< 1 Rois 19 >

1 Et Achab apprit à Jézabel sa femme tout ce qu'avait fait Elle, et comment il avait tué les prophètes par l'épée.
Tsono Ahabu anawuza Yezebeli zonse zimene anachita Eliya ndi momwe anaphera aneneri onse ndi lupanga.
2 Et Jézabel envoya chez Elie, et elle dit: Si tu es Elie, moi je suis Jézabel: que Dieu me punisse et me punisse encore, si demain, à pareille heure, je n'ai pas fait de ta vie ce que tu as fait de la vie de chacun d'eux.
Choncho Yezebeli anatuma mthenga kwa Eliya kuti akamuwuze kuti, “Milungu indilange, ndipo indilange koopsa, ngati mawa nthawi ngati yomwe ino sindidzakupha iwe monga unaphera aneneriwo.”
3 Et Elie eut crainte; il se leva; il s'éloigna pour sauver sa vie, et se rendit à Bersabée en Juda, où il laissa son serviteur.
Eliya ataona zimenezi, ananyamuka nathawa kupulumutsa moyo wake. Atafika ku Beeriseba ku Yuda, anasiya mtumiki wake kumeneko,
4 Lui-même s'enfonça dans le désert à une journée de marche; il s'assit sous un genévrier, et il demanda la mort, disant: C'est assez, prenez maintenant mon âme, ô Seigneur, car je ne suis pas meilleur que mes pères.
ndipo Eliyayo anayenda ulendo wa tsiku limodzi mʼchipululu. Anafika pa kamtengo ka tsache, nakhala pansi pa tsinde lake napemphera kuti afe. Iye anati, “Yehova, ine ndatopa nazo. Chotsani moyo wanga. Ineyo sindine wopambana makolo anga.”
5 Et il se coucha et il s'endormit sous le genévrier; or voilà qu'un ange le toucha, et lui dit: Lève-toi et mange.
Ndipo Eliya anagona tulo tofa nato pa tsinde pa kamtengoko. Ndipo taonani, mngelo anamukhudza, namuwuza kuti, “Dzuka udye.”
6 Il regarda, et il vit auprès de sa tête des gâteaux d'épeautre et une fiole d'eau; il se leva, il mangea, il but et il s'endormit.
Eliya anayangʼana, ndipo taonani kumutu kwake kunali buledi wootcha pa makala ndi botolo la madzi. Iye anadya ndi kumwa, nʼkugonanso.
7 L'ange du Seigneur revint une seconde fois, le toucha, et lui dit: Lève- toi et mange, car tu as à faire un long chemin.
Mngelo wa Yehova anabweranso kachiwiri, anamukhudza, namuwuza kuti, “Dzuka udye, popeza ulendowu ndi wautali.”
8 Et il se leva; il mangea et il but, et il partit fortifié par ces aliments, et il marcha quarante jours et quarante nuits jusqu'au mont Horeb.
Tsono Eliya anadzuka nadya ndi kumwa. Atapeza mphamvu chifukwa cha chakudyacho, anayenda masiku 40, usana ndi usiku mpaka anafika ku Horebu, phiri la Mulungu.
9 Là, il entra dans la caverne; il en fit sa demeure, et la parole du Seigneur vint à lui, disant: Que fais-tu là, Elie?
Kumeneko analowa mʼphanga, nakhala komweko. Ndipo taonani, Yehova anayankhula naye kuti, “Eliya, ukuchita chiyani kuno?”
10 Le prophète répondit: J'ai eu le cœur rempli de zèle pour le Seigneur Tout-Puissant, parce que les fils d'Israël vous ont abandonné, qu'ils ont renversé vos autels, et tué par l'épée vos prophètes; seul j'ai survécu, et ils en veulent à ma vie.
Iye anayankha kuti, “Ndakhala wodzipereka kwambiri kwa Yehova Mulungu Wamphamvuzonse. Aisraeli asiya pangano lanu, agwetsa maguwa anu ansembe, ndipo apha aneneri anu ndi lupanga. Ndatsala ine ndekha ndipo tsopano akufuna kundipha.”
11 Or, la voix reprit: Tu partiras demain; mais tiens-toi devant le Seigneur sur la montagne, regarde: le Seigneur va passer. Aussitôt, voilà qu'un vent violent passa, déchirant la montagne, brisant les rochers, et le Seigneur n'était pas dans le vent; après le vent, il y eut un tremblement de terre, et le Seigneur n'était pas dans le tremblement de terre;
Yehova anati, “Tuluka ndipo ukayime pa phiri pamaso pa Yehova, pakuti Yehova ali pafupi kudutsa pamenepo.” Tsono mphepo yayikulu ndi yamphamvu inawomba ningʼamba mapiri ndi kuswa matanthwe pamaso pa Yehova, koma Yehova sanali mʼmphepomo. Itapita mphepoyo panachita chivomerezi, koma Yehova sanali mʼchivomerezicho.
