< 1 Samuel 1 >

1 Il y avait dans les montagnes d'Ephraïm un homme d'Armathaïm-Sipha; il se nommait Elcana, fils de Jéréméel, fils d'Eliu, fils de Thocé, l'un des Nasib d'Ephraïm.
Panali munthu wina wochokera ku Ramataimu, Mzofimu wa ku dziko la mapiri la Efereimu. Iyeyu dzina lake anali Elikana ndipo anali mwana wa Yerohamu, mwana wa Elihu, mwana wa Tohu, mwana wa Zufu wa fuko la Efereimu.
2 Il avait deux femmes: le nom de la première était Anne; le nom de la seconde, Phenenna; or, Phenenna avait des enfants, et Anne n'en avait point.
Iye anali ndi akazi awiri, Hana ndi Penina. Penina anali ndi ana, koma Hana analibe.
3 Les jours s'écoulèrent, et l'homme partit de la ville d'Armathaïm pour adorer le Seigneur Dieu sabaoth, et lui sacrifier en Silo; Héli et ses deux fils Ophni et Phinéès étaient alors prêtres du Seigneur.
Chaka ndi chaka Elikana ankachoka ku mudzi kwawo kupita ku Silo kukapembedza ndi kukapereka nsembe kwa Yehova Wamphamvuzonse. Ku Siloko kunali ana awiri a Eli, Hofini ndi Finehasi amene anali ansembe a Yehova.
4 Le jour venu, Elcana sacrifia; puis, il donna des parts à Phenenna, sa femme, et à ses fils.
Tsiku lopereka nsembe likafika Elikana amapereka magawo a nsembeyo kwa mkazi wake Penina ndi kwa ana ake onse aamuna ndi aakazi.
5 Mais il ne donna qu'une part à Anne, parce qu'elle n'avait pas d'enfants. Cependant, Elcana aimait Anne plus que la première; et le Seigneur avait clos ses entrailles;
Ngakhale ankamukonda Hana, koma ankamupatsa gawo limodzi popeza Yehova sanamupatse ana.
6 Car le Seigneur, quels que fussent son affliction et l'abattement causé par son affliction, ne lui avait point donné d'enfants. Elle était découragée, parce que le Seigneur avait clos ses entrailles, et ne lui avait point donné d'enfants.
Tsono popeza Yehova sanamupatse Hana ana, mkazi mnzakeyo ankamuyamba dala ndi cholinga chomukwiyitsa.
7 Les choses se passaient de la sorte tous les ans lorsqu'elle montait à la maison du Seigneur; elle était abattue, et elle pleurait, et elle ne mangeait point.
Izi zimachitika chaka ndi chaka. Hana ankati akamapita ku Nyumba ya Yehova mkazi mnzakeyo ankamunyogodola. Choncho Hana ankangokhalira kulira osafuna ndi kudya komwe.
8 Et son époux Elcana lui dit: Anne; et elle répondit: Me voici, seigneur; et il reprit: Qu'as-tu à pleurer? Pourquoi ne manges-tu point? Pourquoi ton cœur te fait-il souffrir? Ne suis-je pas pour toi meilleur que dix enfants?
Tsono mwamuna wake Elikana ankamufunsa kuti, “Hana ukulira chifukwa chiyani? Wakhumudwa ndi chiyani kuti sukufuna ndi kudya komwe? Kodi ine kwa iwe sindili woposa ana aamuna khumi?”
9 Et, après qu'ils eurent mangé à Silo, Anne se leva, puis elle alla se placer devant le Seigneur, pendant qu'Héli le prêtre était sur son siège, devant le seuil du temple du Seigneur.
Tsiku lina atatha kudya ndi kumwa ku Silo kuja, Hana anayimirira kukapemphera. Nthawiyi nʼkuti wansembe Eli atakhala pa mpando pa khomo la Nyumba ya Yehova.
10 Là, tout affligée en son cœur, elle fit au Seigneur une prière, et elle se prit à pleurer amèrement.
Hana anavutika mʼmoyo mwake, ndipo anapemphera kwa Yehova akulira kwambiri.
11 Et elle fit un vœu au Seigneur, disant: Adonaï, Seigneur, Eloé sabaoth, si vous jetez les yeux sur l'humiliation de votre servante, si vous vous souvenez de moi, si vous donnez à votre servante un fils, je vous le consacrerai jusqu'au jour de sa mort; il ne boira ni vin ni boisson enivrante, et le fer ne passera jamais sur sa tête.
Ndipo iye analumbira kuti, “Inu Yehova Wamphamvuzonse, ngati muyangʼana kusauka kwa mtumiki wanune, ndi kuyankha pemphero langa osandiyiwala ine mtumiki wanu pondipatsa mwana wamwamuna, ine ndidzamupereka mwanayo kwa inu Yehova masiku onse a moyo wake. Lumo silidzapita pa mutu pake.”
12 Et pendant qu'elle prolongeait sa prière devant le Seigneur, Héli le prêtre était attentif au mouvement de ses lèvres,
Akupemphera choncho kwa Yehova, Eli ankamuyangʼana pakamwa.
13 Car elle parlait en son cœur, et elle remuait les lèvres, mais on n'entendait point sa voix; or, Héli la crut ivre.
Hana ankapemphera chamumtima ndipo milomo yake inkangogwedera koma mawu ake samamveka. Choncho Eli anaganiza kuti anali ataledzera.
14 Et le serviteur d'Héli alla lui dire: Jusqu'à quand seras-tu donc ivre? Va-t'en avec ton vin; retire-toi de devant le Seigneur.
Ndipo anamufunsa Hana kuti, “Kodi mukhala chiledzerere mpaka liti? Pitani, ayambe wakuchokani vinyo mwamwayo.”
