< 1 Rois 15 >

1 En la dix-huitième année du règne de Jéroboam, fils de Nabat, Abiam, fils de Roboam, devint roi de Juda.
Mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yeroboamu mwana wa Nebati, Abiya anakhala mfumu ya Yuda,
2 Et il régna trois ans à Jérusalem; sa mère, fille d'Absalon, se nommait Maacha.
ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka zitatu. Amayi ake anali Maaka, mwana wa Abisalomu.
3 Et il marcha dans les péchés que son père avait faits devant lui, et son cœur ne fut point parfait avec le Seigneur son Dieu, comme l'était le cœur de son père David.
Abiya anachita zoyipa zonse zimene abambo ake anazichita. Sanali wangwiro pamaso pa Yehova Mulungu wake, monga linachitira kholo lake Davide.
4 Mais, à cause de David, le Seigneur lui donna un rejeton, afin de maintenir ses enfants après lui, et d'affermir Jérusalem;
Komabe chifukwa cha Davide, Yehova Mulungu wake anamupatsa nyale mu Yerusalemu pomupatsa mwana wolowa mʼmalo mwake ndi kumukhazikitsa kukhala wamphamvu mu Yerusalemu;
5 Parce que David avait fait ce qui est droit devant le Seigneur, et que, pendant toute sa vie, il ne s'était jamais écarté des commandements.
pakuti Davide anachita zolungama pamaso pa Yehova ndipo sanalephere kusunga chilichonse chimene Yehova anamulamula masiku onse a moyo wake kupatula nkhani ija ya Uriya Mhiti.
6
Panali nkhondo pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu masiku onse a moyo wa Abiya.
7 Quant au reste de l'histoire d'Abiam, n'est-il pas écrit au livre des Faits et gestes des rois de Juda? Et la guerre ne cessa pas entre Abiam et Jéroboam.
Tsono ntchito zina za Abiya, ndi zina zonse anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? Panali nkhondo pakati pa Abiya ndi Yeroboamu.
8 Et Abiam s'endormit avec ses pères, en la vingt-quatrième année du règne de Jéroboam; il fut enseveli auprès de ses pères en la ville de David; et son fils Asa régna à sa place.
Ndipo Abiya anamwalira nayikidwa mʼmanda momwe anayikidwa makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Asa, mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
9 Dans la vingt-quatrième année du règne de Jéroboam, roi d'Israël, Asa devint roi de Juda.
Mʼchaka cha makumi awiri cha Yeroboamu mfumu ya Israeli, Asa anakhala mfumu ya Yuda,
10 Il régna quarante et un ans à Jérusalem; sa mère, fille d'Absalon, se nommait Ana.
ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 41. Agogo ake akazi anali Maaka mwana wa Abisalomu.
11 Et Asa fit ce qui était droit devant le Seigneur, comme son père David.
Asa anachita zolungama pamaso pa Yehova monga anachitira Davide kholo lake.
12 Et il détruisit, dans la terre promise, les initiations, et il abolit les infâmes pratiques qu'avaient adoptées ses pères.
Iye anachotsa mʼdzikomo amuna onse ochita zadama pochita chipembedzo chawo ndiponso anachotsa mafano onse amene makolo ake anawapanga.
13 Il expulsa Ana, sa mère, pour qu'elle ne fût plus rien, parce qu'elle réunissait une association d'initiés dans son bois sacré, et il abattit ses refuges, et il les livra aux flammes dans la vallée de Cédron.
Iye anachotsanso gogo wake Maaka pa udindo wake wa amayi a mfumu, chifukwa choti anapanga fano lonyansa la Asera. Asa anagwetsa fanolo nakalitentha ku Chigwa cha Kidroni.
14 Mais il ne détruisit pas les hauts lieux; néanmoins, le cœur d'Asa fut parfait avec Dieu tout le temps qu'il vécut.
Ngakhale sanachotse malo opembedzerapo mafano, mtima wa Asa unali wodzipereka kwathunthu kwa Yehova masiku onse a moyo wake.
15 Et il transporta les colonnes de son père; il transporta dans le temple du Seigneur ses colonnes d'or et d'argent, et ses vases.
