< 2 Rois 19 >

1 Lorsque le roi Ezéchias les eut ouïs, il déchira aussi ses vêtements, se couvrit d'un cilice, et alla au temple du Seigneur.
Mfumu Hezekiya atamva zimenezi, anangʼamba zovala zake navala chiguduli ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova.
2 Et il envoya Eliacim, et Sobna et Joas, couverts de cilices, auprès du prophète Isaïe, fils d'Amos.
Iye anatuma Eliyakimu, woyangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi ansembe akuluakulu, onse atavala ziguduli, kwa mneneri Yesaya mwana wa Amozi.
3 Et ils lui dirent: Voici ce que dit Ezéchias: Ce jour est un jour d'affliction, de reproches et de provocation; car les fils prêts à naître sont venus jusqu'aux douleurs; mais la mère, en mal d'enfant, n'a plus de force.
Iwo anamuwuza kuti, “Hezekiya akunena kuti, ‘Lero ndi tsiku lamavuto, lachilango ndi lamanyazi. Ife lero tili ngati mayi woyembekezera amene pofika nthawi yoti achire akupezeka kuti alibe mphamvu zoberekera.
4 Si, de quelque manière, le Seigneur avait ouï toutes les paroles de Rhabsacès, que le roi des Assyriens, son maître, a envoyé pour outrager le Dieu vivant, pour blasphémer par ces paroles qu'a sans doute entendues le Seigneur ton Dieu, prie donc pour ceux de nous qui restent.
Mwina Yehova Mulungu wanu adzamva mawu onse a Rabusake amene mbuye wake, mfumu ya ku Asiriya anamutuma kudzanyoza Mulungu wamoyo, ndipo Mulunguyo adzamulanga chifukwa cha mawu amene Yehova Mulungu wanu wamva. Choncho pemphererani anthu otsala amene akanali ndi moyo.’”
5 Ainsi, les serviteurs du roi Ezéchias vinrent à Isaïe.
Akuluakulu a Mfumu Hezekiya atafika kwa Yesaya,
6 Et le prophète leur dit: Dites à votre maître: Voici ce que dit le Seigneur: Ne crains pas les paroles de blasphème que tu as entendues des serviteurs du roi d'Assyrie.
Yesaya anawawuza kuti, “Kawuzeni mbuye wanu kuti, ‘Yehova akunena kuti: Usachite mantha ndi zimene wamva, mawu amene nthumwi za mfumu ya ku Asiriya zandinyoza nawo Ine.
7 Voilà que je mets en lui un esprit; il va apprendre une nouvelle, il va retourner en son royaume, et je le ferai périr, par le glaive, en son royaume.
Tamverani! Ine ndidzayika mwa mfumuyo mzimu wina kotero kuti akadzamva mphekesera ya nkhondo, adzabwerera ku dziko lake ndipo Ine ndidzachititsa kuti aphedwe ndi lupanga kwawo komweko.’”
8 Pendant ce temps, Rhabsacès, ayant ouï dire que le roi était parti de Lachis, le rejoignit à Lobna, qu'il assiégeait.
Rabusake atamva kuti mfumu ya ku Asiriya yachoka ku Lakisi, iye anabwerera mʼmbuyo ndipo anakapeza mfumu ikuchita nkhondo ndi mzinda wa Libina.
9 Alors, le roi entendit parler de Tharaca, roi d'Ethiopie; on disait: Voilà qu'il s'est mis en campagne pour te combattre. Sennachérib s'en retourna donc; il envoya des messagers à Ezéchias, disant:
Nthawi imeneyi Senakeribu analandira uthenga wakuti Tirihaka, mfumu ya ku Kusi, akubwera kudzachita naye nkhondo. Choncho iye anatumanso amithenga kwa Hezekiya ndi mawu awa:
10 Que ton Dieu, en qui tu as mis ta confiance, ne t'excite pas, en te disant: Jérusalem ne sera pas livrée aux roi des Assyriens.
“Kawuzeni Hezekiya mfumu ya Yuda kuti: Usalole kuti Mulungu amene ukumudalira akupusitse ponena kuti, ‘Yerusalemu sadzaperekedwa mʼmanja mwa mfumu ya ku Asiriya.’
11 Tu as ouï tout ce que les rois d'Assyrie ont fait à toutes les contrées en les vouant à la destruction? Et toi tu leur échapperais!
Ndithu iwe unamva chimene mafumu a Asiriya anachita ku mayiko ena onse, kuti anawawononga kotheratu. Ndipo kodi iwe nʼkupulumuka?
12 Est-ce que les dieux des nations que nos pères ont anéanties, les ont préservées? Ont-ils sauvé Gozan, et Haran, et Rhaphis et les fils d'Edem, qui habitaient Thaesthen?
Kodi milungu ya mitundu imene makolo anga anayigonjetsa, milungu ya anthu a ku Gozani, Harani, Rezefi ndi Aedeni amene anali ku Teli Asara, inawapulumutsa?
