< 2 Chroniques 32 >

1 Or, après ces choses faites avec sincérité, Sennachérib, roi des Assyriens, vint envahir Juda, et campa devant les villes fortes pour s'en emparer.
Zitatha zonse zimene Hezekiya anachita mokhulupirika, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anabwera ndi kuthira nkhondo dziko la Yuda. Iye anazinga mizinda yotetezedwa ya Yuda, kuganiza kuti ayigonjetsa.
2 Et Ezéchias vit que Sennachérib s'avançait et menaçait Jérusalem.
Pamene Hezekiya anaona kuti Senakeribu wabwera ndipo wakonzeka kuchita nkhondo ndi Yerusalemu,
3 Et il tint conseil avec ses anciens et ses vaillants, leur proposant de clore les fontaines hors de la ville; et ils l'appuyèrent de toute leur force.
iye anakambirana ndi akuluakulu ake pamodzi ndi atsogoleri a gulu lankhondo za kutseka akasupe ochoka ku kasupe amene anali kunja kwa mzinda, ndipo iwo anamuthandiza.
4 Il assembla donc beaucoup de monde, et il renferma en des murs les eaux des fontaines, ainsi que le ruisseau qui traverse la ville, disant: C'est de peur que le roi d'Assyrie, venant, ne trouve une abondance d'eau qui le fortifierait.
Gulu lalikulu la anthu linasonkhana, ndipo anatseka akasupe onse pamodzi ndi mtsinje umene umayenda mʼkati mwa nthakamo. Iwo ankanena kuti, “Nʼchifukwa chiyani mafumu a Asiriya akabwera kuno adzapeze madzi ambiri?”
5 Et Ezéchias augmenta ses défenses; il rétablit toutes les parties des remparts qui s'étaient écroulées et les tours; il bâtit en dehors une seconde enceinte, il releva les fortifications de la ville de David; enfin, il fit faire beaucoup d'armes.
Kenaka iye anagwira ntchito molimbika kukonza madera ogumuka a khoma ndi kumangapo msanja. Anamanganso mpanda wina kunja kwa mpanda winawo ndipo anamanga zolimbitsa Milo ku mzinda wa Davide.
6 Ensuite, il mit des chefs de guerre à la tête du peuple qui s'assembla devant lui sur l'esplanade, vers la porte de la Vallée, et il lui parla au cœur, disant:
Iye anasankha atsogoleri a ankhondo olamulira anthu ndipo anawasonkhanitsa pamaso pake pa bwalo la chipata cha mzinda ndi kuwalimbikitsa ndi mawu awa:
7 Soyez forts, agissez en hommes, n'ayez ni crainte ni faiblesse devant le roi d'Assyrie, et devant les peuples qui le suivent; car il y a plus d'auxiliaires avec nous qu'avec lui.
“Khalani amphamvu ndi olimba mtima. Musachite mantha kapena kutaya mtima chifukwa cha mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lalikulu lankhondo limene ali nalo, pakuti ife tili ndi mphamvu yayikulu kuposa imene ili ndi iye.
8 Il a pour lui des bras de chair; nous, nous avons le Seigneur notre Dieu, qui combattra pour nous et nous sauvera. Et le peuple fut encouragé par le discours d'Ezéchias, roi de Juda.
Iye ali ndi mphamvu ya anthu basi, koma ife tili ndi Yehova Mulungu wathu kutithandiza ndi kuchita nkhondo zathu.” Ndipo anthu anapeza chilimbikitso kuchokera pa zimene Hezekiya mfumu ya Yuda ananena.
9 Après cela, Sennachérib, roi des Assyriens, envoya ses serviteurs à Jérusalem, et lui-même, avec toute son armée, était autour de Lachis, et il envoya ses serviteurs au roi Ezéchias et à tout le peuple de Juda renfermé dans Jérusalem, disant:
Nthawi ina, pamene Senakeribu mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo anali atazinga Lakisi, iye anatumiza atsogoleri ake ankhondo ku Yerusalemu ndi uthenga uwu kwa Hezekiya mfumu ya Yuda ndi anthu onse a ku Yuda amene anali kumeneko:
10 Voici ce que dit Sennachérib, roi des Assyriens: Sur quoi vous appuyez- vous pour rester immobiles dans l'enceinte de Jérusalem?
“Senakeribu mfumu ya ku Asiriya akuti: Kodi inu mukukhulupirira chiyani, kuti mukukhalabe mu Yerusalemu mutazingidwa?
11 Ezéchias ne vous a-t-il pas trompés, pour vous livrer à la faim, à la soif, à la mort, quand il vous a dit: Le Seigneur notre Dieu nous sauvera des mains du roi d'Assyrie?
Pamene Hezekiya akunena kuti ‘Yehova Mulungu wathu adzatipulumutsa kuchoka mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya,’ iye akukusocheretsani, kuti mufe ndi njala ndi ludzu.