Asa anabweretsa ku Nyumba ya Yehova zinthu zimene abambo ake anazipereka, ndiponso zinthu zimene iye mwini anazipereka: zagolide, siliva ndi ziwiya zotengera.
16 Et la guerre ne cessa point entre Asa et Baasa, roi d'Israël, tout le temps de leur vie.
Panali nkhondo pakati pa Asa ndi Baasa mfumu ya Israeli nthawi yonse ya ulamuliro wawo.
17 Baasa, roi d'Israël, marcha contre Juda, et il se mit à bâtir Rhama, pour qu'il n'y eût personne qui pût sortir ni rentrer, en faveur du roi Asa.
Baasa mfumu ya Israeli anapita kukathira nkhondo dziko la Yuda, ndipo anamangira linga mzinda wa Rama kuletsa kuti wina aliyense asatuluke kapena kulowa mʼdziko la Asa, mfumu ya Yuda.
18 Asa, alors, prit tout l'argent et tout l'or qui se trouva dans les trésors du temple et du palais; il les confia à ses serviteurs, et il les envoya chez le fils d'Ader, fils de Tabremon, fils d'Esion, roi de Syrie, qui résidait à Damas, disant:
Tsono Asa anatenga siliva yense pamodzi ndi golide zimene zinatsala ku malo osungira chuma cha ku Nyumba ya Yehova ndiponso ku nyumba yake yaufumu. Anazipereka kwa atumiki ake, nawatuma kupita nazo kwa Beni-Hadadi mwana wa Tabirimoni, mwana wa Heziyoni, mfumu ya Aramu, amene ankakhala ku Damasiko ndipo anakamuwuza kuti,
19 Fais alliance entre moi et toi, entre la maison de mon père et la maison de ton père; voilà que je t'ai envoyé des présents: de l'argent et de l'or; viens, romps ton alliance avec Baasa, roi d'Israël, et il s'éloignera de moi.
“Tiyeni tigwirizane inu ndi ine, monga panali mgwirizano pakati pa abambo anu ndi abambo anga. Onani, ndikukutumizirani mphatso za siliva ndi golide. Tsopano kathetseni mgwirizano wanu ndi Baasa mfumu ya Israeli kuti andisiye.”
20 Et Ben-Ader écouta le roi Asa; il fit partir les chefs de ses armées contre les villes d'Israël; ils dévastèrent Ahion, Dan, Abel de la maison de Maacha, et tout Cennereth jusqu'aux confins de Nephthali.
Choncho Beni-Hadadi anamvera zimene ananena mfumu Asa ndipo anatumiza olamulira magulu ake ankhondo ku mizinda ya Israeli. Ndipo iye anagonjetsa Iyoni, Dani, Abeli-Beti-Maaka ndi dera lonse la Kinereti kuphatikiza dziko lonse la Nafutali.
21 Quand Baasa l'apprit, il abandonna les constructions de Rhama, et il retourna à Thersa.
Baasa atamva zimenezi, anasiya kumangira linga Rama ndipo anakakhala ku Tiriza.
22 Et le roi Asa, dans Enacim, donna ses ordres à tout Juda, ils enlevèrent les pierres de Rhama, et les bois que Baasa avait employés pour la bâtir. Ensuite, le roi s'en servit pour fortifier toutes les collines de Benjamin, et pour y établir la tour du guet.
Pamenepo Mfumu Asa analamula anthu onse a ku Yuda osasiya ndi mmodzi yemwe, ndipo anachotsa ku Rama miyala ndi matabwa amene Baasa ankamangira kumeneko. Zipangizo zimenezi Mfumu Asa inamangira linga la Geba ku Benjamini ndi la ku Mizipa.
23 Quant au reste de l'histoire d'Asa, à toutes les actions qu'il fit en sa puissance, à toutes les villes qu'il bâtit, ne sont-ils pas inscrits au livre des Faits et gestes des rois de Juda? Toutefois, dans sa vieillesse, il, perdit l'usage de ses pieds.
