< 1 Samuel 7 >

1 Et les hommes de Cariath-Iarim vinrent; ils emmenèrent l'arche de l'alliance du Seigneur, et ils l'introduisirent dans la maison qu'Aminadab possédait sur la colline. Puis ils sanctifièrent son fils Eléazar, afin qu'il gardât l'arche de l'alliance du Seigneur.
Choncho anthu a ku Kiriati-Yearimu anabwera ndi kudzatenga Bokosi la Yehova. Iwo anapita nalo ku nyumba ya Abinadabu ya ku phiri ndipo anapatula Eliezara mwana wake kuti aziyangʼanira Bokosi la Yehovalo.
2 A partir du jour où l'arche entra à Cariath-Iarim, bien des jours s'écoulèrent, elle y était déjà depuis vingt ans, quand tout Israël se tourna vers le Seigneur.
Zaka makumi awiri zinapita kuyambira pamene Bokosi la Yehova linakhala ku Kiriati-Yearimu, ndipo anthu a Israeli onse analira kupempha Yehova kuti awathandize.
3 Alors, Samuel parla à toute la maison d'Israël, disant: Si c'est de tout votre cœur que vous revenez à Dieu, chassez du milieu de vous les dieux étrangers, détruisez leurs bois sacrés, préparez vos âmes pour le Seigneur Dieu, ne servez que lui seul; et il vous affranchira du joug des Philistins.
Ndipo Samueli anati kwa nyumba yonse ya Israeli, “Ngati mukubwerera kwa Yehova ndi mtima wanu wonse, muchotse milungu yachilendo ndi Asiteroti pakati panu ndipo mitima yanu ikhazikike pa Yehova ndi kutumikira Iye yekha. Mukatero Iye adzakupulumutsani mʼmanja mwa Afilisti.”
4 Les fils d'Israël chassèrent donc Baal; ils détruisirent les bois sacrés d'Astaroth, et ils ne servirent que le Seigneur.
Choncho Aisraeli anachotsa milungu yawo ya Baala ndi Asitoreti ndi kutumikira Yehova yekha.
5 Et Samuel dit: Réunissez tout Israël en Masphath; et je prierai pour vous le Seigneur.
Kenaka Samueli anati, “Sonkhanitsani Aisraeli onse ku Mizipa ndipo ine ndidzakupemphererani kwa Yehova.”
6 Et ils se rassemblèrent en Masphath; ils puisèrent de l'eau, et la répandirent sur la terre devant le Seigneur; ce jour-là ils jeûnèrent, et ils dirent: Nous avons péché devant le Seigneur. Puis, Samuel jugea les fils d'Israël en Masphath.
Choncho anasonkhana ku Mizipa, ndipo anatunga madzi ndi kuwathira pansi pamaso pa Yehova. Pa tsiku limenelo anasala kudya namanena kuti, “Ife tachimwira Yehova.” Ndipo Samueli anali mtsogoleri wa Israeli ku Mizipa.
7 Et les Philistins apprirent que tous les fils d'Israël étaient assemblés en Masphath, les chefs des Philistins se mirent aussitôt en marche contre Israël; les fils d'Israël le surent, et ils eurent crainte des étrangers.
Afilisti anamva kuti Aisraeli asonkhana ku Mizipa, choncho akalonga awo anabwera kudzawathira nkhondo. Ndipo Aisraeli atamva anachita mantha chifukwa cha Afilisti.
8 Et les fils d'Israël dirent à Samuel: Ne cesse pas de crier pour nous au Seigneur ton Dieu; il nous sauvera des mains de nos ennemis.
Choncho anati kwa Samueli, “Musasiye kutipempherera kwa Yehova Mulungu wathu, kuti atipulumutse mʼdzanja la Afilistiwa.”
9 Samuel prit un agneau de lait, et avec tout le peuple, il l'offrit en holocauste au Seigneur; Samuel cria au Seigneur en faveur du peuple, et le Seigneur l'exauça.
Ndipo Samueli anatenga mwana wankhosa wamkazi woyamwa ndi kumupereka monga nsembe yopsereza kwa Yehova. Iye anapemphera kwa Yehova mʼmalo mwa Aisraeli, ndipo Yehova anamuyankha.
10 Samuel était à offrir l'holocauste pendant que les Philistins s'avançaient pour combattre Israël; et ce jour-là le Seigneur fit entendre contre les Philistins la grande voix du tonnerre; ils furent confondus, et ils s'enfuirent devant Israël.
Samueli akupereka nsembe yopsereza, Afilisti anayandikira kuti ayambe kuwathira nkhondo Aisraeli. Koma tsiku limenelo Yehova anawaopseza Afilisti aja ndi mawu aakulu ngati bingu. Choncho anasokonezeka motero kuti Aisraeli anawagonjetsa.
11 Et les hommes d'Israël sortirent de Masphath, poursuivirent les Philistins, et les taillèrent en pièces jusqu'au-dessous de Bethchor.
Aisraeli anatuluka ku Mizipa kuthamangitsa Afilisti aja nʼkumawapha mʼnjira yonse mpaka kumunsi kwa Beti-Kari.
12 Après cela, Samuel prit une pierre qu'il dressa entre Masphath et la vieille ville; et il l'appela Abenézer, Pierre du Secours, et il dit: ici le Seigneur nous a secourus.
Kenaka Samueli anatenga mwala nawuyika pakati pa Mizipa ndi Seni. Iye anawutcha Ebenezeri, popeza anati, “Yehova watithandiza mpaka pano.”
13 Ainsi, le Seigneur humilia les Philistins; ils cessèrent d'envahir le territoire d'Israël, et la main du Seigneur se tourna contre les Philistins durant tous les jours de Samuel.
Kotero Afilisti anagonjetsedwa ndipo sanadzalowenso mʼdziko la Israeli. Yehova analimbana ndi Afilisti masiku onse a Samueli.
14 Et les Philistins rendirent toutes les villes qu'ils avaient prises aux fils d'Israël; ils les rendirent à Israël depuis Ascalon jusqu'à Azot. Israël recouvra ses limites qu'il reprit aux Philistins; cependant la paix régnait entre Israël et l'Amorrhéen.
Mizinda yonse imene Afilisti analanda kuchokera ku Ekroni mpaka ku Gati inabwezedwa kwa Aisraeli. Choncho Aisraeli anapulumutsa dziko lawo. Ndipo panalinso mtendere pakati pa Aisraeli ndi Aamori.
15 Ensuite, Samuel jugea le peuple, durant tons les jours de sa vie.
Samueli anatsogolera Aisraeli moyo wake wonse.
16 Tous les ans il voyageait; il passait dans sa tournée par Béthel, Galgala et Masphath; et en tous ces lieux saints, il jugeait Israël.
Chaka ndi chaka Samueli ankakonza ulendo wozungulira kuchokera ku Beteli mpaka ku Giligala ndi Mizipa, kuweruza milandu ya Aisraeli mʼmadera onsewa.
17 Enfin, il rentrait en Armathem, où était sa demeure; il y jugeait Israël, et il y bâtit un autel au Seigneur.
Koma pambuyo pake ankabwerera ku Rama, kumene kunali nyumba yake. Ankaweruza Aisraeli kumeneko. Ndipo iye anamanga guwa lansembe la Yehova kumeneko.

< 1 Samuel 7 >