12 N'est-ce point cet Ezéchias qui a détruit ses autels et ses hauts lieux, et qui a dit à Juda et à Jérusalem: Vous adorerez sur cet autel, et, sur cet autel, vous offrirez de l'encens?
Kodi si Hezekiya amene anachotsa malo opembedzerapo Mulungu ameneyu ndi maguwa ansembe ndi kunena kwa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kuti, ‘Muzipembedza pa guwa lansembe limodzi ndi kupserezapo nsembe?’
13 Ignorez-vous ce que moi et mes pères avons fait aux peuples de toute la terre? Parmi les dieux des nations de la terre, en est-il un seul qui ait pu sauver son peuple de mes mains?
“Kodi inu simukudziwa zimene ine ndi makolo anga tachita kwa anthu a mitundu ina? Kodi milungu ya mitundu imeneyi inatha kupulumutsa dziko lawo kuchoka mʼdzanja langa?
14 Qui l'a fait, parmi les dieux des nations que nos pères ont exterminées? Si nul d'eux n'a pu sauver son peuple de nos mains, votre Dieu pourra t-il le faire?
Kodi ndi milungu iti mwa milungu ya mitundu ina ya anthuwo, imene makolo anga anayiwononga kotheratu, inatha kupulumutsa anthu ake mʼdzanja langa? Nanga tsono Mulungu wanuyo adzakupulumutsani mʼdzanja langa motani?
15 Qu'Ezéchias cesse donc de vous tromper, qu'il ne vous inspire pas une folle confiance, ne le croyez pas; car nul, des dieux des nations et des royaumes, n'a pu sauver son peuple de mes mains et des mains de nos pères, et votre Dieu ne vous sauvera pas non plus.
Choncho inu musalole kuti Hezekiya akunamizeni ndi kukusocheretsani motere. Musamukhulupirire, pakuti palibe mulungu wa mtundu wina uliwonse kapena ufumu wina uliwonse umene unatha kupulumutsa anthu ake kuchoka mʼdzanja langa kapena mʼdzanja la makolo anga. Nanga bwanji Mulungu wanuyo, sadzatha kukupulumutsani kuchoka mʼdzanja langa!”
16 Or, les serviteurs de Sennachérib continuèrent de parler contre le Seigneur Dieu et contre son serviteur Ezéchias.
Atsogoleri a ankhondo a Senakeribu anapitiriza kuyankhula zotsutsana ndi Yehova Mulungu ndi mtumiki wake Hezekiya.
17 Lui-même écrivit une lettre pour outrager le Seigneur Dieu d'Israël, et il dit: De même que les dieux des nations de la terre n'ont pu délivrer leurs peuples de mes mains, le Dieu d'Ezéchias ne pourra en aucune manière sauver son peuple.
Mfumunso inalemba makalata onyoza Yehova, Mulungu wa Israeli, ndipo inanena zotsutsana naye izi: “Monga momwe milungu ya anthu a mayiko ena sinathe kuwapulumutsa kuchoka mʼdzanja langa, chonchonso Mulungu wa Hezekiya sadzapulumutsa anthu ake kuchoka mʼdzanja langa.”
18 Et l'un des serviteurs cria, en langue judaïque, au peuple de Jérusalem qui se tenait sur les remparts, l'invitant à haute voix à les seconder à démolir les murailles, à leur livrer la ville.
Kenaka iwo anafuwula mu Chihebri kwa anthu a mu Yerusalemu amene anali pa khoma, kuwaopseza ndi kuwachititsa mantha ndi cholinga choti alande mzindawo.
19 Il parla aussi contre le Seigneur Dieu d'Israël, de la même manière que contre les dieux des nations de la terre, œuvres des mains des hommes.
Iwo anayankhula za Mulungu wa Yerusalemu monga anayankhulira za milungu ya anthu ena a pa dziko lapansi, ntchito ya manja a anthu.
20 Et, sur ces paroles, le roi Ezéchias et le prophète Isaïe, fils d'Amos, prièrent, et crièrent au ciel.
Mfumu Hezekiya ndi mneneri Yesaya mwana wa Amozi anafuwulira kumwamba mʼpemphero chifukwa cha zimenezi.
21 Et le Seigneur envoya un ange, et il extermina dans le camp assyrien tous les combattants, les chefs et les généraux. Et Sennachérib, la honte au front, retourna en son royaume, et il entra dans le temple de son Dieu; et des hommes, issus de son sang, le firent périr par le glaive.
Ndipo Yehova anatumiza mngelo amene anadzapha anthu onse odziwa nkhondo ndi atsogoleri ndiponso oyangʼanira misasa ya mfumu ya ku Asiriya. Choncho Senakeribu anabwerera kwawo wamanyazi. Ndipo atalowa mʼnyumba ya mulungu wake, ena mwa ana ake anamupha ndi lupanga.
22 Et le Seigneur sauva Ezéchias, ainsi que les habitants de Jérusalem, des mains de Sennachérib, roi d'Assyrie, et des mains de tous les rois, et il leur donna le repos tout alentour.
