< 2 Rois 25 >

1 Dans la neuvième année de son règne, le dixième mois, le roi Nabuchodonosor arriva de Babylone avec toute son armée contre Jérusalem; il campa autour de ses remparts, et il les enveloppa d'une muraille qu'il bâtit.
Choncho mʼchaka chachisanu ndi chinayi cha ulamuliro wa Zedekiya, mwezi wakhumi, pa tsiku lakhumi la mwezi, Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anabwera ndi gulu lake lonse la ankhondo, nadzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu. Iye anamanga misasa kunja kwa mzindawo ndipo anamanga mitumbira ya nkhondo kuzungulira mzindawo.
2 Et la ville fut investie jusqu'au neuvième mois de la onzième année du règne de Sédécias.
Mzindawo anawuzinga mpaka chaka cha khumi ndi chimodzi cha Mfumu Zedekiya.
3 La famine prévalait dans la cité, et il n'y avait pas de pains pour le peuple de la terre.
Pa tsiku lachisanu ndi chinayi pa mwezi wachinayi, njala inakula kwambiri mu mzindamo kotero kuti anthu analibe chakudya.
4 Une brèche fut faite aux murailles, et à la nuit les hommes de guerre sortirent par le chemin de la porte qui est entre les remparts, la porte même du jardin du roi; cependant, les Chaldéens entouraient le reste de la ville. Alors, le roi prit la route de la plaine.
Pamenepo khoma la mzindawo linabowoledwa ndipo gulu lonse la ankhondo linathawa usiku kudzera pa chipata cha pakati pa makoma awiri pafupi ndi munda wa mfumu, ngakhale kuti Ababuloni anali atazinga mzindawo. Iwo anathawira cha ku Araba,
5 Et l'armée des Chaldéens les poursuivit; Sédécias fut pris en Araboth-Jéricho, et toute sa troupe se dispersa tout alentour.
koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola mfumu Zedekiya ndi kumupeza mʼchigwa cha ku Yeriko. Ankhondo onse anamusiya yekha nabalalika.
6 Les Chaldéens firent donc le roi captif; ils le menèrent au roi de Babylone à Reblatha, et Nabuchodonosor prononça contre lui son arrêt.
Anagwidwa napita naye kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula, kumene anagamula mlandu wa Zedekiyayo.
7 Il égorgea tous ses fils sous ses yeux, qu'ensuite il arracha; puis, après l'avoir chargé de chaînes et d'entraves, il l'emmena à Babylone.
Iwo anapha ana a Zedekiya iyeyo akuona. Kenaka anakolowola maso a Zedekiya namumanga ndi unyolo wamkuwa ndi kupita naye ku Babuloni.
8 Le septième jour du cinquième mois de la dix-neuvième année du règne de Nabuchodonosor, Nabuzardan son général en chef, celui qui se tenait devant lui, marcha sur Jérusalem.
Mwezi wachisanu, pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi, mʼchaka cha 19 cha Nebukadinezara, mfumu ya Babuloni, Nebuzaradani, mkulu wa asilikali oteteza mfumu, nduna ya mfumu ya Babuloni, anabwera ku Yerusalemu.
9 Et il livra aux flammes le temple du Seigneur, le palais du roi et toutes les maisons de Jérusalem;
Iye anatentha Nyumba ya Yehova, nyumba ya mfumu pamodzi ndi nyumba zonse za mu Yerusalemu. Anatentha nyumba iliyonse yofunika.
10 Le général en chef [brûla tout].
Gulu lonse la ankhondo la ku Babuloni limene linali ndi mkulu wa asilikali oteteza mfumu ija, linagumula malinga ozungulira Yerusalemu.
11 Et Nabuzardan enleva tout ce qui survivait du peuple demeuré dans la ville, et ceux qui étaient tombés dans les mains du roi de Babylone, et tout le reste de la multitude.
