.’
3 En punition de cela, ainsi dit le Seigneur: Voilà que je suis contre toi, Tyr, et je conduirai coutre toi maintes nations, comme la mer monte avec ses vagues.
Nʼchifukwa chake, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakulangani, inu anthu a ku Turo. Ndidzakuyitanirani anthu a mitundu ina kuti adzakulangeni monga momwe mafunde amawombera pa Nyanja.
4 Et elles abattront tes remparts, ô Tyr, et elles abattront tes tours; et je vannerai loin d'elle sa poussière, et je ferai d'elle une roche nue.
Anthuwo adzawononga makoma a Turo ndi kugwetsa nsanja zake. Ndidzapala dothi lake ndipo ndidzamusandutsa thanthwe losalala.
5 Elle sera au milieu de la mer un lieu à faire sécher les filets; car c'est moi qui ai parlé, dit le Seigneur. Et elle sera livrée en proie aux nations.
Udzakhala poyanikapo makoka pakati pa nyanja. Ine Ambuye Yehova ndayankhula zimenezo. Udzasanduka chofunkha cha anthu a mitundu ina.
6 Et ses filles, dans les champs, périront par le glaive, et elles sauront que je suis le Seigneur.
Anthu okhala ku mtunda adzasakazidwa ndi lupanga. Pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
7 Car ainsi dit le Seigneur: Voilà que de l'aquilon je conduis contre toi, Tyr, Nabuchodonosor, roi de Babylone; il est le roi des rois, avec des chevaux et des chars, et des cavaliers, et un rassemblement de maintes nations.
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Iwe Turo, ndidzakubweretsera Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni mfumu ya mafumu, kuchokera kumpoto pamodzi ndi akavalo ndiponso magaleta, anthu okwera pa akavalo ndi gulu lalikulu la ankhondo.
8 Il fera périr tes filles par le glaive dans les champs; il placera contre toi des gardes avancées; il bâtira autour de toi des forts; il t'enveloppera de palissades; il t'entourera de camps; il lancera devant toi ses javelines.
Anthu okhala ku mtunda adzawapha ndi lupanga. Adzapanga mitumbira yankhondo ndi kukukwezera zishango kuti alimbane nawe.
9 Il renversera de ses glaives tes remparts et tes tours.
Adzagwetsa makoma ako ndi zida zogumulira khoma ndi kugwetsa nsanja zako ndi nkhwangwa zake.
10 À cause de la multitude de ses chevaux, tu seras couverte de poussière par le fracas de ses cavaliers et des roues de ses chars; tes murs seront ébranlés quand il franchira tes portes, comme on franchit dans la plaine l'entrée d'une ville.
Akavalo ake adzakhala ochuluka kwambiri kotero kuti adzakukwirira ndi fumbi lawo. Makoma ako adzagwedezeka ndi mdidi wa akavalo, ngolo ndi magaleta pamene iye adzalowa pa zipata monga mmene amalowera mu mzinda umene makoma ake agwetsedwa.
11 Les sabots de ses coursiers fouleront toutes tes places, et il passera ton peuple au fil de l'épée, et tout ce qui fait ta force, il le renversera par terre.
Akavalo ake adzapondaponda mʼmisewu yako yonse ndi ziboda zawo. Adzapha anthu ako ndi lupanga. Mizati yako yolimba idzagwetsedwa.
12 Et il pillera tes richesses, et il enlèvera tes marchandises; il abattra tes murs; il détruira tes maisons si convoitées, et il jettera au fond de la mer qui te baigne tes pierres, tes bois et ta poussière.
Iwo adzafunkha chuma chako ndipo adzalanda zinthu zako za malonda. Adzagwetsa makoma ako ndi kuwononga nyumba zako zabwino. Adzaponya miyala yako, matabwa ako ndi dothi lako mʼnyanja.
13 Et il fera cesser tes nombreux concerts, et on n'entendra plus la voix de tes harpes.
Choncho ndidzathetsa phokoso la nyimbo zanu, ndipo kulira kwa apangwe ako sikudzamvekanso.
