< Daniel 6 >

1 Et il plut à Darius d'instituer cent vingt satrapes pour être en tout son royaume;
Kunamukomera Dariyo kusankha akalonga 120 kuti alamulire mu ufumu wonse,
2 Et au-dessus d'eux, trois gouverneurs, dont l'un fut Daniel, pour que les satrapes leur rendissent compte, et que lui-même n'en fût pas surchargé.
ndikusankha nduna zazikulu zitatu kuti ziwayangʼanire ndipo imodzi mwa ndunazo anali Danieli. Akalongawo amayangʼaniridwa ndi nduna zazikuluzo kuti zinthu za mfumu zisawonongeke.
3 Et Daniel fut au-dessus d'eux, parce qu'il y avait en lui un esprit supérieur, et le roi le mit à la tête de tout son royaume.
Tsono Danieli anadzionetsa kuti akhoza kugwira ntchito bwino kopambana nduna zinzake chifukwa anali wanzeru kwambiri. Ndiye mfumu inaganiza zomuyika kuti akhale woyangʼanira ufumu wonse.
4 Or les autres gouverneurs et les satrapes s'efforcèrent de trouver un sujet d'accusation contre Daniel, et ils ne purent trouver contre lui ni grief, ni délit, ni soupçon, parce qu'il était fidèle.
Chifukwa cha ichi, anzake ndi akalonga anayesa kupeza zifukwa zomutsutsira Danieli pa kayendetsedwe ka ntchito za dzikolo, koma sanapeze cholakwa chilichonse. Iwo sanapeze chinyengo mwa iye, chifukwa anali wokhulupirika ndipo sankachita chinyengo kapena kutayirira ntchito.
5 Et les gouverneurs se dirent: Nous ne trouverons pas de sujet d'accusation contre Daniel, sinon à cause des lois de son Dieu.
Pomaliza, anthu awa ananena kuti, “Sitidzapeza cholakwa chilichonse chomutsutsira Danieli kupatula chokhacho chimene chikhudza chipembedzo cha Mulungu wake.”
6 Alors les gouverneurs et les satrapes comparurent devant le roi, et lui dirent: Ô roi Darius, vis à jamais!
Choncho akalonga ndi nduna pamodzi anapita kwa mfumu ndipo anati: “Inu mfumu Dariyo, mukhale ndi moyo wautali!
7 Tous les officiers de ton royaume, généraux et satrapes, magistrats et intendants, ont tenu conseil pour qu'il fût rendu un édit royal, et formellement ordonné que tout homme qui durant trente jours fera une demande soit à un dieu, soit à un homme autre que le roi, sera jeté dans la fosse aux lions.
Nduna zoyendetsa ufumu wanu, aphungu, akalonga ndi abwanamkubwa tonse tagwirizana kuti inu mfumu mukhazikitse lamulo ndi kulisindikiza kuti aliyense amene apemphera kwa mulungu wina kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, pa masiku makumi atatu otsatirawa, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango.
8 Maintenant, ô roi, rends l'édit, et publie-le, afin que rien ne soit changé à ce qu'ont résolu les Perses et les Mèdes.
Tsopano inu mfumu khazikitsani lamulo limeneli ndipo musindikizepo dzina lanu kuti lisasinthike monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sasinthidwa.”
9 Et le roi Darius fit publier l'édit.
Choncho mfumu Dariyo anasindikizapo dzina lake pa lamuloli.
10 Or Daniel, aussitôt qu'il sut ce que prescrivait l'édit, entra dans sa maison, à l'étage supérieur, les fenêtres ouvertes; tourné vers Jérusalem, trois fois par jour il se mit à genoux, priant son Dieu, et lui rendant grâces, comme il avait coutume de le faire auparavant.
