< Ézéchiel 18 >

1 Et la parole du Seigneur me vint, disant:
Yehova anandiyankhula nati:
2 Fils de l'homme, d'où vient cette parabole qui se dit parmi les enfants d'Israël: Les pères ont mangé du verjus, et les dents des enfants en ont été agacées?
“Kodi anthu inu mumatanthauza chiyani mukamabwerezabwereza kunena mwambi uwu wokhudza dziko la Israeli kuti: “‘Nkhuyu zodya akulu zimapota ndi ana omwe?’”
3 Par ma vie, dit le Seigneur, on ne répètera plus cette parabole en Israël.
“Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, simudzanenanso mwambi umenewu mu Israeli.
4 Car toutes les âmes sont à moi; les âmes des fils sont à moi, comme l'âme du père. L'âme qui pèche, voilà celle qui mourra.
Pakuti moyo uliwonse ndi wanga. Moyo wa abambo ndi wanga, wamwananso ndi wanga. Munthu wochimwa ndi amene adzafe.
5 L'homme qui sera juste, qui observera les jugements et l'équité,
“Tiyerekeze kuti pali munthu wolungama amene amachita zolungama ndi zolondola.
6 Ne mangera pas sur les hauts lieux; il ne lèvera pas les yeux sur les idoles de la maison d'Israël; il ne profanera point la femme de son prochain; il ne s'approchera pas de sa femme dans son impureté.
Iye sadyera nawo pa mapiri a chipembedzo kapena kupembedza mafano a Aisraeli. Iye sayipitsa mkazi wa mnzake kapena kugonana ndi mkazi pamene akusamba.
7 Il n'opprimera pas âme qui vive; il rendra le gage du débiteur; il ne commettra aucune rapine; il donnera de son pain au pauvre, et il vêtira les nus.
Iye sapondereza munthu wina aliyense, koma amabwezera wangongole nʼchigwiriro chake. Iye salanda zinthu za osauka, koma amapereka chakudya kwa anthu anjala, ndipo amapereka zovala kwa anthu ausiwa.
8 Et il ne placera pas son argent à usure, et il ne prendra pas plus qu'il ne lui est dû, et il détournera la main de l'iniquité, et il rendra un jugement juste entre un homme et son prochain.
Iye sakongoletsa ndalama mwa katapira, kapena kulandira chiwongoladzanja chachikulu. Amadziletsa kuchita zoyipa ndipo sakondera poweruza milandu.
9 Celui-là aura marché en mes commandements; il aura gardé mes ordonnances pour les mettre en pratique. Celui-là est juste, et il vivra de la vie, dit le Seigneur.
Iye amatsatira malangizo anga, ndipo amasunga malamulo anga mokhulupirika. Munthu ameneyo ndi wolungama; iye adzakhala ndithu ndi moyo, akutero Ambuye Yehova.
10 Et s'il a engendré un fils corrompu qui verse le sang et commette des péchés,
“Tiyerekeze kuti munthu wolungama chotere wabala mwana chimbalangondo amene amakhalira kupha anthu ndi kuchita zinthu zina zotere.
11 Celui-là n'aura pas marché dans la voie de son père; mais il aura mangé sur les hauts lieux, il aura profané la femme de son prochain;
Iye nʼkumachita zinthu zimene ngakhale abambo ake sanachitepo. “Amadyera nawo ku mapiri achipembedzo. Amayipitsa mkazi wa mnzake.
12 Il aura opprimé le pauvre et le mendiant; il aura pris avec violence; il n'aura pas rendu le gage; il aura arrêté ses regards sur les idoles; il aura fait l'iniquité;
Iye amapondereza munthu wosauka ndi wosowa. Amalanda zinthu za osauka. Sabweza chikole cha munthu wa ngongole. Iye amatembenukira ku mafano nachita zonyansa.
