< 1 Rois 2 >

1 Le jour où David allait mourir était proche; et il parla à son fils Salomon en ces termes:
Davide ali pafupi kumwalira, analangiza mwana wake Solomoni kuti:
2 Je m'en vais dans la voie de toute la terre; quant â toi, sois fort et agis en homme.
“Ndatsala pangʼono kupita kumene munthu wina aliyense amayenera kupitako. Tsono khala wamphamvu, uvale zilimbe,
3 Observe les commandements du Seigneur ton Dieu, afin de marcher dans ses voies, de garder ses commandements, sa justice, ses jugements, et les préceptes qui sont écrits en la loi de Moïse; conduis-toi sagement en toutes choses, comme je te l'ai prescrit;
ndipo uzichita zimene Yehova Mulungu wako amafuna, uziyenda mʼnjira zake, uzisunga malangizo ndi malamulo ake monga momwe zinalembedwera mʼMalamulo a Mose, kuti zonse zimene udzachite zidzakuyendere bwino kulikonse kumene udzapite.
4 Afin que le Seigneur confirme la parole qu'il a dite: Si tes fils sont attentifs à suivre leur voie, devant moi, dans la vérité et de tout leur cœur, jamais il ne manquera d'homme issu de toi pour monter sur le trône d'Israël.
Ndipo Yehova akwaniritse zimene anandilonjeza kuti, ‘Ngati zidzukulu zako zidzakhala mosamala, niziyenda mokhulupirika pamaso panga ndi mtima wawo wonse ndi moyo wawo wonse, sudzasowa munthu wokhala pa mpando waufumu wa Israeli.’
5 Or, tu sais ce que m'a fait Joab, fils de Sarvia; tu sais comment il a traité les deux chefs de l'armée d'Israël: Abner, fils de Ner, et Amessaï, fils de Jéther. Il les a tués; le sang, réservé au combat, il l'a fait couler pendant la paix; il a versé le sang innocent sur la ceinture qui ceignait ses reins, et sur les sandales qui chaussaient ses pieds.
“Tsono iwe ukudziwanso zoyipa zimene Yowabu mwana wa Zeruya anandichitira pakupha atsogoleri awiri a ankhondo a Israeli, Abineri mwana wa Neri ndi Amasa mwana wa Yeteri. Iye anawapha ndi kukhetsa magazi nthawi ya mtendere ngati nthawi ya nkhondo, ndipo anapaka magazi amenewo pa lamba wa mʼchiwuno mwake ndi pa nsapato za ku mapazi ake.
6 Tu feras ce que t'inspirera ta sagesse, et tu ne laisseras pas sa vieillesse descendre en paix au tombeau. (Sheol h7585)
Iwe uchite kwa iye molingana ndi nzeru zako, koma usalole kuti afe ndi ukalamba ndi kupita ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
7 Et tu seras bienveillant pour les fils de Berzelli le Galaadite; ils seront de ceux qui mangeront à ta table, car c'est ainsi qu'ils ont agi envers moi quand je fuyais devant Absalon ton frère.
“Koma ana a Barizilai wa ku Giliyadi uwakomere mtima ndipo uwalole kuti akhale mʼgulu la anthu amene azidya pamodzi nawe. Pakuti anandisamalira pamene ndinkathawa mʼbale wako Abisalomu.
8 Tu vois avec toi Sémeï, fils de Géra, de la famille de Jémini de Bathurim; c'est lui qui m'a poursuivi de malédictions bien amères, le jour où je m'en allais au camp; à mon retour, il est venu à ma rencontre vers le Jourdain; je lui ai alors prêté serment au nom du Seigneur, et j'ai dit: Je ne te ferai point mourir par l'épée.
“Ndipo kumbukira kuti uli ndi Simei mwana wa Gera, wa fuko la Benjamini wochokera ku Bahurimu, amene ananditemberera koopsa tsiku limene ndimapita ku Mahanaimu. Atabwera kudzakumana nane ku Yorodani, ine ndinalumbira mʼdzina la Yehova kuti, ‘Sindidzakupha iwe ndi lupanga.’