13 Où sont les rois d'Emath et d'Arphad? Où est le roi des villes de Sepharvaïm, d'Ana et d'Aba?
Kodi mafumu a Hamati, Aripadi ndi mafumu a mizinda ya Sefaravaimu, Hena ndi Iva, ali kuti?”
14 Et Ezéchias prit cette lettre de Sennachérib des mains de ses messagers, et il la lut; puis, il monta au temple du Seigneur; il la déploya devant le Seigneur.
Hezekiya analandira kalata kwa amithenga aja nayiwerenga. Pomwepo anapita ku Nyumba ya Yehova nayika kalatayo pamaso pa Yehova.
15 Et il dit: Seigneur Dieu d'Israël, qui êtes assis sur les chérubins, vous êtes le seul Dieu de tous les royaumes de la terre, vous avez créé le ciel et la terre.
Ndipo Hezekiya anapemphera kwa Yehova nati, “Inu Yehova Mulungu wa Israeli, Inu amene mumakhala pa Akerubi, Inu nokha ndinu Mulungu wolamulira maufumu onse a dziko lapansi. Inu munalenga kumwamba ndi dziko lapansi.
16 Seigneur, inclinez votre oreille, et écoutez; Seigneur, ouvrez les yeux, et voyez; soyez attentif aux paroles que Sennachérib envoie pour outrager le Dieu vivant.
Inu Yehova, tcherani khutu lanu ndipo mumve Yehova tsekulani maso anu ndipo muone, imvani mawu onse amene Senakeribu watumiza kunyoza Inu Mulungu wamoyo.
17 Il est vrai, Seigneur, que les rois des Assyriens ont dépeuplé les nations.
“Inu Yehova, nʼzoonadi kuti mafumu a Asiriya anawononga mitundu iyi ndi mayiko awo.
18 Ils ont livré leurs dieux aux flammes; car ce n'étaient pas des dieux, mais des œuvres des mains des hommes, du bois ou de la pierre; ils les ont détruits.
Iwo anaponya milungu yawo pa moto ndi kuyiwononga pakuti sinali milungu koma mitengo ndi miyala chabe, yopangidwa ndi anthu.
19 Maintenant, Seigneur notre Dieu, délivrez-nous des mains de Sennachérib, et tous les royaumes de la terre sauront que vous seul êtes le Seigneur Dieu.
Ndipo tsopano Inu Yehova Mulungu wathu, tipulumutseni ndithu mʼdzanja lake, kuti maufumu onse a dziko lapansi adziwe kuti Inu nokha, Inu Yehova, ndinu Mulungu.”
20 Et Isaïe, fils d'Amos, envoya un messager chez Ezéchias, disant: Voici ce que dit le Seigneur Dieu des armées, Dieu d'Israël: La prière que tu m'as faite au sujet de Sennachérib, roi des Assyriens, je l'ai entendue.
Ndipo Yesaya mwana wa Amozi anatumiza uthenga kwa Hezekiya wakuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndamva pemphero lako lonena za Senakeribu mfumu ya ku Asiriya.’”
21 Voici les paroles qu'a dites sur lui le Seigneur: La vierge fille de Sion t'a méprisé, et elle t'a raillé; la vierge fille de Jérusalem a secoué sur toi la tête.
Mawu amene Yehova wayankhula wotsutsana naye ndi awa: “Namwali wa Ziyoni akukunyoza ndi kukuseka iwe. Mwana wamkazi wa Yerusalemu akupukusa mutu wake kumbuyo kwako.
22 Qui donc as-tu outragé? Contre qui donc as-tu blasphémé? Contre qui donc as-tu élevé la voix et lancé tes regards hautains? C'est contre le Saint d'Israël.
Kodi iweyo wanyoza ndi kuchitira chipongwe yani? Kodi ndani amene wamufuwulira mawu ako ndi kumuyangʼana monyada? Wachitiratu izi Woyera wa Israeli!
23 Tu as outragé le Seigneur par tes messagers, et tu as dit: Avec la multitude de mes chars je suis monté sur la cime des montagnes, sur les pics du Liban; j'ai abattu ses grands cèdres et ses plus beaux cyprès; je suis venu au cœur de la forêt de chênes du Carmel.
Kudzera mwa amithenga ako wonyoza Ambuye. Ndipo wanena kuti, ‘Ndi magaleta ochuluka ndinakwera mapiri ataliatali, pa msonga za mapiri a Lebanoni. Ndigwetsa mitengo yake ya mkungudza yayitali kwambiri, mitengo yake ya payini yabwino kwambiri. Ndalowanso mʼkati mwake mwenimweni, mwa nkhalango yake yowirira kwambiri.
24 Je me suis baigné dans des eaux étrangères, j'en ai bu; et, sous la plante de mes pieds, j'ai desséché tous les fleuves, même les plus profonds.
Ndakumba zitsime ku mayiko achilendo ndipo ndinamwa madzi a kumeneko. Ndi mapazi anga ndawumitsa mitsinje yonse ya ku Igupto.’”
25 Or, c'est moi le Seigneur qui ai formé ce dessein et qui l'ai accompli; j'ai d'abord excité l'insolence de bandes étrangères habiles à combattre les villes fortifiées.
