< 2 Rois 24 >

1 En ce temps-là, Nabuchodonosor, roi de Babylone, vint, et Joacin lui fut asservi trois ans; ensuite il changea de pensée, et il refusa de lui obéir.
Pa nthawi ya ulamuliro wa Yehoyakimu, Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anadzathira nkhondo dzikolo ndipo Yehoyakimu anakhala pansi pa ulamuliro wake zaka zitatu. Koma kenaka anasintha maganizo ake nawukira Nebukadinezara.
2 Alors, le Seigneur envoya contre lui des bandes de la Chaldée, de la Syrie, de Moab et des fils d'Ammon; il les envoya en la terre de Juda pour prévaloir sur elle, selon la parole que le Seigneur avait dite par la voix de ses serviteurs les prophètes;
Yehova anatumiza magulu a Ababuloni, Aaramu, Amowabu ndi Aamoni, kudzathira nkhondo Yuda. Iye anawatumiza kudzawononga Yuda molingana ndi mawu amene Yehova ananeneratu kudzera mwa aneneri ake.
3 De plus, la colère du Seigneur contre Juda voulait l'expulser de devant sa face à cause des péchés de Manassé, et de tout ce qu'avait fait ce roi;
Ndithu, izi zinachitikira Yuda monga momwe Yehova analamulira nʼcholinga choti awachotse pamaso pake chifukwa cha machimo a Manase ndi zonse zimene anachita,
4 Car il avait versé le sang innocent, il en avait rempli Jérusalem; et le Seigneur ne voulait point s'apaiser.
kuphatikizapo kukhetsa magazi a anthu osalakwa. Chifukwa iye anadzaza Yerusalemu ndi magazi a anthu osalakwa ndipo Yehova sanafune kumukhululukira.
5 Quant au reste de l'histoire de Joacin, n'est-il pas écrit au livre des Faits et gestes des rois de Juda?
Ntchito zina za Yehoyakimu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
6 Et Joacin s'endormit avec ses pères, et son fils Joachim, régna à sa place.
Yehoyakimu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Yehoyakini mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
7 Et le roi d'Égypte ne sortit plus de sa contrée, parce que, depuis le torrent d'Égypte jusqu'à l'Euphrate, le roi de Babylone avait pris tout ce qui appartenait à l'Égyptien.
Mfumu ya Igupto sinatulukenso mʼdziko lake chifukwa mfumu ya Babuloni inalanda mayiko onse kuchokera ku Mtsinje wa ku Igupto mpaka ku Mtsinje wa Yufurate.
8 Joachim avait dix-huit ans quand il monta sur le trône, et il régna trois mois à Jérusalem; sa mère se nommait Nestha, fille d'Ellanastham, de Jérusalem.
Yehoyakini anakhala mfumu ali ndi zaka 18 ndipo analamulira mu Yerusalemu miyezi itatu. Amayi ake anali Nehusita mwana wa Elinatani wa ku Yerusalemu.
9 Et il fit le mal devant le Seigneur, comme avait fait son père.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira abambo ake.
10 En ce temps-là, Nabuchodonosor, roi de Babylone, marcha sur Jérusalem, et la ville fut investie.
Nthawi imeneyo ankhondo a Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anabwera ku Yerusalemu nazinga mzindawo ndi misasa ya nkhondo
11 Et Nabuchodonosor mit le siège devant la ville, et ses serviteurs la tinrent assiégée.
ndipo Nebukadinezara anafika ku mzindawo pamene ankhondo ake anawuzinga.
12 Or, Joachim, roi de Juda, se rendit au roi de Babylone, lui, ses serviteurs, sa mère, ses chefs et ses eunuques; le roi de Babylone le fit captif en la huitième année de son règne.
Yehoyakini mfumu ya Yuda pamodzi ndi amayi ake, atumiki ake, anthu ake olemekezeka ndiponso akuluakulu onse anadzipereka kwa mfumu ya ku Babuloni. Mfumu ya Babuloni inagwira Yoyakini ukapolo mʼchaka chachisanu ndi chitatu cha ufumu wake.
13 Et il enleva de Jérusalem tous les trésors du temple du Seigneur et tous les trésors du palais du roi; il brisa tous les vaisseaux d'or qu'avait faits, dans le temple, le roi Salomon, selon la parole du Seigneur.
Monga ananenera Yehova, Nebukadinezara anachotsa chuma chonse cha mʼNyumba ya Yehova ndiponso cha mʼnyumba ya mfumu ndipo anatenga ziwiya zonse zagolide za ku Nyumba ya Yehova zimene Solomoni mfumu ya Israeli anapanga.
14 Et il emmena en captivité, au nombre de dix mille, tous les chefs, tous les hommes vaillants, et en outre tous les charpentiers et tous les maçons; il ne resta dans la terre que les indigents.
Anatenga anthu onse a mu Yerusalemu kupita nawo ku ukapolo. Akuluakulu onse pamodzi ndi anthu ankhondo, anthu onse aluso ndi amisiri osula onse pamodzi analipo 10,000. Osauka okha ndiye anatsala mʼdzikomo.
15 Il transporta aussi à Babylone, Joachim, la mère du roi, les femmes du roi et ses eunuques; il conduisit tous les riches de la terre de Jérusalem à Babylone,
Nebukadinezara anatenga Yehoyakini ngati kapolo kupita naye ku Babuloni. Mu Yerusalemu anatenganso amayi a mfumu, akazi ake, akuluakulu ake ndiponso anthu olemekezeka mʼdzikomo.
16 Et tous les hommes dans la force de l'âge au nombre de soixante-dix mille, et mille charpentiers ou maçons, tous faisant la guerre. Le roi Nabuchodonosor les emmena captifs à Babylone.
Mfumu ya Babuloni inatumizanso ku Babuloni anthu ankhondo 70,000, anthu amphamvu ndi okonzeka kupita ku nkhondo, anthu aluso ndi amisiri osula 1,000.
17 Et il remplaça Joachim par Batthanias, fils de Josias, et il donna à ce roi le nom de Sédécias.
Iye analonga ufumu Mataniya, malume wa Yoyakini mʼmalo mwake ndipo anasintha dzina lake kuti akhale Zedekiya.
18 Sédécias avait vingt-neuf ans quand il monta sur le trône, et il régna onze ans à Jérusalem; le nom de sa mère était Amital, fille de Jérémie.
Zedekiya anakhala mfumu ali ndi zaka 21 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11. Amayi ake anali Hamutali mwana wa Yeremiya wa ku Libina.
19 Et il fit le mal devant le Seigneur, comme avait fait Joacin;
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira Yehoyakimu.
20 Car, telle était la pensée du Seigneur contre Jérusalem et contre Juda, jusqu'à ce qu'il les eut expulsés de devant sa face. Or, Sédécias se révolta contre le roi de Babylone.
Zonsezi zinachitikira Yerusalemu ndi Yuda chifukwa cha mkwiyo wa Mulungu ndipo pa mapeto pake anawachotsa pamaso pake. Ndipo Zedekiya anawukira mfumu ya Babuloni.

< 2 Rois 24 >