< 1 Chroniques 2 >

1 Voici les noms des fils d'Israël: Ruben, Siméon, Lévi, Juda, Issachar, Zabulon,
Ana a Israeli anali awa: Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda, Isakara, Zebuloni,
2 Dan, Joseph, Benjamin, Nephthali, Gad, Aser.
Dani, Yosefe, Benjamini, Nafutali, Gadi ndi Aseri.
3 Fils de Juda: Her, Onan, Sela; tous trois naquirent de la fille de Savas (Sué), la Chananéenne; et Her, le premier-né de Juda, fit le mal devant le Seigneur, qui le tua.
Ana a Yuda anali awa: Eri, Onani ndi Sela. Ana atatu awa anabereka ndi mkazi wa Chikanaani, Batisuwa. Eri, mwana woyamba wa Yuda anali woyipa kwambiri pamaso pa Yehova, kotero Yehova anamupha.
4 Et Thamar, bru de Juda, enfanta Pharès et Zara; en tout: cinq fils de Juda.
Mpongozi wake Tamara anamuberekera Perezi ndi Zera. Ana onse a Yuda analipo asanu.
5 Fils de Pharès: Esron et Jemuhel.
Ana a Perezi anali awa: Hezironi ndi Hamuli.
6 Fils de Zara: Zambri, Etham, Aimuan, Calchal et Darad; en tout: cinq.
Ana a Zera anali awa: Zimuri, Etani, Hemani, Kalikoli ndi Dara. Onse analipo asanu.
7 Fils de Charmi: Achar, le perturbateur d'Israël, qui désobéit au sujet de l'anathème.
Mwana wa Karimi anali Akani, amene anabweretsa mavuto pakati pa Israeli pamene anatenga zinthu zoyenera kuwonongedwa.
8 Fils d'Etham: Azarias.
Mwana wa Etani anali Azariya.
9 Fils d'Esron, qui lui furent enfantés: Jeraméel, Aram et Caleb.
Ana amene anabadwa kwa Hezironi anali: Yerahimeeli, Ramu ndi Kelubai.
10 Aram engendra Aminadab; Aminadab engendra Nahasson, chef de la maison de Juda.
Ramu anabereka Aminadabu ndipo Aminadabu anali abambo ake a Naasoni, mtsogoleri wa fuko la Yuda.
11 Nahasson engendra Salmon; Salmon engendra Booz;
Naasoni anabereka Salima, Salima anabereka Bowazi,
12 Booz engendra Obed; Obed engendra Jessé;
Bowazi anabereka Obedi ndipo Obedi anabereka Yese.
13 Jessé engendra son premier-né Eliab, le second Aminadab, le troisième Samaa,
Yese anabereka Eliabu mwana wake woyamba, wachiwiri Abinadabu, wachitatu Simea,
14 Nathanael le quatrième, Zabdé le cinquième,
wachinayi Netaneli, wachisanu Radai,
15 Azam le sixième, et David le septième.
wachisanu ndi chimodzi Ozemu ndi wachisanu ndi chiwiri Davide.
16 Et leurs sœurs furent: Sarvia et Abigaïl. Les fils de Sarvia furent: Abessa, Joab et Asaël; trois.
Alongo awo anali Zeruya ndi Abigayeli. Ana atatu a Zeruya anali Abisai Yowabu ndi Asaheli.
17 Abagaïl enfanta Amessab, et le père d'Amessab fut Jolhor l'Ismaélite.
Abigayeli anali amayi ake a Amasa amene abambo ake anali Yeteri wa fuko la Ismaeli.
18 Caleb, fils d'Esron, prit pour femmes Gazuba et Jerioth; voici ses fils: Jasar, Subab et Ardon.
Kalebe mwana wa Hezironi anabereka ana mwa Azuba mkazi wake (ndi mwa Yerioti). Ana a mkaziyo anali awa: Yeseri, Sobabu ndi Aridoni.
19 Et Gazuba mourut, et Caleb prit pour femme Ephratha, et elle lui enfanta Hur.
Azuba atamwalira, Kalebe anakwatira Efurata, amene anamuberekera Huri.
20 Hur engendra Urias; Urias engendra Beseléel.
Huri anabereka Uri ndipo Uri anabereka Bezaleli.
