< Ecclésiaste 7 >

1 Bon renom vaut mieux que bon parfum; le jour de la mort vaut mieux que le jour de la naissance.
Mbiri yabwino ndi yopambana mafuta onunkhira bwino, ndipo tsiku lomwalira ndi lopambana tsiku lobadwa.
2 Il vaut mieux aller à la maison du deuil qu'à la maison du festin, puisque le deuil est la fin de tout homme, et que le vivant donnera ainsi de bons avertissements à son cœur.
Kuli bwino kupita ku nyumba yamaliro kusiyana ndi kupita ku nyumba yamadyerero: Pakuti imfa ndiye mathero a munthu aliyense; anthu amoyo azichisunga chimenechi mʼmitima mwawo.
3 La tristesse vaut mieux que le rire; parce que, par la tristesse du visage, le cœur deviendra bon.
Chisoni nʼchabwino kusiyana ndi kuseka, pakuti nkhope yakugwa ndi yabwino chifukwa imakonza mtima.
4 Le cœur des sages est à la maison des pleurs; le cœur des insensés est à la maison d'allégresse.
Mtima wa munthu wanzeru nthawi zonse umalingalira za imfa, koma mitima ya zitsiru imalingalira za chisangalalo.
5 Mieux vaut écouter la réprimande d'un sage, que d'entendre le chant des insensés.
Kuli bwino kumva kudzudzula kwa munthu wanzeru kusiyana ndi kumvera mayamiko a zitsiru.
6 Le rire des insensés est comme le pétillement des épines sous une chaudière; et cela encore est vanité.
Kuseka kwa zitsiru kuli ngati kuthetheka kwa moto kunsi kwa mʼphika, izinso ndi zopandapake.
7 La calomnie trouble le sage, et lui fait perdre sa force d'âme.
Kuzunza ena kumasandutsa munthu wanzeru kukhala chitsiru, ndipo chiphuphu chimawononga mtima.
8 La fin du discours vaut mieux que le commencement; un homme patient vaut mieux qu'un esprit présomptueux.
Mathero ake a chinthu ndi abwino kupambana chiyambi chake, ndipo kufatsa nʼkwabwino kupambana kudzikuza.
9 Ne t'abandonne pas trop vite au souffle de la colère; car la colère réside dans le sein des insensés.
Usamafulumire kukwiya mu mtima mwako, pakuti mkwiyo ndi bwenzi la zitsiru.
10 Garde-toi de dire: Comment se fait-il que les jours d'autrefois ont été meilleurs que ceux d'à présent? Car il n'est point sage de s'enquérir de ces choses.
Usamafunse kuti, “Nʼchifukwa chiyani masiku amakedzana anali abwino kupambana masiku ano?” pakuti si chinthu chanzeru kufunsa mafunso oterewa.
11 La sagesse est bonne, unie aux richesses; elle est alors profitable à ceux qui vivent sous le soleil.
Nzeru ngati cholowa, ndi chinthu chabwino ndipo imapindulitsa wamoyo aliyense pansi pano.
12 Car on s'abrite à l'ombre de la sagesse, comme à l'ombre de l'argent; mais l'avantage de la science et de la sagesse, c'est qu'elles font vivre celui qui les possède.
Nzeru ndi chitetezo, monganso ndalama zili chitetezo, koma phindu la chidziwitso ndi ili: kuti nzeru zimasunga moyo wa munthu amene ali nazo nzeruzo.
13 Considère les œuvres de Dieu; car qui pourrait redresser celui que Dieu a courbé?
Taganizirani zimene Mulungu wazichita: ndani angathe kuwongola chinthu chimene Iye anachipanga chokhota?
14 Au jour de la prospérité vis dans le bien-être, et prévois le jour du malheur; prévois-le: car Dieu a fait telle chose concordant avec telle autre, à cause des propos des hommes, afin qu'ils ne trouvent rien à blâmer en Lui.
Pamene zinthu zili bwino, sangalala; koma pamene zinthu sizili bwino, ganizira bwino: Mulungu ndiye anapanga nthawi yabwinoyo, ndiponso nthawi imene si yabwinoyo. Choncho munthu sangathe kuzindikira chilichonse cha mʼtsogolo mwake.
15 J'ai vu toutes choses au jour de ma vanité. Le juste meurt avec sa justice; l'impie subsiste avec sa perversité.
Pa moyo wanga wopanda phinduwu ndaona zinthu ziwiri izi: munthu wolungama akuwonongeka mʼchilungamo chake, ndipo munthu woyipa akukhala moyo wautali mʼzoyipa zake.