Danieli atamva kuti lamulo lasindikizidwa, anapita ku nyumba kwake nalowa mʼchipinda chapamwamba chimene mazenera ake anali otsekula kuloza ku Yerusalemu. Katatu pa tsiku iye ankagwada pansi pa mawondo ndipo amapemphera, kuyamika Mulungu wake, monga momwe ankachitira kale.
11 Cependant ces hommes l'épièrent, et ils surprirent Daniel rendant grâces à son Dieu et lui faisant sa prière.
Ndipo anthu awa anapita pamodzi ndi kukapeza Danieli akupemphera ndi kupempha Mulungu wake kuti amuthandize.
12 Et s'approchant du roi, ils lui dirent: Ô roi, n'as-tu point rendu cet édit, que tout homme qui, durant trente jours, fera une demande à un dieu ou à un homme autre que le roi, soit jeté dans la fosse aux lions? Et le roi répondit: Ce que vous dites est véritable, et l'édit des Perses et des Mèdes ne sera pas violé.
Kotero iwo anapita kwa mfumu ndipo anayankhula naye za lamulo lake kuti, “Kodi simunasindikize lamulo lakuti pa masiku makumi atatu otsatirawa aliyense amene apemphera kwa mulungu wina aliyense kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango?” Mfumu inayankha kuti, “Lamulo lilipobe monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sangathe kusinthika.”
13 Et ils reprirent, disant au roi: Daniel, l'un des fils des captifs de la Judée, ne s'est point soumis à ton édit, et trois fois par jour il demande à son Dieu ce qu'il veut lui demander.
Kenaka iwo anati kwa mfumu, “Danieli, amene ndi mmodzi mwa akapolo ochokera ku Yuda, sakulabadira inu mfumu, kapena lamulo limene munasindikizapo dzina lanu lija. Iye akupempherabe katatu pa tsiku.”
14 Aussitôt que le roi eut oui ces paroles, il en fut fort contristé, et il fut combattu par le désir de sauver Daniel, et jusqu'au soir il fut combattu par le désir de le sauver.
Mfumu itamva izi, inavutika kwambiri mu mtima mwake. Iyo inayesa kupeza njira yopulumutsira Danieli. Iyo inachita chotheka chilichonse kufikira kulowa kwa dzuwa kuti imupulumutse.
15 Mais ces hommes dirent à Darius: Sache, ô roi, qu'il est réglé chez les Mèdes et les Perses que nul changement ne peut être fait à un édit, à un décret du roi.
Ndipo anthuwo anapita pamodzi kwa mfumu ndipo anati kwa iye, “Kumbukirani, inu mfumu kuti monga mwa lamulo la Amedi ndi Aperezi, palibe chimene mfumu inalamulira kapena kukhazikitsa chimasinthidwa.”
16 Et le roi donna ses ordres, et l'on emmena Daniel, et on le jeta dans la fosse aux lions, et le roi dit à Daniel: Ton Dieu que tu sers avec constance, lui-même te délivrera.
Choncho mfumu inalamula, ndipo anabwera naye Danieli ndi kukamuponya mʼdzenje la mikango. Mfumu inati kwa Danieli, “Mulungu wako amene umutumikira nthawi zonse, akupulumutse!”
17 Et l'on apporta une pierre, et on la posa sur l'ouverture de la fosse, et le roi la scella de son anneau et de l'anneau de ses grands, afin que rien concernant Daniel ne fût changé.
Anatenga mwala natseka pa khoma pa dzenje la mikango, ndipo mfumu inadindapo chizindikiro chake ndi cha nduna zake kuti wina asasinthepo kanthu pa za Danieli.
18 Et le roi rentra dans son palais; mais il se coucha sans avoir soupé; on ne lui présenta point d'aliments, et le sommeil s'éloigna de lui. Et Dieu ferma la gueule des lions, et ils ne firent aucun mal à Daniel.
Kenaka mfumu inabwerera ku nyumba yake ndipo inakhala usiku wonse osadya kanthu, osalola chosangalatsa chilichonse. Ndipo sinagone tulo.
