< 2 Rois 9 >

1 Alors, le prophète Elisée appela l'un des fils des prophètes, et il lui dit Ceins-toi les reins; prends en tes mains cette fiole d'huile, et va à Ramoth- Galaad.
Mneneri Elisa anayitanitsa mmodzi mwa ana a aneneri, namuwuza kuti, “Manga lamba mʼchiwuno mwako, tenga botolo la mafuta mʼdzanja lako ndipo upite ku Ramoti Giliyadi.
2 Entre, et tu verras Jéhu, fils de Josaphat fils de Namsi; tu iras auprès de lui et tu l'emmèneras du milieu de ses frères, en un lieu retiré de ses appartements.
Ukakafika kumeneko, ukafunefune Yehu mwana wa Yehosafati, mwana wa Nimisi. Ukapite kwa iye, ukamuchotse pakati pa anzake ndi kukamulowetsa mʼchipinda chamʼkati.
3 Et tu prendras la fiole d'huile; tu la lui verseras sur la tête, et tu diras: Voici ce que dit le Seigneur: Je t'ai sacré roi d'Israël; cela dit, tu ouvriras la porte, et tu partiras rapidement sans t'arrêter.
Ndipo ukatenge botololi ndi kuthira mafuta pa mutu wake ndipo ukanene kuti, ‘Yehova akuti, Ine ndikudzoza iwe kukhala mfumu ya Israeli.’ Kenaka ukatsekule chitseko ndi kuthawa ndipo usakachedwe!”
4 Et le jeune prophète alla en Ramoth-Galaad.
Choncho mneneri wachinyamatayo anapita ku Ramoti Giliyadi.
5 Il entra, il vit les chefs de l'armée assis ensemble, et il dit: Un mot à toi, chef. Jéhu demanda: Auquel de nous? Il répondit: A toi, chef,
Atafika ku Giliyadiko anapeza atsogoleri a ankhondo ali pa msonkhano. Iye anati, “Mtsogoleri, ine ndili ndi uthenga wanu.” Ndipo Yehu anafunsa kuti, “Uthengawo ndi wa yani pakati pathu?” Mneneriyo anayankha kuti, “Ndi wa inuyo, mtsogoleri.”
6 Et Jéhu se leva, et ils allèrent à l'intérieur de la maison; là, le prophète lui versa l'huile sur la tête, et lui dit: Voici ce que dit le Seigneur Dieu d'Israël: Je t'ai sacré roi du peuple du Seigneur, roi d'Israël.
Yehu anayimirira nakalowa mʼnyumba. Pamenepo mneneriyo anakhuthulira mafuta pamutu pa Yehu ndipo ananena kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndikukudzoza kukhala mfumu ya Israeli, anthu a Yehova.
7 Et tu extermineras de devant ma face la maison d'Achab, ton maître; tu vengeras le sang des prophètes, mes serviteurs, et le sang de tous mes serviteurs qu'a répandu la main de Jézabel,
Uyenera kuwononga nyumba ya mbuye wako Ahabu ndipo ndidzabwezera imfa ya atumiki anga, aneneri ndiponso imfa ya atumiki ena onse a Yehova amene anaphedwa ndi Yezebeli.
8 Et celui qu'a répandu toute la maison d'Achab; tu extermineras tout mâle de la maison d'Achab, tout ce qui se tient enfermé et survit en Israël.
Banja lonse la Ahabu lidzatheratu. Ndidzachotsa munthu aliyense wamwamuna wa banja la Ahabu kaya ndi kapolo kapena mfulu.
9 Et je traiterai la maison d'Achab comme celle de Jéroboam, fils de Nabat, comme celle de Baasa, fils d'Achias,
Ndidzachititsa kuti banja la Ahabu lifanane ndi banja la Yeroboamu mwana wa Nebati ndiponso ngati banja la Baasa mwana wa Ahiya.
10 Et les chiens dévoreront Jézabel dans le champ de Jezraël, et il n'y aura personne qui l'ensevelisse. Puis, le prophète ouvrit la porte et s'enfuit.
Kunena za Yezebeli, agalu adzamudya ku dera la Yezireeli ndipo palibe amene adzamuyike mʼmanda.’” Kenaka mneneriyo anatsekula chitseko nʼkuthawa.
11 Jéhu revint auprès des serviteurs de son maître, et ils lui dirent: Tout va bien. Pourquoi cet épileptique est-il venu te trouver? Il leur répondit: Vous connaissez l'homme et son bavardage?