15 Anne répondit, et elle dit au prêtre: Non, seigneur, je suis aujourd'hui une femme pleine d'affliction, je n'ai bu ni vin ni boisson enivrante, et je répands mon âme devant le Seigneur.
Koma Hana anayankha kuti, “Sichoncho mbuye wanga. Ndakhala ndikumukhuthulira Yehova chisoni changa. Sindinamwe vinyo kapena chakumwa choledzeretsa chilichonse, popeza nthawi yonseyi ndakhala ndikupereka kwa Yehova nkhawa yayikulu ndi mavuto anga.
16 Ne prends pas ta servante pour une fille de pestilence; c'est à cause de l'abondance de mes méditations que j'ai prolongé jusqu'à ce moment ma prière.
Musaganize kuti mtumiki wanu ndi kukhala mkazi wachabechabe. Ine ndakhala ndi kupereka nkhawa yanga yayikulu ndi zowawa zanga.”
17 Héli reprenant, lui dit: Va en paix, que le Dieu d'Israël t'accorde toute ta prière, tout ce que tu lui as demandé.
Eli anayankha, “Pitani mu mtendere, ndipo Mulungu wa Israeli akupatseni zimene mwamupemphazo.”
18 Alors, elle dit: Ta servante a trouvé grâce devant tes yeux. Et la femme s'en alla, elle rentra à son logis, elle mangea et but avec son mari, et son visage cessa d'être abattu.
Hana anati, “Mundikomerebe mtima mtumiki wanune.” Kenaka anachoka nakadya, ndipo sanaonekenso wachisoni.
19 Ensuite, s'étant levés de grand matin, ils adorèrent le Seigneur, et reprirent leur chemin; Elcana rentra dans sa maison d'Armathaïm, et il connut Anne; or, le Seigneur se souvint d'elle, et elle conçut.
Elikana ndi banja lake anadzuka mmawa mwake nakapemphera pamaso pa Yehova. Pambuyo pake anabwerera kwawo ku Rama. Elikana anakhala pamodzi ndi mkazi wake, ndipo Yehova anamukumbuka Hanayo.
20 Le temps révolu, elle enfanta un fils, et elle l'appela Samuel, parce que, dit-elle, je l'avais demandé au Seigneur Dieu sabaoth.
Motero Hana anakhala ndi pakati ndipo anabereka mwana wamwamuna. Anamutcha dzina lake Samueli, popeza anati, “Ndinachita kumupempha kwa Yehova.”
21 Or, son époux Elcana, avec toute sa famille, monta à Silo pour offrir au Seigneur le sacrifice de la saison, ses oblations votives, et la dîme de tous les fruits de ses champs.
Elikana ndi banja lake lonse anapita kukapereka nsembe ya pa chaka kwa Yehova ndi kukakwaniritsa malonjezo ake.
22 Mais Anne ne partit pas avec lui, et elle dit à son époux: J'irai quand l'enfant ira, quand je l'aurai sevré, et qu'il sera présenté au Seigneur pour y rester toujours.
Koma Hana sanapite nawo popeza anawuza mwamuna wake kuti, “Mwanayu akadzaleka kuyamwa, ndidzapita naye ndi kukamupereka pamaso pa Yehova ndipo adzakhala kumeneko moyo wake wonse.”
23 Son époux Elcana lui répondit: Fais ce que bon te semble, demeure ici jusqu'à ce que tu l'aies sevré; que le Seigneur accomplisse toutes les paroles qui sont sorties de ta bouche. Et la femme ne bougea pas, et elle allaita son fils jusqu'à ce qu'elle le sevrât.
Elikana mwamuna wake anamuwuza kuti, “Chita chimene chakukomera. Tsala kuno mpaka utamusiyitsa kuyamwa, Yehova yekha akwaniritse mawu ake.” Choncho mkaziyo anatsala ku nyumba ndi kusamalira mwana wake mpaka atamuletsa kuyamwa.
24 Alors, elle partit avec Elcana pour Silo; ils avaient un bœuf de trois ans, des pains, un éphi de fleur de farine et un nébel de vin; elle entra à Silo dans la maison du Seigneur, et son enfant était avec eux.
Atamuletsa kuyamwa, Hana anatenga mwanayo ali wachichepere, ndikupita naye ku nyumba ya Yehova ku Silo. Anatenga ngʼombe yamphongo ya zaka zitatu, ufa wa makilogalamu khumi, ndi thumba lachikopa la vinyo.
25 Et ils le conduisirent devant le Seigneur; son père égorgea la victime que de saison en saison il sacrifiait au Seigneur; il présenta l'enfant après avoir égorgé le bœuf; et Anne, la mère de l'enfant, le conduisit à Héli,
Tsono anapha ngʼombe yamphongo ija ndi kupereka mwana uja kwa Eli.
26 Et elle dit: Je te prie, seigneur, aussi vrai que tu vis, je suis la femme que tu as vue assise devant toi, priant le Seigneur.
Ndipo Hana anati kwa Eli, “Mbuye wanga, ine ndikunenetsadi pamaso panu kuti ndine mkazi uja amene anayima pamaso panu ndi kumapemphera kwa Yehova.
27 J'ai prié pour obtenir cet enfant, et le Seigneur a exaucé la prière que je lui avais faite.
Ndinapempha mwana uyu, ndipo Yehova wandipatsa chimene ndinamupempha.
28 Cet enfant, je le donne au Seigneur pour être tous les jours de sa vie au service du Seigneur; puis, elle dit:
Ndiye tsopano ine ndikumupereka kwa Yehova. Pa moyo wake wonse adzakhala wa Yehova.” Ndipo onse anapembedza Yehova kumeneko.

< 1 Samuel 1 >