“‘Kodi sunamvepo? Zimenezi ndinazikhazikitsa kalekale. Ndinazikonzeratu masiku amakedzana; tsopano ndachita kuti zichitikedi, iwe kwako kunali kungosandutsa mizinda yotetezedwa kukhala milu ya miyala.
26 Et ceux qui les habitaient ont eu les mains énervées; ils ont tremblé, ils ont été couverts de honte. Ils sont devenus comme l'herbe des champs, comme la plante verte, comme le gazon des terrasses qu'en marchant on foule aux pieds.
Anthu a kumeneko ndi opanda mphamvu, athedwa nzeru ndipo ali ndi manyazi. Ali ngati mbewu za mʼmunda, ngati udzu wanthete, ali ngati udzu womera pa denga, umene umawuma usanakule nʼkomwe.’”
27 Je connaissais ta demeure, ton départ, ta fureur et ta rage contre moi;
“‘Koma Ine ndimadziwa kukhala kwako, kutuluka kwako ndi kulowa kwako, ndi mkwiyo wako pa Ine.
28 Tes menaces insolentes sont parvenues à mes oreilles; mais je mettrai un harpon dans tes narines et un mors à ta bouche, et je te renverrai par le chemin qu'en venant tu as pris.
Chifukwa chakuti wandikwiyira ndipo ndamva za mwano wako, ndidzakola mphuno yako ndi mbedza ndi kuyika chitsulo changa mʼkamwa mwako, ndipo ndidzakubweza pokudzeretsa njira yomwe unadzera pobwera.’
29 Pour toi, Ezéchias, voici le signe: mange cette année ce qui vient de soi-même; puis, l'année prochaine, ce qui aura poussé. En la troisième année, il y aura semence et moisson; vous replanterez vos vignes et vous mangerez leurs fruits.
“Koma iwe Hezekiya, chizindikiro chako chidzakhala ichi: “Chaka chino mudzadya tirigu wamphulumukwa, ndipo chaka chamawa mudzadya tirigu wongodzimerera. Koma chaka chachitatu mudzadzala ndi kukolola, mudzawoka mphesa ndipo mudzadya zipatso zake.
30 Et Sennachérib partit; il s'en retourna, et il ne sortit plus de Ninive.
Anthu a nyumba ya Yuda amene adzatsale adzazika mizu ndi kubereka zipatso.
31 Car il sortira un reste de Jérusalem, un débris sauvé de la montagne de Sion; et cela nous sera accordé par l'amour du Seigneur des armées.
Pakuti ku Yerusalemu kudzachokera anthu otsala, ndi ku phiri la Ziyoni kudzachokera gulu la anthu opulumuka.” “Changu cha Yehova Wamphamvuzonse chidzachita zimenezi.
32 N'en est-il pas ainsi? Voici ce que dit le Seigneur, concernant le roi des Assyriens: Il n'entrera point en cette ville, ses archers n'y lanceront pas une flèche; il n'y aura pas de bouclier qui s'avance contre elle, on n'élèvera point de retranchements autour de ses remparts.
“Choncho chimene Yehova akunena za mfumu ya ku Asiriya ndi ichi: “‘Iye sadzalowa mu mzinda umenewu kapena kuponyamo muvi. Sadzayandikira mzindawu ndi zishango zake kapena kumanga nthumbira ya nkhondo.
33 Il s'en retournera par le chemin qu'en venant il a pris, et il n'entrera point en cette ville, dit le Seigneur.
Adzabwerera potsata njira imene anadzera pobwera; sadzalowa mu mzinda umenewu, akutero Yehova.
34 J'étendrai mon bouclier sur cette ville, à cause de moi-même, et à cause de David, mon serviteur.
Ndidzateteza mzinda umenewu kuwupulumutsa, chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha Davide mtumiki wanga.’”
35 Or, la nuit survint, et l'ange du Seigneur s'avança, et il extermina, dans le camp des Assyriens, cent quatre-vingt-cinq mille hommes; les survivants se levèrent dès l'aurore, et ils ne virent que des cadavres.
Usiku umenewo mngelo wa Yehova anapita ku misasa ya ku Asiriya ndi kupha ankhondo 185,000. Ndipo pamene anthu anadzuka mmawa, taonani, mitembo inali ngundangunda!
36 Et Sennachérib partit; il s'en retourna, et il ne sortit plus de Ninive.
Choncho Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anapasula misasa ndi kuchoka. Anabwerera ku Ninive nakakhala kumeneko.
37 Et, comme il adorait dans le temple son dieu Méserach, ses fils Adramélech et Sarasar le tuèrent à coups d'épée; puis, ils se sauvèrent en la terre d'Ararat, et Asordan, son fils, régna à sa place.
Tsiku lina, pamene Senakeribu ankapembedza mʼnyumba ya Nisiroki mulungu wake, ana ake Adirameleki ndi Sarezeri anamupha ndi lupanga ndipo anathawira ku dziko la Ararati. Tsono Esrahadoni, mwana wake, analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Rois 19 >