< Néhémie 11 >

1 Les notables parmi le peuple s’établirent à Jérusalem; le reste du peuple désigna, par la voie du sort, un sur dix pour habiter Jérusalem, la ville sainte, neuf dixièmes restant dans les autres villes.
Nthawi imeneyo atsogoleri a anthu ankakhala ku Yerusalemu. Tsono anthu ena onse anachita maere kuti apeze munthu mmodzi pa anthu khumi aliwonse kuti azikhala ku Yerusalemu, mzinda wopatulika. Anthu asanu ndi anayi otsalawo ankakhala mʼmidzi yawo.
2 Le peuple bénit tous les hommes qui s’offraient d’eux-mêmes à habiter Jérusalem.
Anthu anayamikira onse amene anadzipereka kuti azikhala mu Yerusalemu.
3 Voici les chefs de la province qui se fixèrent à Jérusalem; quant aux villes de Juda, chacun s’était établi dans sa propriété, dans sa ville respective, Israélites, prêtres, Lévites, serviteurs du temple et descendants des esclaves de Salomon.
Aisraeli wamba, ansembe, Alevi, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu ndiponso zidzukulu za antchito a Solomoni ankakhala mʼmidzi yawo, aliyense mu dera lake. Koma atsogoleri a chigawo cha Yuda anali atakhazikika mu Yerusalemu.
4 A Jérusalem s’établirent donc une partie des enfants de Juda et des enfants de Benjamin des enfants de Juda: Ataïa, fils d’Ouzzia, fils de Zacharie, fils d’Amaria, fils de Chefatia, fils de Mahalalel, descendants de Péreç;
Ku Yerusalemu kunkakhalanso anthu ena a mafuko a Yuda ndi Benjamini. Ena mwa zidzukulu za Yuda ndi awa: Ataya, mwana wa Uziya, mwana wa Zekariya, mwana wa Amariya mwana wa Sefatiya, mwana wa Mahalaleli. Onsewa anali ana a Perezi.
5 Maassèya, fils de Baruch, fils de Kol-Hozé, fils de Hazaïa, fils d’Adaïa, fils de Yoyarib, fils de Zacharie, fils de Chiloni.
Ena ndi awa: Maaseya mwana wa Baruki, mwana wa Koli-Hoze mwana wa Hazaya, mwana wa Adaya, mwana wa Yowaribu, Zekariya mwana wa Msiloni.
6 Tous les descendants de Péreç, établis à Jérusalem, étaient au nombre de quatre-cent soixante-huit, tous hommes vaillants.
Zidzukulu zonse za Perezi, anthu amphamvu zawo amene ankakhala ku Yerusalemu analipo anthu okwanira 468.
7 Voici les enfants de Benjamin: Sallou, fils de Mechoullam, fils de Joëd, fils de Pedaïa, fils de Kolaïa, fils de Maassèya, fils d’Itiël, fils d’Isaïe;
Nazi zidzukulu za Benjamini: Salu mwana wa Mesulamu, mwana wa Yowedi, mwana wa Pedaya, mwana wa Kolaya, mwana wa Maaseiya, mwana wa Itieli, mwana wa Yesaiya.
8 après lui, Gabbaï, Sallaï, au nombre de neuf cent vingt-huit;
Abale ake anali Gabayi ndi Salaya. Onse pamodzi anali 928.
9 Joël, fils de Zikhri, était leur chef, et Juda, fils de Hassenoua, commandait la ville en second.
Yoweli mwana wa Zikiri ndiye anali mtsogoleri wawo, ndipo Yuda mwana wa Hasenuya ndiye amayangʼanira chigawo cha chiwiri cha mzinda.
10 Parmi les prêtres: Yedaïa, fils de Joyarib, Yakhîn;
Ansembe anali awa: Yedaya mwana wa Yowaribu; Yakini;
11 Seraïa, fils de Hilkia, fils de Mechoullam, fils de Çadok, fils de Meraïot, fils d’Ahitoub préposé au temple de Dieu;
Seraya mwana wa Hilikiya mwana wa Mesulamu, mwana wa Zadoki, mwana wa Merayoti, mwana wa Ahitubi amene anali woyangʼanira Nyumba ya Mulungu,
12 leurs frères, chargés de la besogne du temple, au nombre de huit cent vingt-deux; Adaïa, fils de Yeroham, fils de Pelalia, fils d’Amci, fils de Zacharie, fils de Pachhour, fils de Malkia;
ndi abale awo, amene ankagwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu. Onse pamodzi anali 822. Panalinso Adaya mwana wa Yerohamu, mwana wa Pelaliya, mwana wa Amizi, mwana wa Zekariya, mwana wa Pasi-Huri, mwana wa Malikiya,
13 ses frères, chefs de famille, au nombre de deux cent quarante-deux; Amachsaï, fils d’Azarel, fils d’Ahzaï, fils de Mechillêmot, fils d’Immêr;
ndi abale ake, amene anali atsogoleri a mabanja. Onse pamodzi anali 242. Kuphatikiza apo panalinso Amasisai mwana wa Azaireli, mwana wa Ahazayi, mwana wa Mesilemoti, mwana wa Imeri
14 leurs frères, tous hommes vaillants, au nombre de cent vingt-huit. Le chef qui les dirigeait était Zabdiêl, fils de Haggedolîm.
ndi abale ake. Onse pamodzi anali 128 ndipo anali anthu olimba mtima kwambiri. Mtsogoleri wawo wamkulu anali Zabidieli mwana wa Hagedolimu.