9 Tu ne l'innocenteras point, car tu es un homme sage; tu sauras comment le traiter, et tu feras descendre sa vieillesse au tombeau dans le sang. (Sheol h7585)
Koma tsopano usamuyese ngati munthu wosalakwa. Iwe ndiwe munthu wanzeru. Udzadziwa choti uchite naye. Ngakhale ndi wokalamba, aphedwe ndithu.” (Sheol h7585)
10 Et David s'endormit avec ses pères, et il fut enseveli dans la ville de David.
Tsono Davide anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu Mzinda wa Davide.
11 Les jours du règne de David sur Israël formèrent quarante ans; il régna sept ans à Hébron et trente-trois ans à Jérusalem.
Iyeyo nʼkuti atalamulira Israeli kwa zaka makumi anayi. Ku Hebroni analamulira zaka zisanu ndi ziwiri ndipo ku Yerusalemu analamulira zaka 33.
12 Et Salomon s'assit sur le trône de David son père, et son règne était parfaitement préparé.
Choncho Solomoni anakhala pa mpando waufumu wa abambo ake Davide, ndipo ufumu wake unakhazikika kwambiri.
13 Ensuite, Adonias, fils d'Aggith, entra chez Bethsabée, mère de Salomon; il se prosterna devant elle, et elle lui dit: En entrant, nous apportes-tu la paix? Et il répondit: La paix;
Tsono Adoniya, mwana wa Hagiti, anapita kwa Batiseba, amayi ake a Solomoni. Batiseba anamufunsa kuti, “Kodi wabwera mwamtendere?” Iye anayakha kuti, “Eya, ndi zamtendere.”
14 J'ai à te dire un mot. Parle, reprit-elle.
Ndipo iye anawonjezera kunena kuti, “Ndili ndi mawu oti ndiyankhule nanu.” Batiseba anayankha kuti, “Yankhula.”
15 Tu sais, lui dit-il, que la royauté m'appartenait, et que tout Israël avait jeté les yeux sur moi pour que je régnasse; mais la royauté a été détournée de moi, et elle a passé à mon frère, parce que telle était la volonté du Seigneur.
Tsono Adoniya anati, “Monga inu mukudziwa, ufumu unali wanga. Aisraeli onse ankayembekezera kuti ine ndidzakhala mfumu yawo. Koma zinthu zinasintha ndipo ufumu wapita kwa mʼbale wanga; pakuti wapatsa iye ufumuwu ndi Yehova.
16 Maintenant, j'ai à te faire une seule demande; ne détourne pas de moi ton visage. Et Bethsabée lui dit: Parle.
Tsono ndili ndi pempho limodzi kwa inu. Musandikanize ayi.” Batiseba anati, “Nena.”
17 Et il continua: Parle au roi Salomon; car il ne détournera pas de toi son visage; qu'il me donne pour femme Abisag la Sunamite.
Adoniya anapitiriza kunena kuti, “Chonde, inu mupemphe mfumu Solomoni kuti andipatse Abisagi wa ku Sunemu kuti akhale mkazi wanga pakuti mukapempha inu sadzakukanizani.”
18 A quoi Bethsabée reprit: Bien; je parlerai au roi en ta faveur.
Batiseba anayankha kuti, “Chabwino. Ndidzakuyankhulira kwa mfumu.”
19 Bethsabée alla trouver le roi Salomon, afin de lui parler en faveur d'Adonias. Le roi se leva, alla au-devant d'elle, la baisa et s'assit sur son trône; puis on plaça un trône pour la mère du roi, et elle s'assit à sa droite.
Batiseba atapita kwa Mfumu Solomoni kukayankhula naye mʼmalo mwa Adoniya, mfumu inanyamuka kukumana naye, ndipo inaweramira amayi akewo, kenaka inakhala pa mpando wake waufumu. Iye anayitanitsa mpando wina kuti amayi ake akhalepo ndipo anakhala pansi ku dzanja lake lamanja.
20 Et elle lui dit: J'ai à te faire une petite demande; ne repousse pas mon visage. Et le roi répondit: Demande, ma mère, et je ne te repousserai point.