13 Il aura placé à usure; il se sera fait rendre plus qu'il ne lui était dû; celui-là ne vivra pas de la vie: pour avoir fait toutes ces iniquités, il mourra de mort, et son sang sera sur sa tête.
Iye amakongoletsa mwa katapira ndipo amalandira chiwongoladzanja chachikulu. Kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu! Chifukwa wachita zinthu zonyansa zonsezi, adzaphedwa ndipo adzalandira chilango chomuyenera.
14 Et si cet homme a engendré un fils qui ait vu tous les péchés commis par son père, mais qui en ait eu peur et ne les ait pas commis;
“Tsono tiyerekeze kuti munthu woyipa uyu wabala mwana amene amaona machimo onse amene abambo ake ankachita. Ngakhale amaona koma osatsanzira ntchito zake zoyipazo.
15 Qui ne monte pas sur les hauts lieux; qui n'arrête pas ses regards sur les idoles de la maison d'Israël; qui ne profane point la femme de son prochain;
“Sadyera nawo pa mapiri achipembedzo. Sapembedza mafano a ku Israeli. Sayipitsa mkazi wa mnzake.
16 Qui n'opprime pas âme qui vive; qui ne retienne pas de gages; qui ne commette aucune rapine; qui donne de son pain au pauvre et vêtisse les nus;
Sapondereza munthu wina aliyense. Satenga chikole akabwereketsa chinthu. Salanda zinthu za osauka. Salanda zinthu za munthu. Amapereka chakudya kwa anthu anjala. Amapereka zovala kwa anthu aumphawi.
17 Qui détourne sa main de l'iniquité, qui ne reçoive ni usure ni plus qu'il ne lui est dû; qui fasse justice; qui marche en mes commandements: il ne mourra pas à cause des iniquités de son père, il vivra de la vie.
Amadziletsa kuchita zoyipa. Sakongoletsa kuti apezepo phindu. Salandira chiwongoladzanja. Amasunga malangizo anga ndi kumvera malamulo anga. Munthu wotereyo sadzafa chifukwa cha machimo a abambo ake. Adzakhala ndi moyo ndithu.
18 Et son père, pour avoir opprimé, pour avoir pris avec violence, pour avoir fait le mal devant mon peuple, mourra dans son iniquité.
Koma abambo ake, popeza kuti anazunza anthu ena ndi kubera mʼbale wawo ndiponso popeza kuti sanachitire zabwino anansi ake, adzafera machimo ake omwe.
19 Et vous direz: Pourquoi le fils n'a-t-il pas porté la peine de l'iniquité du père? Parce que le fils a fait justice et miséricorde, qu'il a gardé mes ordonnances et les a mises en pratique: il vivra de la vie.
“Mwina inu mukhoza kufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani mwana salangidwa chifukwa cha kulakwa kwa abambo ake? Ayi, mwanayo adzakhala ndi moyo chifukwa ankachita zolungama ndi zolondola ndipo ankasamala kumvera malamulo anga onse.
20 Et l'âme qui pèche mourra; le fils ne portera pas la peine de l'iniquité du père; le père ne portera pas la peine de l'iniquité du fils. La justice du juste sera sur lui, et l'iniquité de l'injuste sera sur lui.
Munthu wochimwa ndiye amene adzafe. Mwana sadzapezeka wolakwa chifukwa cha abambo ake, kapena abambo kupezeka wolakwa chifukwa cha mwana wawo. Chilungamo cha munthu wolungama ndicho chidzamupulutse, ndipo kuyipa kwa munthu wochimwa ndiko kudzamuwonongetse.
21 Et le pécheur, s'il revient de ses dérèglements, garde tous mes commandements, s'il fait justice et miséricorde, vivra de la vie et ne mourra point.
“‘Munthu woyipa akatembenuka mtima ndi kusiya machimo amene ankachita ndi kuyamba kumvera malamulo anga ndi kumachita zolungama ndi zokhulupirika, ndiye kuti adzakhala ndi moyo. Sadzafa ayi.
