< Ézéchiel 12 >

1 Et la parole du Seigneur me vint, disant:
Yehova anayankhula nane kuti,
2 Fils de l'homme, tu demeures au milieu des iniquités de ceux qui ont des yeux pour voir, et ne voient point; qui ont des oreilles pour entendre, et n'entendent point; car c'est une maison qui m'irrite.
“Iwe mwana wa munthu, ukukhala pakati pa anthu owukira, iwowo maso openyera ali nawo, koma sakuona ndipo makutu omvera ali nawo, koma sakumva chifukwa choti ndi anthu owukira.
3 Et maintenant, fils de l'homme, prépare ton bagage, pour aller en captivité devant eux en plein jour; et devant eux tu seras emmené captif de ce lieu en un autre lieu, afin qu'ils te voient; car c'est une maison qui m'irrite.
“Choncho, iwe mwana wa munthu, longedza katundu wako wopita naye ku ukapolo. Unyamuke nthawi yamasana iwo akuona. Uchite ngati wanyamuka kuchoka kumene ukukhala kupita ku dziko lachilendo iwowo akuona. Mwina adzamvetsetsa, paja ndi anthu aupandu.
4 Et tu transporteras ton bagage pour aller en captivité devant eux, en plein jour; puis, sous leurs yeux, tu sortiras le soir, comme sort un captif.
Utulutse katundu wako wopita naye ku ukapolo nthawi ya masana iwo akuona. Ndipo nthawi ya madzulo, iwo akuona, uchoke monga ngati ukupita ku ukapolo.
5 Creuse-toi un trou dans le mur de ta maison, et tu passeras par ce trou,
Iwo akuona, ubowole pa khoma ndipo utulutsirepo katundu wako.
6 Devant eux. Tu te feras porter sur des épaules, et tu sortiras dans les ténèbres; tu te cacheras le visage, et tu ne verras pas la terre; car je t'ai donné comme un signe à la maison d'Israël.
Usenze katundu wako pa phewa iwo akuona, ndipo upite kunja ku mdima. Uphimbe nkhope yako kuti usaone pansi, pakuti ndakusandutsa iwe chizindikiro chochenjeza Aisraeli.”
7 Et je fis toutes ces choses, comme le Seigneur me l'avait commandé, et je transportai en plein jour mon bagage pour aller en captivité; et le soir je fis pour moi un trou au mur, et je sortis dans les ténèbres, et je me fis porter sur des épaules devant eux.
Choncho ine ndinachita monga momwe anandilamulira. Nthawi yamasana ndinatulutsa zinthu zanga nditazimanga ngati ndikupita ku ukapolo. Ndipo nthawi yamadzulo ndinabowola khoma ndi manja anga. Pamene chisisira chinkayamba, ndinasenza katundu wanga pa phewa kutuluka naye iwo akuona.
8 Et le matin, la parole du Seigneur me vint, disant:
Mmawa mwake Yehova anandiyankhula nati:
9 Fils de l'homme, la maison d'Israël, cette maison qui m'irrite, n'a-t-elle pas dit: Que fais-tu?
“Iwe mwana wa munthu, kodi anthu aupandu a Israeli sanakufunse kuti ukuchita chiyani?
10 Dis-leur: Ainsi parle le Seigneur: Moi, le prince et le chef de Jérusalem, à tout le peuple d'Israël, à tous ceux qui sont dans la ville,
“Uwawuze kuti, ‘zimene ndikunena Ine Ambuye Wamphamvuzonse ndi izi: Uthengawu ndi wonena za kalonga wa ku Yerusalemu pamodzi ndi banja lonse la Israeli amene akukhala kumeneko.’
11 J'ai dit: Je fais pour eux des signes; et comme j'ai fait, il leur adviendra. Ils partiront pour l'exil et la captivité.
Uwawuze kuti, ‘Ndiwe chizindikiro chowachenjeza.’ “Zidzakuchitikirani monga momwe zakuchitikira iwemu. Iwo adzatengedwa kupita ku ukapolo.”
12 Et, au milieu d'eux, le roi sera porté sur des épaules, et il sortira dans les ténèbres, par une brèche de mur, et il aura fait cette brèche pour sortir; il se cachera le visage, de sorte que nul œil ne le verra, et lui-même ne verra pas la terre.
“Kalonga wawo adzatenga katundu wake nʼchisisira nʼkunyamuka. Adzatulukira pa bowo limene anthu anabowola pa khoma. Adzaphimba nkhope yake kuti asaone kumene akupita.
13 Et je tendrai mon filet sur lui, et il y sera pris, et je le conduirai à Babylone, en la terre des Chaldéens; et il ne la verra pas, et il y mourra.
Ndidzayala ukonde wanga pa iye ndi kumukola mu msampha wanga. Ndidzabwera naye ku Babuloni, dziko la Akaldeya, koma sadzaliona dzikolo, ndipo adzafera kumeneko.
14 Et tous ses auxiliaires d'alentour, et tous ses alliés, je les disperserai à tous les vents, et je les poursuivrai à coups d'épée.