Amayi akewo anati, “Ndikufuna ndikupempheni kanthu kakangʼono. Chonde musandikanize.” Mfumu inayankha kuti, “Pemphani amayi, ine sindikukanizani.”
21 Et elle dit: Que la Sunamite Abisag soit donnée pour femme à ton frère Adonias.
Ndipo amayiwo anati, “Mulole kuti Abisagi wa ku Sunemu akhale mkazi wa mʼbale wanu Adoniya.”
22 Le roi Salomon répondit, et il dit à sa mère: Pourquoi as-tu demandé Abisag pour Adonias? Demande aussi pour lui la royauté, car il est mon frère, il est plus âgé que moi, et il a pour compagnon Abiathar le prêtre, et Joab, fils de Sarvia, général en chef.
Koma Mfumu Solomoni inayankha amayi ake aja kuti, “Chifukwa chiyani mukupemphera Adoniya Abisagi wa ku Sunemu? Mungathenso kumupemphera ufumu pakuti iyeyu ndi mkulu wanga ndipo mupemphereninso wansembe Abiatara ndi Yowabu mwana wa Zeruya!”
23 Et le roi jura au nom du Seigneur, disant: Que le Seigneur me punisse, et qu'il me punisse encore, si, en faisant cette demande, Adonias n'a pas parlé contre sa vie.
Pamenepo Mfumu Solomoni inalumbira mʼdzina la Yehova kuti, “Mulungu andilange ine koopsa ngati Adoniya saphedwa chifukwa cha pempho lakeli!
24 Maintenant, vive le Seigneur qui m'a préparé, qui m'a placé sur le trône de David mon père, qui a établi ma maison comme il l'avait promis! aujourd'hui même Adonias mourra.
Tsono pali Yehova wamoyo, amene anandikhazikitsa ine pa mpando waufumu wa abambo anga Davide ndi kundipatsa ufumu monga analonjezera, Adoniya aphedwa lero lomwe lino!”
25 Salomon confia l'exécution de ce dessein à Banaïas, fils de Joïada. Celui- ci tua Adonias, qui mourut le jour même.
Choncho Mfumu Solomoni inalamula Benaya mwana wa Yehoyada ndipo anakantha Adoniyayo, nafa.
26 Et le roi dit à Abiathar le prêtre: Retourne vite à ton champ en Astaroth, car tu es, en ce jour-ci, un homme digne de mort; toutefois, je ne te ferai point périr, parce que tu as porté devant mon père l'arche de l'alliance du Seigneur, et que tu as souffert en tout ce qu'a souffert David.
Ndipo mfumu inati kwa Abiatara wansembe, “Pita ku Anatoti ku minda yako chifukwa ndiwe woyenera kufa, koma sindikupha tsopano, chifukwa unkanyamula Bokosi la Chipangano la Ambuye Yehova pamaso pa abambo anga Davide ndipo unazunzika limodzi ndi abambo angawo.”
27 Et Salomon interdit le sacerdoce à Abiathar, pour que s'accomplît la parole que le Seigneur avait prononcée contre la maison d'Héli.
Kotero Solomoni anachotsa Abiatara pa udindo wokhala wansembe wa Yehova, kukwaniritsa mawu a Yehova amene anayankhula za nyumba ya Eli ku Silo.
28 La nouvelle en arriva jusqu'à Joab, fils de Sarvia; or, Joab avait été l'un des convives d'Adonias, et il ne s'était point rapproché de Salomon. Joab se réfugia dans le tabernacle du Seigneur, et il embrassa la corne de l'autel.
Yowabu atamva zimenezi anathawira ku tenti ya Yehova ndipo anakagwira msonga za guwa lansembe, popeza Yowabu ndiye anathandiza Adoniya kuwukira koma sanathandize Abisalomu.
29 Et l'on vint l'annoncer au roi Salomon; on lui dit: Joab s'est réfugié dans le tabernacle du Seigneur, et le voilà qui tient la corne de l'autel. Aussitôt, Salomon envoya auprès de Joab, et il lui dit: Que t'arrive-t-il, pour que tu te réfugies à l'autel? Joab répondit: J'ai eu crainte de toi, et je me suis réfugié auprès du Seigneur. Et Salomon envoya Banaïas, fils de Joïada, disant: Va, tue-le, et ensevelis-le.