19 Et le roi se leva de grand matin, dès les premières lueurs du jour, et il alla en toute hâte à la fosse aux lions.
Mʼbandakucha, mfumu inanyamuka ndi kufulumira kupita ku dzenje la mikango lija.
20 Et, quand il fut près de la fosse, il cria à haute voix: Daniel, serviteur du Dieu vivant, ton Dieu, que tu sers avec constance, a-t-il pu te sauver de la gueule des lions?
Itayandikira pa dzenjelo, inayitana Danieli moonetsa nkhawa, “Danieli, mtumiki wa Mulungu wa moyo! Kodi Mulungu wako, amene umutumikira nthawi zonse, wakulanditsa ku mikango?”
21 Et Daniel dit à Darius: Roi, vis à jamais
Danieli anayankha kuti, “Inu mfumu mukhale ndi moyo wautali!
22 Mon Dieu m'a envoyé son ange, et il a fermé la gueule des lions, et ils ne m'ont fait aucun mal, parce qu'à ses yeux j'ai été trouvé juste, et qu'à ton égard, ô roi, je n'ai fait aucune offense.
Mulungu wanga anatumiza mngelo wake, ndipo anatseka pakamwa pa mikango. Iyo sinandivulaze chifukwa Mulungu anaona kuti ndine wosalakwa ndi kutinso sindinakulakwireni inu mfumu.”
23 À ces mots le roi fut extrêmement réjoui, et il ordonna de retirer Daniel de la fosse, et il fut trouvé sain et sauf, parce qu'il avait mis sa confiance en Dieu.
Mfumu inali ndi chimwemwe chopambana ndipo inalamulira kuti amutulutse Danieli mʼdzenjemo. Ndipo atamutulutsa Danieli mʼdzenjemo, sanapezeke ndi chilonda chilichonse pa thupi lake, chifukwa iye anadalira Mulungu wake.
24 Et le roi donna ses ordres, et l'on amena les hommes qui avaient accusé Daniel, et on les jeta dans la fosse aux lions, eux, leurs fils et leurs femmes; et avant qu'ils eussent touché le fond de la fosse, les lions s'en emparèrent et leur broyèrent tous les os.
Mwa lamulo la mfumu, anthu onse amene ananeneza Danieli aja anagwidwa ndi kukaponyedwa mʼdzenje la mikango, pamodzi ndi akazi awo ndi ana awo. Ndipo asanafike pansi pa dzenjelo, mikango inawawakha ndi mphamvu ndi kuteketa mafupa awo onse.
25 Alors le roi Darius écrivit à tous les peuples, aux tribus, aux hommes de toutes langues, à tous les habitants de la terre: Que la paix se multiplie parmi vous!
Kenaka mfumu Dariyo inalembera anthu a mitundu yonse, ndi anthu a ziyankhulo zosiyanasiyana a mʼdziko lonse kuti, “Mtendere uchuluke pakati panu!
26 Le présent édit est rendu par moi pour toutes les principautés de mon royaume, afin que chacun soit plein de crainte et de tremblement devant la force du Dieu de Daniel; car lui seul est le Dieu vivant, et il demeure dans tous les siècles, et son royaume ne périra jamais, et son règne durera jusqu'à la fin des temps.
“Ndikukhazikitsa lamulo kuti paliponse mʼdziko langa anthu ayenera kuopa ndi kuchitira ulemu Mulungu wa Danieli.
27 Il protège et il sauve, et il fait des signes et des miracles dans le ciel et sur la terre; c'est lui qui a tiré Daniel de la griffe des lions.
Iye amalanditsa ndipo amapulumutsa,
28 Et Daniel vécut plein de prospérité, sous le règne de Darius et sous le règne de Cyrus le Perse.
Choncho Danieli anapeza ufulu pa nthawi ya ulamuliro wa Dariyo ndi ulamuliro wa Koresi wa ku Perisiya.

< Daniel 6 >