Nebuzaradani mkulu wa asilikali uja anatenga anthu amene anatsala mu mzindamo, ndi ena amene anathawira kwa mfumu ya Babuloni, pamodzi ndi ena onse kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
12 Il ne laissa pour être vignerons et laboureurs que la plus infinie populace.
Koma mkulu wa asilikaliyo anasiya anthu ena osauka kwambiri mʼdzikomo kuti azisamalira minda ya mpesa ndi minda ina.
13 Et les Chaldéens brisèrent les colonnes d'airain, les bassins et la mer d'airain du temple; et ils emportèrent le métal à Babylone.
Ababuloni anaphwanya zipilala zamkuwa, maphaka ndiponso mbiya ya mkuwa zimene zinali mʼNyumba ya Yehova ndipo anatenga mkuwawo napita nawo ku Babuloni.
14 Ils prirent aussi les chaudières, les fourchettes, les coupes, les encensoirs et les vases d'airain employés dans le temple.
Iwo anatenganso miphika, mafosholo, mbaniro za nyale, mbale ndi ziwiya zonse zamkuwa zimene ankagwiritsa ntchito potumikira mʼNyumbayo.
15 Le général en chef prit les portes, les coupes d'or et d'argent,
Mkulu wa asilikali uja anatenganso zofukizira lubani ndi mbale zowazira magazi. Zonsezi zinali zopangidwa ndi golide wabwino kwambiri kapena siliva.
16 Les deux colonnes, la mer et les bassins que Salomon avait placés dans le temple; on ne sut pas le poids de tous les ornements d'airain.
Mkuwa wochokera ku zipilala ziwiri zija, mbiya ija ndi maphaka aja, zimene Solomoni anapanga mʼNyumba ya Yehova, kuchuluka kwake kunali kosawerengeka.
17 Chaque colonne avait dix-huit coudées de haut; elle était surmontée d'un chapiteau d'airain, haut de trois coudées, avec un filet entouré de grenades; elles étaient toutes les deux pareilles.
Chipilala chilichonse chinali chotalika mamita asanu ndi atatu. Mutu wa mkuwa umene unali pamwamba pa chipilalacho unali mita imodzi ndi theka ndipo unakongoletsedwa ndi ukonde wa makangadza a mkuwa amene anazungulira mutuwo. Chipilala chachiwiri chinali chofanana ndi chinacho, ndipo chinali ndi ukonde.
18 Le général en chef fit aussi captifs Saraïas le grand prêtre, Sophonie prêtre du second rang, et les trois gardiens des portes.
Mkulu wa asilikali uja anagwira ukapolo mkulu wa ansembe Seraya, Zefaniya wachiwiri wa mkulu wa ansembe ndi alonda atatu apakhomo.
19 On prit en outre: hors de la ville, un eunuque commandant les hommes de guerre; dans la ville, cinq de ceux qui voyaient la face du roi, et le scribe du chef de l'armée qui rangeait les troupes en bataille, et soixante hommes de la campagne alors à Jérusalem.
Mwa anthu amene anali mu mzindamo, anatenga mkulu amene ankalamulira ankhondo ndiponso alangizi asanu a mfumu. Anatenganso mlembi wa mtsogoleri wa ankhondo amene ankalemba anthu ntchito ya usilikali mʼdzikomo pamodzi ndi anthu ake 60 amene anali mu mzindamo.
20 Nabuzardan conduisit les captifs au roi de Babylone, à Reblatha.
Nebuzaradani mkulu wa asilikali uja anawatenga onsewo napita nawo kwa mfumu ya Babuloni ku Ribula.
21 Et Nabuchodonosor les frappa, et les fit mettre à mort à Reblatha dans la terre d'Emath; puis, il emmena Juda loin de sa terre.
Ku Ribulako, mʼdziko la Hamati, mfumu ya ku Babuloni inalamula kuti awakwapule ndi kuwapha. Choncho Ayuda anatengedwa ukapolo kuwachotsa mʼdziko lawo.