Mfumu Solomoni inawuzidwa kuti Yowabu wathawira ku tenti ya Yehova ndipo ali pambali pa guwa lansembe. Tsono Solomoni analamula Benaya mwana wa Yehoyada kuti, “Pita, kamukanthe!”
30 Banaïas, fils de Joïada, alla trouver Joab dans le tabernacle du Seigneur, et il lui dit: Voici ce que dit le roi: Sors; mais Joab répondit: Je ne sortirai point, c'est ici que je mourrai. Banaïas retourna chez le roi, et il lui dit: Voici ce que j'ai dit à Joab, voici ce qu'il m'a répondu.
Choncho Benaya analowa mʼtenti ya Yehova ndipo anati kwa Yowabu, “Mfumu ikuti ‘Tuluka!’” Koma iye anayankha kuti, “Ayi, ine ndifera muno.” Benaya anakafotokozera mfumu kuti, “Umu ndi mmene Yowabu wandiyankhira.”
31 Le roi reprit: Va et fais-lui comme il a dit: Tue-le, ensevelis-le, et tu auras aujourd'hui détourné de moi et de la maison de mon père le sang que Joab a versé sans motif.
Pamenepo mfumu inalamula Benaya kuti, “Kachite monga iye wanenera. Ukamukanthe ndi kumuyika mʼmanda. Ukatero udzandichotsera ine pamodzi ndi nyumba ya abambo anga mlandu wa anthu osalakwa amene Yowabu anawapha.
32 Le Seigneur a ramené sur sa tête le sang de son iniquité, car il est allé à la rencontre de deux hommes plus justes et meilleurs que lui; il les a fait périr par le glaive, et mon père David ne savait rien du meurtre d'Abner, fils de Ner, général en chef d'Israël, ni du meurtre d'Amessaï, fils de Jéther, général en chef de Juda.
Yehova adzamubwezera zomwe anachita pokhetsa magazi, chifukwa iye anakantha ndi lupanga anthu awiri abwino ndi olungama kuposa iye, nawapha, abambo anga Davide osadziwa. Anthu awiriwo ndi Abineri mwana wa Neri, wolamulira gulu lankhondo la Israeli ndi Amasa mwana wa Yeteri, wolamulira gulu lankhondo la Yuda.
33 Leur sang est retombé sur sa tête, et sur la tête de sa postérité à jamais. Que la paix du Seigneur soit toujours avec David, avec sa race, avec sa maison et avec son trône.
Magazi amene Yowabu anakhetsa akhale pamutu pake ndi pa zidzukulu zake kwamuyaya. Koma pa Davide ndi zidzukulu zake, nyumba yake ndi mpando wake waufumu pakhale mtendere wochokera kwa Yehova kwamuyaya.”
34 Et Banaïas, fils de Joïada, alla retrouver Joab; il le tua, et il l'inhuma dans sa maison près du désert.
Choncho Benaya mwana wa Yehoyada anapita kukakantha Yowabu nʼkumupha ndipo anayikidwa mʼmanda mʼnyumba yakeyake ya ku chipululu.
35 Le roi, à sa place, donna le commandement de l'armée à Banaïas, et la royauté fut affermie dans Jérusalem. Sadoc fut premier prêtre à la place d'Abiathar.
Mfumu inayika Benaya mwana wa Yehoyada kuti akhale woyangʼanira gulu lankhondo mʼmalo mwa Yowabu ndipo inayika Zadoki kuti akhale wansembe mʼmalo mwa Abiatara.
36 Et le roi appela Semeï, et il lui dit: Bâtis pour toi une maison dans Jérusalem, demeures-y, et de là tu n'iras en aucun lieu.
Kenaka mfumu inatuma anthu kukayitana Simei ndipo inamuwuza kuti, “Udzimangire nyumba mu Yerusalemu ndipo uzikhala kumeneko, koma usatuluke mu mzinda kupita kwina kulikonse.