Yehu atatuluka kupita kumene kunali atsogoleri anzake, mmodzi mwa iwo anamufunsa kuti, “Kodi zonse zili bwino? Kodi munthu wamisala uja anabwera kudzatani kwa iwe?” Yehu anayankha kuti, “Iwe ukumudziwa munthu uja ndiponso ukudziwa zomwe amayankhula.”
12 Mais ils dirent: Nullement, raconte-nous-le donc. Alors, Jéhu leur dit: Il m'a parlé de telle et de telle manière, ajoutant: Voici ce que dit le Seigneur: Je t'ai sacré roi d'Israël.
Atsogoleri aja anati, “Ukunama! Tiwuze.” Yehu anati, “Zimene wandiwuza ndi izi: ‘Yehova akuti: Ine ndakudzoza iwe kukhala mfumu ya Israeli.’”
13 Dès qu'ils l'eurent ouï, ils s'empressèrent; chacun ôta son manteau et le mit sous les pieds de Jéhu au faîte des degrés; puis, ils sonnèrent du cor, et ils dirent: Jéhu est roi.
Atsogoleri aja mofulumira anatenga zofunda zawo naziyala pansi pa makwerero kuti Yehu akhalepo. Kenaka analiza lipenga, nafuwula kuti, “Yehu ndiye mfumu!”
14 Ainsi, Jéhu, fils de Josaphat, fils de Namsi, se révolta contre Joram. Alors, Joram défendait Ramoth-Galaad, avec tout Israël, contre Azaël, roi de Syrie.
Choncho Yehu mwana wa Yehosafati, mwana wa Nimisi, anachitira chiwembu Yoramu. (Nthawi imeneyi nʼkuti Yoramu ndi Aisraeli onse akuteteza Ramoti Giliyadi kwa Hazaeli mfumu ya ku Aramu,
15 Et le roi Joram était revenu à Jezraël pour se guérir des blessures que les Syriens lui avaient faites quand il avait combattu Azaël, roi de Syrie. Et Jéhu dit aux siens: Si votre âme est avec moi, ne laissez sortir de la ville personne qui puisse aller tout dire à Jezraël.
koma nʼkuti Yoramu atabwerera ku Yezireeli kuti akachire mabala amene Aaramu anamuvulaza pa nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya ku Aramu.) Yehu anati, “Ngati mukugwirizana nazo zimenezi, wina aliyense asatuluke mu mzinda muno kupita kukafotokoza nkhaniyi ku Yezireeli.”
16 Ensuite, Jéhu monta à cheval, partit, et descendit à Jezraél, où le roi Joram était à panser les blessures que lui avaient faites les flèches des archers syriens quand il avait combattu Azaël, roi de Syrie; car il était vaillant et plein de force. Et Ochozias, roi de Juda, était venu voir Joram.
Pamenepo Yehu anakwera galeta lake, napita ku Yezireeli, chifukwa Yoramu anali akupumula kumeneko ndipo Ahaziya, mfumu ya ku Yuda, nʼkuti ali komweko kudzamuona.
17 Et une sentinelle montée sur la tour de Jezraël, vit la poussière que soulevait Jéhu en approchant; et elle dit: Je vois de la poussière. A quoi Joram répondit: Prends un cavalier; fais-le partir au-devant d'eux; qu'il demande: Est-ce la paix?
Mlonda amene ankayimirira pa nsanja yolondera mzinda wa Yezireeli ataona gulu lankhondo la Yehu likuyandikira, anafuwula kuti, “Ndikuona gulu lankhondo likubwera.” Yoramu analamula kuti, “Peza munthu wokwera kavalo, mutume kuti akakumane nawo ndi kuwafunsa kuti, ‘Kodi mukubwera mwamtendere?’”
18 Et un cavalier partit à leur rencontre, et il dit: Voici ce que dit le roi: Est-ce la paix? Jéhu répliqua: Qu'y a-t-il entre toi et la paix? Va te joindre à ceux qui me suivent. Cependant, la sentinelle fit ce rapport: Le messager est allé jusqu'à eux, et il n'est point revenu.