12 Après le tremblement de terre, vint une flamme, et le Seigneur n'était pas dans la flamme; après la flamme, vint le murmure d'un souffle léger.
Chitapita chivomerezicho, panafika moto, koma Yehova sanali mʼmotomo. Ndipo utapita motowo, panamveka kamphepo kayaziyazi.
13 Quand Elie entendit ce souffle, il se voila le visage de son manteau de peau de brebis; puis, il sortit et il se tint à l'entrée de la caverne; alors, une voix s'approcha de lui, disant: Que fais-tu là, Elie?
Eliya atamva kamphepoko, anakokera chovala chake naphimba kumutu. Anatuluka ndipo anayima pa khomo la phanga. Ndipo panamveka mawu akuti, “Eliya, ukuchita chiyani kuno?”
14 Et le prophète répondit: J'ai eu le cœur plein de zèle pour le Seigneur Tout-Puissant, parce que les fils d'Israël ont abandonné votre alliance, renversé vos autels, et tué par l'épée vos prophètes; seul j'ai survécu, et ils en veulent à ma vie.
Iye anayankha kuti, “Ndakhala wodzipereka kwambiri kwa Yehova Mulungu Wamphamvuzonse. Aisraeli asiya pangano lanu, agwetsa maguwa anu ansembe, ndipo apha aneneri anu ndi lupanga. Ndatsala ine ndekha ndipo tsopano akufuna kundipha.”
15 Et le Seigneur lui dit: Pars, remets-toi en marche, prends le chemin du désert de Damas, tu iras, et tu sacreras Azaël pour être roi de Syrie.
Yehova anati kwa Eliyayo, “Bwerera njira imene unadzera, ndipo upite ku Chipululu cha ku Damasiko. Ukakafika kumeneko, ukadzoze Hazaeli kuti akhale mfumu ya ku Aramu.
16 Et tu sacreras Jéhu, fils de Namsi, pour être roi d'Israël; et tu sacreras Elisée, fils de Saphat, pour être prophète après toi.
Ukadzozenso Yehu mwana wa Nimisi kuti akhale mfumu ya Israeli, ndiponso ukadzoze Elisa mwana wa Safati wa ku Abeli-Mehola kuti akhale mneneri wolowa mʼmalo mwako.
17 Celui qu'épargnera l'épée d'Azaël, Jéhu le mettra à mort; celui qu'épargnera l'épée de Jéhu, Elisée le mettra à mort.
Yehu adzapha aliyense amene adzapulumuke ku lupanga la Hazaeli, ndipo Elisa adzapha aliyense amene adzapulumuke ku lupanga la Yehu.
18 Et je me réserve, en Israël, sept mille hommes, les seuls qui n'aient point fléchi le genou devant Baal, les seuls dont la bouche ne l'ait point adoré.
Komabe ndasunga anthu 7,000 ku Israeli, anthu onse amene mawondo awo sanagwadirepo Baala, onse amene pakamwa pawo sipanapsompsoneko fano lake.”
19 Et Elie partit de ce lieu, et il trouva Elisée, fils de Saphat; celui-ci labourait avec des bœufs; il avait devant lui douze attelages, et seul il les conduisait. Le prophète alla droit à Elisée, et jeta sur lui son manteau de peau de brebis.
Kotero Eliya anachoka kumeneko, nakapeza Elisa mwana wa Safati. Iye ankatipula ndi mapulawo khumi ndi awiri okokedwa ndi ngʼombe ziwiriziwiri zapamagoli, ndipo iye mwini ankayendetsa goli la khumi ndi chiwiri. Eliya anapita kumene anali namuveka chofunda chake.
20 Et Elisée abandonna ses bœufs; il suivit à grands pas Elie, et il lui dit: Je vais embrasser mon père; puis, je t'accompagnerai. Elie reprit: Reviens, car j'ai travaillé pour toi.
Pomwepo Elisa anasiya ngʼombe zake nathamangira Eliya. Iye anati, “Mundilole kuti ndikatsanzike abambo ndi amayi anga, ndipo kenaka ndidzakutsatani.” Eliya anayankha kuti, “Bwerera. Ine ndachita chiyani kwa iwe?”
21 Et il s'éloigna d'Elie, il prit ses couples de bœufs, il les sacrifia, il les fit cuire avec l'attirail des attelages, il les donna au peuple, et il mangea; enfin il rejoignit Elie et il le servit.
Choncho Elisa anamusiya Eliyayo nabwerera kwawo. Anatenga ngʼombe zake ziwiri zapagoli nazipha. Anatenga magoli a mapulawo ake nasonkhera moto kuphikira nyamayo ndipo anayipereka kwa anthu kuti adye. Ndipo ananyamuka natsatira Eliya ndi kukhala mtumiki wake.

< 1 Rois 19 >