16 Ne sois pas juste à l'excès; ne soit point sage plus qu'il ne faut, de peur que tu ne sois confondu.
Usakhale wolungama kwambiri kapena wanzeru kwambiri, udziwonongerenji wekha?
17 Mais ne sois pas non plus impie ni obstiné à l'excès, de peur que tu ne périsses avant le temps.
Usakhale woyipa kwambiri, ndipo usakhale chitsiru, uferenji nthawi yako isanakwane?
18 Il est bon que tu t'attaches à telle chose, et que tu t'éloignes de telle autre, pour ne point souiller tes mains; car tout vient à ceux qui craignent Dieu.
Nʼkwabwino kuti utsate njira imodzi, ndipo usataye njira inayo. Munthu amene amaopa Mulungu adzapewa zinthu ziwiri zonsezi.
19 La sagesse sera utile au sage plus que dix des plus puissants de la cité.
Nzeru zimapereka mphamvu zambiri kwa munthu wanzeru kupambana olamulira khumi a mu mzinda.
20 Car il n'est point sur la terre de juste qui fasse le bien, et ne pèche.
Palibe munthu wolungama pa dziko lapansi amene amachita zabwino zokhazokha ndipo sachimwa.
21 Mais ne dépose pas en ton cœur toutes les paroles que dirent les impies, de peur que tu n'entendes ton serviteur te maudire.
Usamamvetsere mawu onse amene anthu amayankhula, mwina udzamva wantchito wako akukutukwana,
22 Car maintes fois il t'irritera, et il t'affligera de bien des manières; car toi-même aussi tu as maudit les autres.
pakuti iwe ukudziwa mu mtima mwako kuti nthawi zambiri iwenso unatukwanapo ena.
23 J'ai éprouve toutes choses en ma sagesse, et j'ai dit: Je serai sage; et la sagesse s'est éloignée de moi.
Zonsezi ndinaziyesa ndi nzeru zanga ndipo ndinati, “Ine ndatsimikiza mu mtima mwanga kuti ndikhale wanzeru,” koma nzeruyo inanditalikira.
24 Elle était plus loin encore qu'auparavant; l'abîme entre nous était profond: qui le sondera?
Nzeru zimene zilipo, zili kutali ndipo ndi zozama kwambiri, ndani angathe kuzidziwa?
25 Pour moi, j'ai tourné autour de toutes choses, et j'ai appliqué mon esprit à les apprendre, à les examiner avec soin, à chercher la sagesse et la raison des choses, à connaître la démence de l'impie, et ses agitations et son inquiétude.
Kotero ndinayikapo mtima wanga kuti ndidziwe, ndifufuze ndi kumafunafuna nzeru ndi mmene zinthu zimakhalira ndipo ndinafunanso kudziwa kuyipa kwa uchitsiru ndiponso kupusa kwake kwa misala.
26 Et j'ai trouve cette démence, et je la dis plus amère que la mort; de même est la femme que le veneur poursuit comme une proie, tandis que son cœur est un filet, et qu'elle tient des chaînes en sa main. L'homme bon en face du Seigneur fuira loin d'elle, et le pécheur y sera pris.
Ndinapeza kanthu kowawa kupambana imfa, mkazi amene ali ngati khoka, amene mtima wake uli ngati khwekhwe, ndipo manja ake ali ngati maunyolo. Munthu amene amakondweretsa Mulungu adzathawa mkaziyo, koma mkaziyo adzakola munthu wochimwa.
27 Voilà ce que j'ai trouvé, dit l'Ecclésiaste, en prenant les choses une à une, pour en découvrir la raison.
Mlaliki akunena kuti, “Taonani, chimene ndinachipeza ndi ichi: “Kuwonjezera chinthu china pa china kuti ndidziwe mmene zinthu zimachitikira,
28 Mon âme l'a cherchée cette raison, et je ne l'ai point trouvée, et j'ai trouvé un homme sur mille; mais parmi toutes les femmes, je n'en ai pas trouvé une seule.
pamene ine ndinali kufufuzabe koma osapeza kanthu, ndinapeza munthu mmodzi wolungama pakati pa anthu 1,000, koma pakati pawo panalibepo mkazi mmodzi wolungama.
29 Seulement voici ce que j'ai trouvé: Dieu a créé l'homme droit, et les hommes ont cherché une multitude de raisons.
Chokhacho chimene ndinachipeza ndi ichi: Mulungu analenga munthu, anamupatsa mtima wolungama, koma anthu anatsatira njira zawozawo zambirimbiri.”

< Ecclésiaste 7 >