14 Et je ferai de toi une roche nue, un lieu à faire sécher les filets, et tu ne seras plus rebâtie; car moi, le Seigneur, j'ai parlé, dit le Seigneur.
Ndidzakusandutsa thanthwe losalala, ndipo udzakhala malo woyanikapo makoka a nsomba. Sudzamangidwanso, pakuti Ine Yehova ndayankhula, akutero Ambuye Yehova.
15 Car voici ce que dit à Tyr le Seigneur Maître: Les îles ne trembleront-elles pas au bruit de ta chute, quand tes blessés gémiront et que le glaive sera tiré au milieu de toi?
“Ine Ambuye Yehova ndikukuwuza, iwe mzinda wa Turo, kuti zilumba zidzagwedezeka pakumva za kugwa kwako ndiponso poona anthu opweteka akubuwula ndipo anthu akuphedwa pakati pako.
16 Et tous les rois des nations maritimes descendront de leur trône, et ils déposeront leurs mitres de leurs têtes, et ils se dépouilleront de leurs vêtements brodés. Ils seront frappés de stupeur; ils s'asseyeront à terre, et ils craindront de périr, et ils gémiront sur toi.
Pamenepo mafumu a mʼmbali mwa nyanja adzatsika pa mipando yawo yaufumu. Adzayika pambali mikanjo yawo ndi kuvala zovala zawo zamakaka. Adzachita mantha ndipo adzakhala pansi akunjenjemera kosalekeza. Adzathedwa nzeru poona zimene zakugwera.
17 Et ils feront de toi un sujet de lamentation, et ils te diront: Comment as-tu cessé de sillonner la mer, ô ville si célèbre, toi qui inspirais ta crainte à tous ceux qui demeurent sur tes rives?
Pamenepo adzayimba nyimbo yokudandaula ndipo adzati kwa iwe: “‘Nʼkuchita kuwonongeka chotere, iwe mzinda wotchuka, wodzaza ndi anthu a ku nyanja! Unali wamphamvu pa nyanja, iwe ndi nzika zako; unkaopseza anthu onse amene ankakhala kumeneko.
18 Et les elles trembleront au jour de ta chute.
Tsopano mayiko a mʼmbali mwa nyanja akunjenjemera chifukwa cha kugwa kwako; okhala pa zilumba nawonso agwidwa ndi mantha aakulu chifukwa cha kugwa kwako.’
19 Car voici ce que dit le Seigneur Maître: Lorsque j'aurai fait de toi une solitude comme des villes qui ne seront plus habitées, quand j'aurai fait passer sur toi l'abîme, et que les grandes eaux te couvriront,
“Mawu a Ine Ambuye Yehova ndi awa: Ndidzakusandutsa bwinja, ngati mizinda imene anthu sangathe kukhalamo. Ndidzakuphimba ndi madzi ozama a mʼnyanja, madzi amphamvu woti akumize.
20 Je te précipiterai parmi ceux qui sont tombés dans le gouffre, chez le peuple éternel, et je te placerai au plus profond de la terre, comme en un désert éternel parmi ceux qui sont tombés dans le gouffre, afin que tu ne sois plus habitée; et tu ne reviendras plus sur la terre des vivants.
Ndidzakugwetsa pansi kuti ukhale pamodzi ndi anthu amvulazakale amene akutsikira ku manda. Ine ndidzakusunga ku dzenjeko ngati ku bwinja losiyidwa kalekale, pamodzi ndi anthu amene anafa kale motero sudzabwererako kukhala pakati pa anthu amoyo.
21 Je te perdrai, et tu ne subsisteras plus dans les siècles, dit le Seigneur Maître.
Ine ndidzakuthetsa mochititsa mantha, ndipo sudzakhalaponso. Anthu adzakufunafuna, koma sudzapezekanso, akutero Ambuye Yehova.”

< Ézéchiel 26 >