22 Toutes ses iniquités seront oubliées; il vivra dans son équité et à cause d'elle.
Zoyipa zake zonse zidzakhululukidwa. Chifukwa cha zinthu zolungama zimene anazichita adzakhala ndi moyo.
23 Est-ce que je veux la mort du pécheur? dit le Seigneur. Est-ce que je ne veux pas plutôt qu'il se détourne de sa voie mauvaise et qu'il vive?
Kodi Ine ndimakondwera ndi imfa ya munthu woyipa? Ayi, ndimakondwera pamene woyipa watembenuka mtima kuti akhale ndi moyo. Akutero Ambuye Yehova.
24 Si le juste se détourne de sa justice et tombe dans tous les péchés que fait l'homme inique, toutes les œuvres de sa justice seront oubliées; il mourra dans sa chute et dans ses péchés.
“‘Koma ngati munthu wolungama apatuka kusiya zachilungamo ndi kuyamba kuchita tchimo ndi zonyansa za mtundu uliwonse zimene amachita anthu oyipa, kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu, zolungama zake zonse sizidzakumbukiridwa. Iye adzayenera kufa chifukwa cha machimo amene anachita.
25 Et vous dites: La voie du Seigneur n'est pas droite! Écoutez donc, ô vous tous, maison d'Israël: Est-ce ma voie qui n'est pas droite? Est-ce votre voie qui est droite!
“Komabe inu mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Tamvani tsono inu Aisraeli: Kodi zochita zanga ndizo zosalungama? Kodi si zochita zanu zimene ndi zosalungama?
26 Quand le juste se détourne de sa justice, quand il fait un péché, quand il meurt dans le péché qu'il a fait, il meurt en ce péché.
Ngati munthu wolungama atembenuka kusiya chilungamo chake ndi kuchita tchimo, iye adzafa chifukwa cha tchimolo.
27 Et quand l'impie revient de son impiété, et qu'il fait jugement et justice, celui-là sauve son âme.
Koma ngati munthu woyipa aleka zoyipa zake zimene anazichita ndi kuyamba kuchita zimene ndi zolungama ndi zolondola, iye adzapulumutsa moyo wake.
28 Il s'est converti de toutes les impiétés qu'il avait faites; il vivra de la vie et ne mourra point.
Popeza waganizira za zolakwa zonse ankachita ndipo wazileka, iye adzakhala ndi moyo ndithu; sadzafa.
29 Et en la maison d'Israël ils disent: La voie du Seigneur n'est pas droite! Est-ce ma voie qui n'est pas droite, maison d'Israël? N'est-ce pas votre voie qui n'est pas droite?
Komabe Aisraeli akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Kodi zochita zanga ndizo zopanda chilungamo, inu Aisraeli? Kodi si zochita zanu zimene ndi zopanda chilungamo?
30 Je jugerai chacun de vous selon sa voie, maison d'Israël, dit le Seigneur; convertissez-vous, revenez de toutes vos impiétés, et vous ne serez point punis pour cause d'iniquités.
“Chifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: inu Aisraeli, Ine ndidzakuweruzani aliyense wa inu molingana ndi ntchito zake. Lapani! Lekani zoyipa zanu kuti musawonongeke nazo.
31 Repoussez loin de vous toutes les impiétés que vous avez commises contre moi; faites-vous un nouveau cœur, un esprit nouveau; et pourquoi péririez- vous, maison d'Israël?
Tayani zolakwa zanu zonse zimene munandichimwira nazo ndipo khalani ndi mtima watsopano ndi mzimu watsopano. Kodi muferanji inu Aisraeli?
32 Ce n'est pas moi qui veux la mort de celui qui périt, dit le Seigneur.
Ine sindikondwera ndi imfa ya munthu aliyense, akutero Ambuye Yehova. Chifukwa chake, lapani kuti mukhale ndi moyo.”

< Ézéchiel 18 >