21 Après cela, Esron eut commerce avec la fille de Machir, père de Galaad, et il la prit pour femme; il avait alors soixante-cinq ans, et elle lui enfanta Seruch.
Patapita nthawi, Hezironi anagona ndi mwana wamkazi wa Makiri abambo ake a Giliyadi (iye anamukwatira ali ndi zaka 60) ndipo anamuberekera Segubu.
22 Seruch engendra Jaïr; il possédait vingt-trois villes en Galaad.
Segubu anabereka Yairi, amene anali ndi mizinda 23 ku Giliyadi.
23 Il prit de plus Gessur et Aram, villes de Jaïr, parmi les siennes, et la terre de Canath avec ses villes: soixante villes; toutes appartenaient aux fils de Machir, père de Galaad.
(Koma Gesuri ndi Aramu analanda Havoti Yairi komanso Kenati ndi madera ake onse ozungulira, mizinda makumi asanu ndi umodzi). Onsewa anali adzukulu, a Makiri abambo ake a Giliyadi.
24 Après la mort d'Esron, Caleb épousa Ephratha; or, Abia, femme d'Esron, lui avait enfanté Ascho, père de Thécoé.
Atamwalira Hezironi ku Kalebe Efurata, Abiya mkazi wa Hezironi anamuberekera Asihuri abambo a Tekowa.
25 Les fils de Jeraméel, premier-né d'Esron, furent: Ram, premier-né; puis, Banaa, Aram et Asan, son frère.
Ana a Yerahimeeli, mwana woyamba wa Hezironi anali: Ramu, mwana wake woyamba, Buna, Oreni, Ozemu ndi Ahiya.
26 Et Jeraméel avait une autre femme qui se nommait Atara; celle-ci fut la mère d'Ozom.
Yerahimeeli anali ndi mkazi wina amene dzina lake linali Atara, amene anali amayi a Onamu.
27 Les fils de Ram, premier-né de Jeraméel, furent: Mass, Jamin et Acor.
Ana a Ramu, mwana woyamba wa Yerahimeeli, anali awa: Maazi, Yamini ndi Ekeri.
28 Les fils d'Ozom furent: Samaï et Jadaé, et les fils de Samaï: Nadab et Abisur.
Ana a Onamu anali awa: Shamai ndi Yada. Ana a Shamai anali awa: Nadabu ndi Abisuri.
29 La femme d'Abisur se nommait Abihaïl, et elle lui enfanta Achobor et Moêl.
Mkazi wa Abisuri anali Abihaili, amene anamuberekera Ahibani ndi Molidi.
30 Fils de Nadab: Salad et Aphaïn; Salad mourut sans enfants.
Ana a Nadabu anali awa: Seledi ndi Apaimu. Koma Seledi anamwalira wopanda ana.
31 Fils d'Aphaïn: Iséuniel; fils d'Isémiel: Sosan; fils de Sosan: Dadaï.
Ana a Apaimu anali awa: Isi, amene anabereka Sesani. Sesani anabereka Ahilai.
32 Fils de Dadaï: Achisamas, Jéther, Jonatham; Jéther mourut sans enfants.
Ana a Yada, mʼbale wa Samai, anali awa: Yereri ndi Yonatani. Koma Yeteri anamwalira wopanda ana.
33 Fils de Jonathan: Phaleth et Ozam; voilà les fils de Jonathan.
Ana a Yonatani anali awa: Peleti ndi Zaza. Amenewa anali adzukulu a Yerahimeeli.
34 Sosan n'eut pas de fils, mais des filles; or, il avait un serviteur égyptien qui se nommait Johel.
Sesani sanabereke ana aamuna koma aakazi okhaokha. Iye anali ndi wantchito wa ku Igupto, dzina lake Yariha.
35 Et Sosan donna sa fille, pour femme, à son serviteur Johel; elle lui enfanta Ethi.
Sesani anapereka mwana wake wamkazi kwa Yariha wantchito wake kuti amukwatire ndipo anamuberekera Atayi.
