< Psaumes 7 >

1 Chigayon de David, qu’il chanta à l’Eternel à propos de Couchi, le Benjamite. Eternel, mon Dieu, en toi je m’abrite; assiste-moi contre tous mes persécuteurs, délivre-moi.
Sigioni wa Davide, amene anayimbira Yehova zokhudza Kusi, wa fuko la Benjamini. Inu Yehova Mulungu wanga, Ine ndikuthawira kwa Inu; pulumutseni ndi kundilanditsa kwa onse amene akundithamangitsa,
2 Sans cela, on déchirerait, tel un lion, ma personne, on me mettrait en pièces, et nul ne me sauverait.
mwina angandikadzule ngati mkango, ndi kundingʼamba popanda wondipulumutsa.
3 Eternel, mon Dieu, si j’ai agi de la sorte, s’il y a de l’iniquité en mes mains:
Inu Yehova Mulungu wanga, ngati ndachita izi ndipo ndapezeka wolakwa,
4 si j’ai rendu la pareille à qui m’a fait du mal, et dépouillé qui m’a pris en haine sans motif,
ngati ndachita zoyipa kwa iye amene ndili naye pa mtendere, kapena popanda chifukwa ndalanda mdani wanga,
5 que l’ennemi se mette à ma poursuite et m’atteigne! qu’il broie ma vie sur le sol, et traîne mon honneur dans la poussière! (Sélah)
pamenepo lolani adani anga andithamangitse ndi kundipitirira, lolani kuti moyo wanga aupondereze pansi ndipo mundigoneke pa fumbi. (Sela)
6 Lève-toi, Seigneur, dans ta colère, oppose-toi à la fureur de mes adversaires, et, en ma faveur, exerce la justice que tu as proclamée.
Nyamukani Yehova, mu mkwiyo wanu; nyamukani kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga. Dzukani Mulungu wanga, lamulirani chilungamo chanu.
7 Que l’assemblée des peuples se groupe autour de toi! t’élevant au-dessus d’elle, regagne ta sublime résidence.
Lolani gulu la anthu a mitundu ina lisonkhane mokuzungulirani. Alamulireni muli kumwambako;
8 Seigneur, qui juges les nations, rends-moi justice, selon ma vertu et ma droiture.
Yehova aweruzeni anthu a mitundu inayo. Ndiweruzeni Yehova, monga mwa chilungamo changa, monga mwa moyo wanga wangwiro, Inu Wammwambamwamba.
9 Que la méchanceté des impies ait donc un terme! Affermis le juste, ô toi qui sondes cœurs et reins, Dieu équitable!
Inu Mulungu wolungama, amene mumasanthula maganizo ndi mitima, thetsani chiwawa cha anthu oyipa ndipo wolungama akhale motetezedwa.
10 Ma sauvegarde est en Dieu: il secourt les cœurs droits.
Chishango changa ndi Mulungu Wammwambamwamba, amene amapulumutsa olungama mtima.
11 Dieu est un juge équitable, le Tout-Puissant fait sentir sa colère tous les jours:
Mulungu amaweruza molungama, Mulungu amene amaonetsa ukali wake tsiku ndi tsiku.
12 si l’on ne s’amende pas, il aiguise son glaive, il bande son arc et l’ajuste.
Ngati munthu satembenuka, Mulungu adzanola lupanga lake, Iye adzawerama ndi kukoka uta.
13 Il s’arme d’engins meurtriers, de ses flèches il fait des brandons.
Mulungu wakonza zida zake zoopsa; Iye wakonzekera mivi yake yoyaka moto.
14 Voyez, le méchant ourdit l’iniquité, il conçoit le mal et enfante le mensonge;
Taonani, munthu woyipa amalingalira zoyipa zokhazokha nthawi zonse. Zochita zake ndi zosokoneza ndi zovutitsa anthu ena.
15 il a creusé une fosse et l’a rendue profonde, mais il glisse dans le précipice qu’il a préparé.
Iye amene akumba dzenje ndi kulizamitsa amagwera mʼdzenje limene wakumbalo.
16 Son injustice lui retombe sur la tête, et sur son crâne sa cruauté s’abat.
Mavuto amene amayambitsa amamubwerera mwini; chiwawa chake chimatsikira pa mutu wake womwe.
17 Je rendrai grâce à l’Eternel pour sa justice, et je chanterai le nom du Seigneur, du Très-Haut.
Ine ndidzayamika Yehova chifukwa cha chilungamo chake; ndipo ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina la Yehova Wammwambamwamba.

< Psaumes 7 >