Choncho munthu wokwera kavalo anapita kukakumana ndi Yehu ndipo anati, “Mfumu ikufunsa kuti, ‘Kodi mukubwera mwamtendere?’” Yehu anayankha kuti, “Kodi iwe nkhani ya mtendere yakukhudza bwanji? Tiye, zinditsata pambuyo panga.” Mlonda uja anakafotokoza kwa mfumu kuti, “Wamthenga uja wakafika kwa anthuwo koma sakubwerera.”
19 Et elle envoya un second messager; celui-ci arriva près d'eux, et il dit: Voici ce que dit le roi: Est-ce la paix? Jéhu répliqua: Qu'y a-t-il entre toi et la paix? Va te joindre à ceux qui me suivent.
Choncho mfumu inatumanso munthu wina wachiwiri wokwera kavalo. Atafika kwa anthuwo iye anati, “Mfumu ikufunsa kuti, ‘Kodi mukubwera mwamtendere?’” Yehu anayankha kuti, “Kodi iwe nkhani ya mtendere yakukhudza bwanji? Tiye, zinditsata pambuyo panga.”
20 L'homme en sentinelle fit derechef ce rapport: Il est allé jusqu'à eux, et il n'est point revenu; le chef paraît être Jéhu, fils de Namsi; car il marche comme un furieux.
Mlonda uja anakanenanso kuti, “Wamthenga uja wakafika kwa anthuwo koma sakubwereranso. Kuyendako kukukhala ngati kwa Yehu mwana wa Nimisi, iye amayenda ngati munthu wamisala.”
21 Et Joram dit: Qu'on attelle. On attela son char; et Joram, roi d'Israël, sortit avec Ochozias, roi de Juda, chacun sur son char; ils allèrent à la rencontre de Jéhu, et ils le trouvèrent dans le champ de Naboth le Jezraélite.
Yoramu analamula kuti, “Konzani galeta langa.” Ndipo atakonza galeta lake, Yoramu mfumu ya Israeli ndi Ahaziya mfumu ya ku Yuda anakwera nʼkutuluka mu mzindamo, aliyense atakwera galeta lake, kukakumana ndi Yehu. Iwo anakumana ndi Yehu pa munda umene unali wa Naboti, wa ku Yezireeli.
22 Dès que Joram vit Jéhu, il s'écria: Est-ce la paix, Jéhu? Jéhu répondit: Quoi! la paix! quand Jézabel, ta mère, multiplie ses débauches et ses sortilèges?
Yoramu ataona Yehu anafunsa kuti, “Yehu, kodi wabwera mwamtendere?” Yehu anayankha kuti, “Pangakhale bwanji mtendere pamene zopembedza mafano zonse zilipo ndiponso ufiti wa amayi ako Yezebeli uli ponseponse?”
23 Alors, Joram tourna bride, s'enfuit, et dit au roi de Juda Trahison! Ochozias.
Yoramu anatembenuka, nathawa akufuwula kwa Ahaziya kuti, “Ahaziya, anthuwa atiwukira!”
24 Mais Jéhu tendit son arc avec force, et il atteignit Joram entre les épaules; la flèche lui traversa le cœur, et il s'affaissa sur ses genoux.
Pamenepo Yehu anakoka uta wake ndipo analasa Yoramu kumsana pakati pa mapewa. Muviwo unakalasa mtima wake ndipo anagwa pansi mʼgaleta lakelo.
25 Puis, Jéhu dit à Badecar, son lieutenant: Jette-le dans le champ de Naboth le Jezraélite; car je me souviens, et tu te souviens aussi, que, quand nous étions sur un char à la suite d'Achab, son père, le Seigneur a prononcé cette sentence:
Yehu anawuza Bidikara, mtsogoleri wa galeta lake kuti, “Munyamule ndipo ukamuponye mʼmunda umene unali wa Naboti wa ku Yezireeli, chifukwa kumbukira mmene iwe ndi ine tinkayenda pambuyo pa Ahabu abambo ake, kuti Yehova ananeneratu za iye kuti,
26 Si je n'avais point vu hier le sang de Naboth et le sang de ses fils! dit le Seigneur; mais je les vengerai dans ce champ même, dit le Seigneur. Maintenant, prends-le et jette-le dans le champ, selon la parole du Seigneur.
‘Zoonadi dzulo ndinaona magazi a Naboti ndi magazi a ana ake, akutero Yehova, ndipo Ine ndidzakubwezera ndithu choyipa chimenechi pa munda womwe uno, akutero Yehova.’ Tsono munyamule ndipo ukamuponye mʼmundamo, potsatira zimene Yehova ananena.”