Kotero Yehova anapulumutsa Hezekiya ndi anthu a ku Yerusalemu kuchoka mʼdzanja la Senakeribu mfumu ya ku Asiriya ndi mʼdzanja la anthu ena. Yehova anawateteza ku mbali zonse.
23 Et nombre de gens apportèrent à Jérusalem des présents pour le Seigneur et pour Ezéchias, roi de Juda, et, après cela, il fut glorifié aux yeux de toutes les nations.
Anthu ambiri anabweretsa zopereka kwa Yehova ku Yerusalemu ndi mphatso zamtengowapatali kwa Hezekiya mfumu ya Yuda. Kuyambira nthawi imeneyo Hezekiya ankalemekezedwa kwambiri ndi mitundu ina yonse.
24 En ces jours-là, Ezéchias tomba malade à en mourir, et il pria le Seigneur, et le Seigneur l'exauça, et il lui donna un signe.
Pa nthawi imeneyo Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Iye anapemphera kwa Yehova, amene anamuyankha ndi kumupatsa chizindikiro chodabwitsa.
25 Mais Ezéchias ne lui rendit pas selon ce qu'il en avait reçu; son cœur s'enorgueillit, et la colère du Seigneur éclata contre le roi, contre Juda, contre Jérusalem.
Koma Hezekiya anali ndi mtima wonyada ndipo sanachite molingana ndi kukoma mtima kumene Mulungu anamuonetsera. Choncho mkwiyo wa Yehova unali pa iye ndi pa Yuda ndi Yerusalemu.
26 Et Ezéchias s'humilia de s'être enorgueilli en son cœur, et, avec lui, tous les habitants de Jérusalem; et la colère du Seigneur ne vint plus sur eux tant que vécut Ezéchias.
Koma kenaka Hezekiya analapa za kunyada kwakeko, monga anachitanso anthu a mu Yerusalemu. Choncho mkwiyo wa Yehova sunafike pa iwo pa nthawi ya Hezekiya.
27 Et Ezéchias eut beaucoup de gloire et de richesses; il amassa, en ses trésors, de l'or, de l'argent, des pierreries; il eut des épices, des vases de prix et des arsenaux.
Hezekiya anali ndi chuma ndi ulemu wambiri ndipo anamanga nyumba zosungiramo chuma cha siliva wake ndi golide ndi za miyala yokongola, zokometsera zakudya, zishango ndi mtundu uliwonse wa zinthu zamtengowapatali.
28 Il eut des villes où l'on conservait du blé, du vin et de l'huile; il eut des villages et des étables pour toute sorte de bétail, et des bergeries pour les menus troupeaux.
Iye anamanganso nyumba zosungiramo tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta a olivi, ndiponso anamanga nyumba zodyeramo ngʼombe zosiyanasiyana, ndi makola a nkhosa.
29 Il eut des villes, qu'il bâtit pour lui-même, et une grande abondance de bœufs et de brebis; car le Seigneur lui donna d'immenses richesses.
Iyeyo anamanga midzi ndipo anali ndi nkhosa ndi ngʼombe zambiri, pakuti Mulungu anamupatsa chuma chambiri.
30 Ce fut Ezéchias qui fit l'aqueduc qui amena les eaux de la haute fontaine de Gihon en la ville basse de David, au midi. Ezéchias réussit en toutes ses entreprises.
Ndi Hezekiya amene anatseka ku mtunda kwa kasupe wa Gihoni, ndi kumuwongolera kuti madzi ake apite mbali ya kumadzulo kwa Mzinda wa Davide. Iye ankachita bwino pa ntchito iliyonse imene ankagwira.
31 Néanmoins, le Seigneur l'abandonna pour l'éprouver et savoir ce qu'il avait dans le cœur, lorsque les envoyés des chefs de Babylone vinrent le trouver et le questionner sur le prodige qui avait éclaté en la terre promise.
Koma pamene nthumwi zotumizidwa ndi atsogoleri a ku Babuloni zinabwera kudzamufunsa za chizindikiro chozizwitsa chimene chinachitika mʼdzikomo, Mulungu anamusiya yekha, kumuyesa kuti adziwe zonse zimene zinali mu mtima mwake.
32 Le reste des actes d'Ezéchias et sa miséricorde sont écrits en la prophétie d'Isaïe, fils d'Amos, le prophète, et au livre des Rois de Juda et d'Israël.
Zina ndi zina zokhudza ulamuliro wa Hezekiya ndi ntchito za kudzipereka kwake zalembedwa mʼmasomphenya a Yesaya mwana wa Amozi, mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli.
33 Et Ezéchias s'endormit avec ses pères, et on l'ensevelit au-dessus des sépulcres des fils de David; et tout Juda et les habitants de Jérusalem l'honorèrent et le glorifièrent à sa mort. Et Manassé, son fils, régna à sa place.
Hezekiya anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pa phiri pamene pali manda a zidzukulu za Davide. Ayuda onse ndi anthu a mu Yerusalemu anamulemekeza atamwalira. Ndipo Manase mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Chroniques 32 >