< Deutéronome 27 >

1 Et Moïse, avec les anciens, continua de donner des ordres à Israël, et il dit: Observez tous les commandements que je vous intime aujourd'hui.
Mose ndi akuluakulu a Israeli analamula anthu kuti, “Sungani malamulo onse amene ndikukupatsani lero lino.
2 Le jour où tu auras traversé le Jourdain pour entrer en la terre que le Seigneur ton Dieu te donne, tu dresseras pour toi de grandes pierres que tu recrépiras de chaux.
Mukawoloka mtsinje wa Yorodani kulowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, muyimiritse miyala ingapo ikuluikulu ndi kuyikulungiza.
3 Tu écriras ensuite sur ces pierres tous les articles de la loi, aussitôt que vous aurez tous franchi le Jourdain, et que vous serez entrés en la terre que le Seigneur Dieu de vos pères vous donne, terre où coulent le lait et le miel, comme le Seigneur l'a dit à vos pères.
Mulembepo mawu onse a malamulo amenewa pamene muwoloka kulowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, dziko loyenda mkaka ndi uchi, monga momwe Yehova Mulungu wa makolo anu anakulonjezerani.
4 Dès que vous aurez franchi le Jourdain, vous dresserez ces pierres dont je vous parle, sur le mont Hebal, puis vous les recrépirez de chaux,
Ndipo mukawoloka Yorodani muyimike miyala iyi pa Phiri la Ebala monga momwe ndikukulamulirani lero lino ndipo muyikulungize.
5 Et vous bâtirez au même lieu un autel au Seigneur votre Dieu, un autel de pierres, où il n'entrera point de fer.
Pamenepo mumange guwa lansembe la miyala la Yehova Mulungu wanu. Musagwiritse ntchito chida chilichonse chachitsulo pa miyalapo.
6 Vous le bâtirez de pierres sans défaut, et sur cet autel vous offrirez des holocaustes au Seigneur votre Dieu.
Mumange guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu ndi miyala yakutchire ndi kuperekerapo nsembe yopsereza kwa Yehova Mulungu wanu.
7 Vous offrirez sur cet autel les hosties pacifiques; vous mangerez, vous vous rassasierez, et vous vous réjouirez devant le Seigneur votre Dieu.
Muperekerepo nsembe zopereka za chiyanjano, muzidye ndi kukondwera pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
8 Et sur les pierres vous écrirez toute la loi, très- manifestement.
Ndipo pa miyalapo mudzalembepo mawu onse a malamulo ndi malemba akuluakulu.”
9 Et Moïse, avec les prêtres lévites, continua de parler à tout Israël, et il dit: Fais silence, écoute, Israël, aujourd'hui tu es devenu le peuple du Seigneur ton Dieu.
Kenaka Mose ndi ansembe, amene ndi Alevi anati kwa Aisraeli onse, “Khalani chete Aisraeli inu ndipo mumvetsere! Tsopano inu ndinu anthu a Yehova Mulungu wanu.
10 Et tu seras docile à la parole du Seigneur, tu exécuteras ses commandements et ses ordonnances, que je t'intime aujourd'hui.
Muzimvera Yehova Mulungu wanu ndi kutsata malamulo ake ndi malangizo ake omwe ndikukupatsani lero lino.”
11 Et ce jour-là même, Moïse donna des ordres au peuple, disant:
Tsiku lomwelo Mose analamula anthu kuti:
12 Voici ceux qui se tiendront sur le mont Garizim, après avoir passé le Jourdain, pour bâtir le peuple: Siméon, Lévi, Juda, Issachar, Joseph, Benjamin.
Mukawoloka Yorodani, mafuko awa akayimirire pa Phiri la Gerizimu ndi kudalitsa anthu: Simeoni, Levi, Yuda, Isakara, Yosefe ndi Benjamini.
13 Voici ceux qui se tiendront sur le mont Hébal, du côté de la malédiction: Ruben, Gad, Aser, Zabulon, Dan et Nephthali.
Ndipo mafuko awa akayimirire pa Phiri la Ebala ndi kutchula matemberero: Rubeni, Gadi, Aseri, Zebuloni, Dani ndi Nafutali.
14 Et les lévites, parlant à haute voix, diront à tout Israël:
Alevi adzayankhula mokweza kwa Aisraeli onse kuti:
15 Maudit soit l'homme qui fera une image sculptée ou jetée en fonte, abomination du Seigneur, ouvrage de la main d'un artisan, et qui la placera en un lieu secret; et le peuple entier répondant, dira: Ainsi soit-il.
“Ndi wotembereredwa munthu amene asema chifanizo kapena kupanga fano, ndi kuchiyika mobisa, pakuti chimenechi ndi chinthu chodetsedwa pamaso pa Yehova, ntchito za manja a anthu.”
16 Maudit celui qui n'honore pas son père ou sa mère; et tout le peuple dira: Ainsi soit-il.
“Ndi wotembereredwa munthu amene sachitira ulemu abambo ake kapena amayi ake.”
17 Maudit celui qui déplace les bornes de son voisin; et tout le peuple dira: Ainsi soit-il.
“Ndi wotembereredwa munthu amene amasuntha mwala wa malire wa mnzake.”
18 Maudit celui qui égare l'aveugle dans le chemin; et tout le peuple dira: Ainsi soit-il.
“Ndi wotembereredwa munthu amene amasocheretsa munthu wosaona pa msewu.”
19 Maudit celui qui fait dévier la justice à regard de l'étranger, de l'orphelin et de la veuve; et tout le peuple dira: Ainsi soit-il.
“Ndi wotembereredwa munthu amene sachitira chilungamo mlendo, ana amasiye kapena mkazi wamasiye.”
20 Maudit celui qui a commerce avec la femme de son père, et soulève la couverture de son père; et tout le peuple dira: Ainsi soit-il.
“Ndi wotembereredwa munthu amene agonana ndi mkazi wa abambo ake pakuti iye sachitira ulemu pogona pa abambo ake.”
21 Maudit celui qui a commerce avec une bête; et le peuple entier dira: Ainsi soit-il.
“Ndi wotembereredwa munthu amene achita chigololo ndi nyama ya mtundu uli wonse.”
22 Maudit celui qui a commerce avec la sœur de son père ou de sa mère; et le peuple entier dira: Ainsi soit-il.
“Ndi wotembereredwa munthu amene agonana ndi mlongo wake, mwana wamkazi wa abambo ake kapena mwana wamkazi wa amayi ake.”
23 Maudit celui qui a commerce avec sa fille; et tout le peuple dira: Ainsi soit-il. Maudit soit celui qui a commerce avec la sœur de sa femme; et tout le peuple dira: Ainsi soit-il.
“Ndi wotembereredwa munthu amene agonana ndi apongozi ake.”
24 Maudit celui qui frappe son prochain dans une embuscade; et tout le peuple dira: Ainsi soit-il.
“Ndi wotembereredwa munthu amene apha mnzake mwachinsinsi.”
25 Maudit soit celui qui acceptera des présents pour condamner à mort et verser le sang innocent; et tout le peuple dira: Ainsi soit-il.
“Ndi wotembereredwa munthu amene alandira chiphuphu kuti aphe munthu wosalakwa.”
26 Maudit tout homme qui ne persévèrera pas en tous les articles de cette loi, pour les mettre en pratique; et tout le peuple dira: Ainsi soit-il.
“Ndi wotembereredwa aliyense amene sachita kapena sasunga mawu a malamulo awa.”

< Deutéronome 27 >