Tsono ntchito zina za Asa, za mphamvu zake ndi mizinda imene anayimanga ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? Koma pa nthawi ya ukalamba wake anadwala nthenda ya mapazi.
24 Et Asa s'endormit avec ses pères; il fut enseveli auprès d'eux en la ville de David, son aïeul. Et Josaphat, son fils, régna à sa place.
Ndipo Asa anamwalira nayikidwa mʼmanda momwe anayikidwa makolo ake mu mzinda wa Davide kholo lake. Ndipo Yehosafati mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
25 Nabat, fils de Jéroboam, devint roi d'Israël dans la seconde année du règne d'Asa en Juda, et Nabat régna deux ans.
Nadabu, mwana wa Yeroboamu anakhala mfumu ya Israeli mʼchaka chachiwiri cha Asa mfumu ya Yuda, ndipo analamulira Israeli zaka ziwiri.
26 Et il fit le mai devant le Seigneur; il marcha dans la voie de son père, et dans les péchés où il avait fait tomber Israël.
Nadabu anachita zoyipa pamaso pa Yehova, anayenda mʼnjira za abambo ake ndi mu uchimo womwe anachimwitsa nawo Israeli.
27 Et Baasa, fils d'Achias, l'assiégea à la tète de la maison de Bélaan, fils d'Achias; il l'entoura de palissades à Gabathon, ville des Philistins, que Nabat et tout Israël avaient investie.
Baasa mwana wa Ahiya, wa banja la Isakara anakonzera Nadabuyo chiwembu, ndipo anamukantha ku Gibetoni, mzinda wa Afilisti, pamene Nadabu ndi anthu onse a ku Israeli anali atawuzungulira.
28 Et Baasa le tua, la troisième année du règne d'Asa en Juda, et il régna à sa place.
Baasa anapha Nadabu mʼchaka chachitatu cha Asa, mfumu ya ku Yuda ndipo analowa ufumu mʼmalo mwake.
29 Dès qu'il fut proclamé, il extermina toute la maison de Jéroboam; nul de ceux des siens, qui avait souffle de vie, ne fut épargné, jusqu'à ce que tout eût péri, selon la parole que le Seigneur avait dite par la voix de son serviteur Achias le Silonite,
Iye atangoyamba kulamulira, anapha anthu onse a banja la Yeroboamu. Sanasiye ndi mmodzi yemwe wamoyo pa banjapo, koma anawononga anthu onse, molingana ndi mawu a Yehova amene anayankhula mwa mtumiki wake Ahiya wa ku Silo
30 Concernant les péchés de Jéroboam, et le péché où il avait fait tomber Israël pour irriter le Seigneur Dieu d'Israël.
chifukwa cha machimo amene Yeroboamu anachita, ndiponso kuchimwitsa anthu a ku Israeli, naputa mkwiyo wa Yehova Mulungu wa Israeli.
31 Quant au reste de l'histoire de Nabat, n'est-il pas écrit au livre des Faits et gestes des rois d'Israël?
Tsono ntchito za Nadabu ndi zina zonse zimene anazichita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
32 En la troisième année du règne d'Asa en Juda, Baasa, fils d'Achias, fut proclamé roi d'Israël, et il régna vingt-quatre ans à Thersa.
Panali nkhondo pakati pa Asa ndi Baasa mfumu ya Israeli pa nthawi yonse ya ulamuliro wawo.
33 En la troisième année du règne d'Asa en Juda, Baasa, fils d'Achias, fut proclamé roi d'Israël, et il régna vingt-quatre ans à Thersa.
Chaka chachitatu cha Asa mfumu ya Yuda, Baasa mwana wa Ahiya anakhala mfumu ya Aisraeli onse ku Tiriza, ndipo analamulira zaka 24.
34 Et il fit le mal devant le Seigneur; il marcha dans la voie de Jéroboam, fils de Nabat, et dans les péchés où il avait fait tomber Israël.
Anachita zoyipa pamaso pa Yehova, nayenda mʼnjira za Yeroboamu ndi kuchita tchimo lake limene linachimwitsa anthu a ku Israeli.

< 1 Rois 15 >