36 Et Ethi engendra Nathan, et Nathan engendra Zabed.
Atayi anali abambo ake a Natani, Natani anali abambo ake a Zabadi,
37 Zabed engendra Aphamel, et Aphamel engendra Obed.
Zabadi anali abambo a Efilali, Efilali anali abambo a Obedi,
38 Obed engendra Jéhu, et Jéhu engendra Azarias.
Obedi anali abambo a Yehu, Yehu anali abambo a Azariya,
39 Azarias engendra Hellès, et Hellès engendra Eléaza.
Azariya anali abambo a Helezi, Helezi anali abambo a Eleasa,
40 Eléaza engendra Sosomaï, et Sosomaï engendra Salum.
Eleasa anali abambo ake a Sisimai, Sisimai anali abambo a Salumu,
41 Salum engendra Jéhémie; Jéhémie engendra Elisama, et Elisama engendra Ismaël.
Salumu anali abambo a Yekamiya, Yekamiya anali abambo a Elisama.
42 Fils de Caleb, frère de Jeraméel Marisa, premier-né; c'est le père de Siph; Marisa eut encore des fils, il fut le père d'Hébron.
Ana a Kalebe mʼbale wa Yerahimeeli anali awa: Mesa mwana wachisamba, anali abambo a Zifi, ndipo mwana wake Maresa anali abambo a Hebroni.
43 Fils d'Hébron: Coré, Thaphus, Rhicom et Samaa.
Ana a Hebroni anali awa: Kora, Tapuwa, Rekemu ndi Sema.
44 Samaa engendra Rahem, père de Jéclan, et Jéclan engendra Samaï.
Sema anali abambo ake Rahamu ndipo Rahamu anali abambo a Yorikeamu. Rekemu anali abambo a Samai.
45 Mahon fut son fils, et Mahon fut le père de Bethsur.
Mwana wa Samai anali Maoni, ndipo Maoni anali abambo a Beti Zuri.
46 Gaïpha, concubine de Caleb, enfanta Aram, et Mosa et Gézué.
Efai, mzikazi wa Kalebe, anali amayi a Harani, Moza ndi Gazezi. Harani anali abambo a Gazezi.
47 Fils d'Adaï: Rahem, Joatham, Sagar, Phalec, Gaïpha et Sagaé.
Ana a Yahidai anali awa: Regemu, Yotamu, Gesani, Peleti, Efai ndi Saafi.
48 Mocha, concubine de Caleb, enfanta Saber et Tharam.
Maaka mzikazi wa Kalebe anali mayi Seberi ndi Tirihana.
49 Sagaé engendra le père de Madmena, et Sahu, père de Mahabena, et le père de Gébal; la fille de Caleb s'appelait Ascha.
Iye anaberekanso Saafi abambo a Madimena ndi Seva abambo a Makibena ndi Gibeya. Mwana wamkazi wa Kalebe anali Akisa.
50 Voilà les fils de Caleb. Voici les fils d'Hur, premier-né d'Ephratha: Sobal, père de Cariathiarim,
Izi zinali zidzukulu za Kalebe. Ana a Huri mwana wachisamba wa Efurata anali awa: Sobala abambo a Kiriati Yearimu,
51 Salomon, père de Bétha, Lammon, père de Béthalaem, et Arim, père de Bethgedor.
Salima abambo a Betelehemu ndi Harefu abambo ake a Beti-Gadera.
52 Fils de Sobal, père de Cariathiarim: Araa, Aïsi, Ammanith
Zidzukulu za Sobala abambo a Kiriati Yearimu zinali izi: Harowe, theka la banja la Manahati,
53 Et Umasphaé; villes de Jdir: Ethalim, Miphitim, Hésamathim et Hémasaraïm, d'où sont sortis les Sarathéens et les fils d'Esthaam.
ndipo mabanja a Kiriati-Yeyarimu anali awa: Aitiri, Aputi, Asumati ndi Amisirai. Azorati ndi Aesitaoli anachokera kwa amenewa.
54 Fils de Salomon: Béthalaem le Netophatite, Ataroth de la maison de Joab, la moitié de Manathi, et Esari.
Zidzukulu za Salima zinali izi: Betelehemu, Anetofati, Atiroti-Beti-Yowabu, theka la banja la Manahati, Azori,
55 Familles de lettrés, demeurant en Jabis: Thargathiim, et Samathiim et Sohathim. Ce sont les Cinéens, issus d'Emath, père de la maison de Rhéchab.
ndiponso mabanja a alembi amene amakhala ku Yabesi: Atiroti, Asimeati ndiponso Asukati. Awa ndi Akeni amene anachokera kwa Hamati, kholo la Arekabu.

< 1 Chroniques 2 >