Ine ndidzabalalitsa kumbali zonse zinayi onse okhala naye pafupi, ndiwo omuthandiza ake pamodzi ndi ankhondo ake. Ndidzawalondola ndi lupanga losolola.
15 Et ils connaîtront que je suis le Seigneur, quand je les aurai dispersés parmi les nations, et ils seront dispersés dans toutes les contrées.
“Iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzawamwaza pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsira ku mayiko ena.
16 Et parmi eux je ferai échapper un petit nombre d'hommes au glaive, à la famine et à la peste, afin qu'ils racontent toutes leurs iniquités chez les nations où ils iront résider, et qu'elles sachent que je suis le Seigneur.
Koma ndidzasiyako ena pangʼono amene adzapulumuke ku lupanga, njala ndi mliri, kuti akafotokoze ntchito zawo zonse zonyansa pakati pa anthu achilendo kumene akupitako. Pamenepo adzadziwa kuti ndine Yehova.”
17 Et la parole du Seigneur me vint, disant:
Pambuyo pake Yehova anandiyankhulanso nati,
18 Fils de l'homme, mange ton pain dans la tristesse; bois ton eau dans les tourments et l'affliction.
“Iwe mwana wa munthu, uzinjenjemera ukamadya chakudya chako, ndipo uzinthunthumira ndi mantha ukamamwa madzi ako.
19 Et dis au peuple de la terre: Ainsi parle le Seigneur à ceux qui demeurent à Jérusalem et sur le territoire d'Israël: Ils mangeront le pain dans la détresse, et ils boiront leur eau dans la désolation, lorsque cette terre sera détruite avec sa richesse; car tous ceux qui l'habitent vivent dans l'impiété.
Uwawuze anthu a mʼdzikomo kuti izi ndi zimene Ambuye Wamphamvuzonse akunena za anthu okhala mu Yerusalemu ndi dziko la Israeli: Iwo adzadya chakudya chawo ndi mantha ndi kumwa madzi awo ndi nkhawa. Zonse za mʼdziko lawo zidzalandidwa chifukwa cha ziwawa za anthu onse okhala mʼmenemo.
20 Et je rendrai désertes leurs villes si peuplées, et leur terre sera dévastée; et vous saurez que je suis le Seigneur.
Mizinda imene ili ndi anthu idzasakazika ndipo dziko lidzasanduka chipululu. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
21 Et la parole du Seigneur me vint, disant:
Yehova anayankhulanso nane kuti,
22 Fils de l'homme, quelle est cette parabole que l'on dit sur la terre: Les jours sont loin, la vision a péri?
“Iwe mwana wa munthu, kodi mwambi umene ukunenedwa mu Israeli ndi wotani: ‘Masiku akupita koma masomphenya onse sakukwaniritsidwa?’
23 À cause de cela, dis-leur: Ainsi parle le Seigneur: Je changerai cette parabole, et on ne répètera plus cette parabole en la maison d'Israël; car tu lui diras: Les jours sont proches, et toutes les paroles de la vision.
Choncho uwawuze anthuwo kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndidzawuthetsa mwambi umenewu ndipo sadzawunenanso mu Israeli.’ Uwawuze kuti, ‘masiku ayandikira oti zonse zimene ndinanena mʼmasomphenya zichitikedi.
24 Car il n'y aura plus de vision fausse, ni de faux prophètes qui prédisent au milieu des fils d'Israël pour leur plaire.
Pakuti masiku amenewo sikudzakhalanso masomphenya abodza kapena kuwombeza kwa chinyengo pakati pa anthu a Israeli.
25 Car moi-même, le Seigneur, je dirai mes paroles; je parlerai et j'exécuterai, et je ne différerai plus; car c'est en ces jours mêmes où cette maison m'irrite, que je vais parler, et j'exécuterai, dit le Seigneur.
Koma Ine Ambuye ndidzayankhula chimene ndikufuna, ndipo chidzachitikadi, osachedwa ayi. Pakuti mʼmasiku anu omwe ano, inu anthu opanduka, ndidzakwaniritsa chilichonse chimene ndidzanena. Ndikutero Ine Yehova.’”
26 Et la parole du Seigneur me vint, disant:
Yehova anandiyankhula nati:
27 Fils de l'homme, voilà que la maison d'Israël m'irrite; ils disent: La vision que cet homme a eue est pour des jours lointains, et il prophétise ainsi pour des temps loin de nous.
“Iwe mwana wa munthu, Aisraeli akunena kuti, ‘masomphenya amene ukuona sadzachitika kwa zaka zambiri. Iwo akuti ukulosa za zinthu zimene zidzachitika ku tsogolo kwambiri.’
28 À cause de cela, dis-leur: Ainsi parle le Seigneur: La parole que j'ai dite ne tardera pas à s'accomplir: je vais parler et j'exécuterai, dit le Seigneur.
“Choncho uwawuze kuti, ‘zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena ndi izi: Zonena zanga sizidzachedwanso; chilichonse chimene ndikunena chidzachitikadi. Ndikutero Ine Yehova.’”

< Ézéchiel 12 >