22 Et à la tête du peuple qui resta sur le territoire de Juda, le roi mit Godolias, fils d'Achiman, fils de Saphan.
Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anasankha Gedaliya mwana wa Ahikamu, mwana wa Safani, kukhala woyangʼanira anthu amene anatsala ku Yuda.
23 Et tous les chefs de l'armée, eux et leurs hommes, apprirent que le roi avait choisi Godolias; alors, Ismaël, fils de Nathanie; Jonas, fils de Careth; Saraïas, fils de Thanamath le Nephthalite, et Jézonias, fils de Machathi, l'allèrent trouver avec leurs hommes à Maspha,
Atsogoleri onse ankhondo ndi anthu awo atamva kuti mfumu ya Babuloni yasankha Gedaliya kukhala bwanamkubwa, anabwera kwa Gedaliya ku Mizipa. Atsogoleriwo mayina awo anali awa: Ismaeli mwana wa Netaniya, Yohanani mwana wa Kareya, Seraya mwana wa Tanihumeti wa ku Netofa ndi Yaazaniya mwana wa Maakati, pamodzi ndi anthu awo.
24 Et Godolias prêta serment à eux et à leurs hommes, disant: Ne craignez plus d'invasion des Chaldéens, demeurez en votre terre, servez le roi de Babylone, et tout ira bien pour vous.
Gedaliya analumbira powatsimikizira iwo ndi anthu awo. Iye anati, “Musachite mantha ndi atsogoleri Ababuloniwa. Khalani mʼdziko muno ndipo tumikirani mfumu ya Babuloni. Mukatero zinthu zidzakuyenderani bwino.”
25 Et le septième mois, Ismaël, fils de Nathanie, de la race royale, et dix de ses hommes allèrent à Maspha; là, ils attaquèrent Godolias, et ils le tuèrent ainsi que les Chaldéens qui s'y trouvaient avec lui.
Koma pa mwezi wachisanu ndi chiwiri, Ismaeli mwana wa Netaniya, mwana wa Elisama, wa banja laufumu, anabwera ndi anthu khumi ndipo anapha Gedaliya pamodzi ndi Ayuda ndi anthu a ku Babuloni amene anali naye limodzi ku Mizipa.
26 Et tout le peuple, du petit au grand, et les chefs de l'armée se levèrent, et ils s'en allèrent en Égypte, car ils craignaient les Chaldéens.
Chifukwa cha zimenezi, anthu onse kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo anathawira ku Igupto chifukwa choopa Ababuloni.
27 En la trente-septième année de la captivité de Joachim, roi de Juda, le vingt-septième jour du douzième mois, Evilmerodach, roi de Babylone, dès la première année de son règne, releva la tête de Joachim, roi de Juda, et le fit sortir de prison.
Pa chaka cha 37 cha ukapolo wa Yehoyakini mfumu ya Yuda, chaka chimene Evili-Merodaki anakhala mfumu ya Babuloni, anamasula Yehoyakini mʼndende pa mwezi wa 12 pa tsiku la 27.
28 Et il lui parla avec douceur, et il lui donna un trône plus élevé que les trônes des autres rois qui l'entouraient à Babylone.
Anamukomera mtima namukweza kupambana mafumu ena onse amene anali naye ku Babuloni.
29 Il lui ôta ses vêtements de prisonnier, et il le fit manger, en sa présence, tous les jours de sa vie.
Choncho Yoyakini anavula zovala zake za ku ndende, ndipo ankadya ndi mfumu masiku onse a moyo wake.
30 Et sa portion, portion perpétuelle, lui fut donnée de la maison du roi; il en fut ainsi tous les jours de sa vie.
Mfumu inkamupatsa Yehoyakini chakudya tsiku lililonse pa moyo wake wonse.

< 2 Rois 25 >