27 Et Ochozias, roi de Juda, vit tout, et il prit la fuite par le chemin de Bethgan; Jéhu le poursuivit, et il dit: Tuez aussi celui-là. L'un de ses gens le frappa sur son char comme il montait en Haï (la même que Jéblaam). Et Ochozias se réfugia dans Mageddo, où il mourut.
Ahaziya mfumu ya ku Yuda ataona zimene zinachitika, anathawira ku Beti Hagani. Yehu anamuthamangitsa, uku akufuwula kuti, “Mupheninso!” Iwo anamuvulaza ali mʼgaleta lakelo pa njira yopita ku Guri pafupi ndi Ibuleamu, koma iye anathawira ku Megido ndipo anakafera kumeneko.
28 Ses serviteurs le placèrent sur son char; ils le ramenèrent à Jérusalem, et ils l'ensevelirent dans son sépulcre en la ville de David.
Antchito ake anamunyamulira mʼgaleta kupita naye ku Yerusalemu ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide.
29 Ochozias était devenu roi de Juda, la onzième année du règne de Joram en Israël.
(Mʼchaka cha khumi ndi chimodzi cha ufumu wa Yoramu mwana wa Ahabu, Ahaziya anakhala mfumu ya ku Yuda).
30 Ensuite, Jéhu entra dans Jezraël; Jézabel l'ouït, elle se farda le tour des yeux, orna sa tête, et se pencha à sa fenêtre.
Kenaka Yehu anapita ku Yezireeli. Yezebeli atamva zimene zinachitika, anapaka zodzikometsera mʼmaso, naluka tsitsi lake, namasuzumira pa zenera.
31 Quand Jéhu passa, elle lui cria: Zambri s'est-il bien trouvé d'avoir tué son maître?
Pamene Yehu ankalowa pa chipata iye anafunsa kuti, “Kodi wabwera mwamtendere, iwe Zimuri, munthu wopha mbuye wako?”
32 Il leva les yeux vers sa fenêtre; il la vit, et il dit: Qui es-tu? Descends auprès de moi. Or, il y avait là deux eunuques qui se penchèrent vers lui.
Yehu anakweza maso nayangʼana pa zenera, ndipo anafuwula kuti, “Kodi ndani ali mbali yanga? Ndani?” Anthu ofulidwa awiri kapena atatu anayangʼana Yehu pansipo.
33 Jéhu leur dit: Jetez-la par la fenêtre. Et ils la jetèrent; son sang jaillit sur les murs et sur les chevaux, et les chevaux la foulèrent aux pieds.
Yehu anawawuza kuti, “Muponyeni pansi!” Motero anamuponya pansi ndipo magazi ake ena anafalikira pa khoma ndi pa akavalo pamene ankamupondaponda.
34 Ensuite, Jéhu entra dans le palais; il mangea et il but; puis, il dit: Allez voir cette maudite, et ensevelissez-la, car c'est une fille de roi.
Yehu analowa mʼnyumba yaufumu ndipo anadya ndi kumwa. Kenaka iye anati, “Kamutoleni mkazi wotembereredwayo, ndipo kamuyikeni mʼmanda, popeza ndi mwana wa mfumu.”
35 Et ses gens sortirent pour l'inhumer; mais ils ne trouvèrent plus rien d'elle que le crâne, les pieds et les paumes des mains.
Koma atapita kuti akamuyike mʼmanda, sanapeze kanthu kupatula chibade cha mutu wokha, mapazi ake ndi manja ake.
36 Ils rentrèrent; ils lui en firent le rapport, et il dit: C'est la parole du Seigneur qu'il a dite par Elie le Thesbite, disant: Dans les champs de Jezraël, les chiens dévoreront les chairs de Jézabel.
Choncho iwo anabwerera kwa Yehu ndi kukamufotokozera kuti, “Mawu amene Yehova anayankhula kudzera mwa mtumiki wake Eliya wa ku Tisibe ndi awa: Pa munda wa ku Yezireeli agalu adzadya mtembo wa Yezebeli.
37 Et son cadavre sera comme du fumier sur la surface du champ de Jezraël, et nul ne pourra dire: C'est Jézabel.
Mtembo wa Yezebeli udzakhala ngati zinyalala pa munda wa ku Yezireeli, kotero kuti palibe amene adzathe kunena kuti, ‘Uyu ndi Yezebeli.’”

< 2 Rois 9 >