< 1 Samuel 27 >

1 Et David dit en son cœur: Je tomberai un jour entre les mains de Saül, et je n'ai rien de bon à attendre, si je ne me réfugie dans la terre des Philistins; Saül alors cessera de me chercher sur toutes les montagnes d'Israël; et j'échapperai à ses mains.
Davide anaganiza mu mtima mwake nati, “Tsiku lina ine ndidzaphedwa ndi Sauli. Palibe chabwino ndingachite, koma kuthawira ku dziko la Afilisti. Kotero Sauli adzasiya kundifunafuna mʼdziko lonse la Israeli, ndipo ndidzapulumuka.”
2 David partit donc avec les six cents hommes qui l'accompagnaient, et il alla chez Achis, fils d'Ammach, roi de Geth.
Choncho Davide ndi anthu 600 amene anali nawo anachoka napita kwa Akisi mwana wa Maoki mfumu ya ku Gati.
3 Et David s'établit chez Achis, lui et ses gens, chacun avec sa famille; David avait avec lui ses deux femmes: Achinaam la Jezraélite, et Abigaïl, femme de Nabal du Carmel.
Davide anakhala ndi Akisi ku Gati pamodzi ndi ankhondo ake, aliyense ndi banja lake. Davide ali ndi akazi ake awiri, Ahinoamu wa ku Yezireeli ndi Abigayeli wa ku Karimeli, mkazi wamasiye wa Nabala.
4 Et l'on alla rapporter à Saül que David s'était réfugié à Geth, et il cessa de le chercher.
Sauli anamva kuti Davide wathawira ku Gati, ndipo sanamufunefunenso.
5 Et David dit à Achis: Si ton serviteur a trouvé grâce à tes yeux, que l'on me donne, dans une des villes de ce pays, un lieu où je demeurerai; car pourquoi ton serviteur réside-t-il avec toi dans ta ville royale?
Kenaka Davide anawuza Akisi kuti, “Ngati ndapeza kuyanja pamaso panu mundipatse malo dera limodzi la dziko lanu kuti ndizikhala kumeneko. Mtumiki wanu adzakhala mu mzinda waufumu chifukwa chiyani?”
6 Ce jour-là même, Achis lui donna Sécelac; à cause de cela, Sécelac a fait partie du royaume de Juda jusqu'à nos jours.
Choncho tsiku limenelo Akisi anamupatsa Zikilagi ndipo mzindawo wakhala wa mafumu a Yuda mpaka lero.
7 Et le nombre des jours que David passa sur les terres des Philistins fit quatre mois.
Davide anakhala mʼdziko la Afilisti kwa chaka chimodzi ndi miyezi inayi.
8 Or, David et sa troupe sortaient, et ils attaquaient tout Gesiri et l'Amalécite. Et la contrée était habitée, depuis les postes fortifiés de Gelampsur, jusqu'à la terre d'Égypte.
Tsono Davide ndi anthu ake ankapita kukathira nkhondo Agesuri, Agirizi ndi Aamaleki. (Mitundu ya anthu imeneyi kuyambira kale inkakhala mʼdziko la pakati pa Suri ndi Igupto).
9 David frappait cette contrée, et il n'y laissait vivants ni homme ni femme; il enlevait les bœufs, les ânes, les chameaux, les vêtements; puis, il s'en retournait et revenait chez Achis.
Davide ankati akathira nkhondo dera lina, sankasiya munthu wamoyo, mwamuna kapena mkazi, koma ankatenga nkhosa, ngʼombe, abulu, ngamira ndi zovala, pambuyo pake nʼkubwerera kwa Akisi.
10 Alors, Achis disait à David: Qui as-tu attaqué aujourd'hui? David répondait: Ceux qui sont au midi de la Judée, au midi de Jesmega, au midi de Cénézi.
Akisi akafunsa kuti, “Kodi lero unapita kukathira nkhondo kuti?” Davide ankayankha kuti, “Ndinapita kukathira nkhondo kummwera kwa Yuda,” mwinanso ankanena kuti, “Ndinapita ku dziko la Ayerahimeeli” kapenanso ankanena kuti, “Ndinapita ku dziko la Akeni.”
11 Je n'ai laissé vivants ni homme ni femme pour les amener à Geth; car je ne veux pas, disais-je, qu'ils parlent de nous dans Geth, et qu'ils disent: Voilà ce qu'a fait David. Telles furent ses habitudes tout le temps qu'il demeura sur les terres des Philistins.
Davide sankasiya mwamuna kapena mkazi wamoyo kuti akafotokozere anthu a ku Gati zochitikazo kuopa kuti opulumukawo akhoza kudzanena kuti “Davide watichita zakutizakuti.” Tsono izi ndi zimene Davide ankachita pamene ankakhala mʼdziko la Afilisti.
12 Et David inspira la plus grande confiance à Achis, qui se disait: On l'a indignement traité au milieu de son peuple en Israël, et il sera toujours mon serviteur.
Akisi ankamukhulupirira Davide ndipo ankati mu mtima mwake, “Davide wadzisandutsa munthu woyipa kwambiri pakati pa anthu ake omwe, Aisraeli. Tsono adzakhala mtumiki wanga mpaka kalekale.”

< 1 Samuel 27 >