37 Le jour où tu en sortirais, où tu passerais le torrent de Cédron, sache-le bien, tu mourrais de mort; et ton sang retomberait sur ta tête. Et le roi, ce jour-là, lui fit prêter serment.
Tsiku lomwe udzatulukemo ndi kuwoloka Chigwa cha Kidroni, udziwiretu kuti udzafa ndipo magazi ako adzakhala pamutu pako.”
38 Ensuite, Sémeï dit au roi: La parole que tu as dite est bonne, ô roi mon maître, ainsi fera ton serviteur. Et Sémeï demeura trois ans à Jérusalem.
Simei anayankha mfumu kuti, “Zimene mwanenazi nʼzabwino. Kapolo wanu adzachita monga mbuye wanga mfumu mwanenera.” Choncho Simei anakhala mu Yerusalemu nthawi yayitali.
39 Après trois ans, deux serviteurs de Sémeï s'enfuirent chez Achis, fils de Maacha, roi de Geth. On l'apprit à Sémeï en lui disant: Voilà tes serviteurs à Geth.
Koma patatha zaka zitatu, akapolo awiri a Simei anathawira kwa Akisi mwana wa Maaka, mfumu ya ku Gati, ndipo Simei anawuzidwa kuti, “Akapolo anu ali ku Gati.”
40 Et Sémeï se leva, bâta son ânesse et, s'en alla chez Achis à Geth, pour réclamer ses deux serviteurs; puis il revint, et les ramena de Geth.
Atamva zimenezi, anakwera bulu wake ndipo anapita kwa Akisi ku Gati kukafunafuna akapolo ake. Choncho Simei anapita ndi kukatenga akapolo ake ku Gati ndipo anabwera nawo.
41 Or, on l'apprit à Salomon en lui disant: Sémeï est allé de Jérusalem à Geth, et il a ramené ses serviteurs.
Solomoni atawuzidwa kuti Simei anatuluka mu Yerusalemu ndi kupita ku Gati ndipo kuti wabwerako,
42 Aussitôt, le roi envoya querir Sémeï, et il lui dit: Ne t'ai-je point fait prêter serment par le Seigneur, ne t'ai-je pas attesté, disant: Le jour où tu sortiras de Jérusalem, où tu iras à droite ou à gauche, sache-le bien, tu mourras?
mfumu inamuyitanitsa Simei ndipo inamufunsa kuti, “Kodi sindinakulumbiritse mʼdzina la Yehova ndi kukuchenjeza kuti, ‘Tsiku limene udzatuluka kupita kwina kulikonse, udziwe kuti udzafa’? Nthawi imeneyo iwe unandiwuza kuti, ‘Zimene mwanena nʼzabwino. Ine ndidzamvera.’
43 Pourquoi n'as-tu point gardé le serment du Seigneur, et le commandement que je t'avais donné?
Chifukwa chiyani tsono sunasunge lumbiro lako kwa Yehova? Bwanji nanga sunamvere lamulo limene ndinakuwuza?”
44 Et le roi ajouta: Tu connais, ton cœur sait tout le mal que tu as fait à David mon père; le Seigneur a fait retomber ta méchanceté sur ta tête.
Mfumuyo inawuzanso Simei kuti, “Ukudziwa mu mtima mwakomo zoyipa zonse zimene unachitira abambo anga Davide. Tsopano Yehova akubwezera zoyipa zakozo.
45 Cependant, Salomon est béni, et le trône de David est affermi devant le Seigneur à jamais.
Koma Mfumu Solomoni idzadalitsidwa ndipo mpando waufumu wa Davide udzakhazikika pamaso pa Yehova kwamuyaya.”
46 Et le roi donna ses ordres à Banaïas, fils de Joïada, qui sortit avec Sémeï et le tua. Le roi Salomon était doué d'une grande intelligence et d'une grande sagesse.
Pamenepo mfumu inalamula Benaya mwana wa Yehoyada ndipo iye anapita kukakantha Simei ndi kumupha. Tsono ufumu unakhazikika mʼdzanja la Solomoni.

< 1 Rois 2 >