15 Parmi les Lévites: Chemaïa, fils de Hachoub, fils d’Azrikâm, fils de Hachabia, fils de Bounni;
Alevi anali awa: Semaya mwana wa Hasubu, mwana wa Azirikamu, mwana wa Hasabiya, mwana wa Buni.
16 Chabbetaï, Yozabad, préposés aux travaux extérieurs de la maison de Dieu, comme faisant partie des chefs des Lévites;
Sabetayi ndi Yozabadi anali atsogoleri amene ankayangʼanira ntchito ya kunja kwa Nyumba ya Mulungu.
17 Mattania, fils de Mikha, fils de Zabdi, fils d’Assaph qui était le coryphée entonnant les eulogies pendant la prière Bakboukia, son second parmi ses frères, Abda, fils de Chammoua, fils de Galal, fils de Yedouthoun.
Mataniya mwana wa Mika, mwana wa Zabidi, mwana wa Asafu ndiye anali wotsogolera pa mapemphero achiyamiko. Panalinso Bakibukiya amene anali wachiwiri pakati pa abale ake. Kuwonjezera apo panalinso Abida mwana wa Samuwa, mwana wa Galali, mwana wa Yedutuni.
18 Tous les Lévites, dans la ville sainte, étaient au nombre de deux cent quatre-vingt-quatre.
Alevi onse amene anali mu mzinda woyera analipo 284.
19 Les portiers, Akkoub, Talmôn et leurs frères, qui étaient de garde aux portes, atteignaient le nombre de cent soixante-douze.
Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Akubu, Talimoni ndi abale awo. Onse pamodzi anali 172.
20 Le reste des Israélites, les prêtres, les Lévites demeuraient dans toutes les villes de Juda, chacun dans sa propriété.
Aisraeli ena onse pamodzi ndi ansembe ndi Alevi ankakhala mʼmizinda ya Yuda, ndipo aliyense ankakhala mʼdera la makolo ake.
21 Les serviteurs du temple étaient établis sur la colline fortifiée, leurs chefs étant Ciha et Ghichpa.
Koma antchito a ku Nyumba ya Mulungu ankakhala pa phiri la Ofeli, ndipo Ziha ndi Gisipa ndiwo anali kuwayangʼanira.
22 Le chef des Lévites à Jérusalem était Ouzzi, fils de Bâni, fils de Hachabia, fils de Mattania, fils de Mikha, faisant partie des descendants d’Assaph, les chanteurs, chargés du service intérieur de la maison de Dieu;
Wamkulu wa Alevi mu Yerusalemu anali Uzi mwana wa Bani, mwana wa Hasabiya, mwana wa Mataniya, mwana wa Mika. Uzi anali mmodzi wa zidzukulu za Asafu, amene anali oyimba nyimbo pa nthawi zachipembedzo mʼNyumba ya Mulungu.
23 car il existait un règlement royal à leur égard et un contrat assurant aux chanteurs l’entretien de chaque jour.
Pakuti mfumu inalamula kuti tsiku ndi tsiku pa nthawi zachipembedzo oyimba nyimbowo azikhalapo.
24 Petahia, fils de Mechêzabel, des descendants de Zérah, fils de Juda, était le mandataire du roi en tout ce qui concernait le peuple.
Petahiya mwana wa Mesezabeli, mmodzi mwa zidzukulu za Zera mwana wa Yuda ndiye ankayimirira Aisraeli pa bwalo la mfumu ya Perisiya.
25 Quant aux bourgades avec leur banlieue, des descendants de Juda occupaient Kiryath-Arba et ses dépendances, Dibôn et ses dépendances, Yekabceêl et ses villages;
Anthu ena a fuko la Yuda ankakhala ku Kiriyati-Ariba ndi midzi yake, ku Diboni ndi midzi yake, ku Yekabizeeli ndi midzi yake,
26 Yêchoua, Molada et Beth-Pélet;
ku Yesuwa, Molada, Beti-Peleti,
27 Haçar-Choual, Bersabée et ses dépendances;
Hazari-Suwali, Beeriseba ndi midzi yawo.
28 Ciklag, Mekhona et ses dépendances;
Ku Zikilagi, Mekona ndi midzi yawo,
29 En-Rimmôn, Çorea et Yarmout:
ku Eni-Rimoni, Zora, Yarimuti,
30 Zanoah, Adoullam et leurs villages, Lakhich avec sa banlieue, Azêka avec ses dépendances; ils occupaient donc le pays depuis Beer Sheva jusqu’à la vallée de Hinnom.
Zanowa, Adulamu ndi midzi yake, ku Lakisi ndi minda yake, ku Beeriseba mpaka ku chigwa cha Hinomu.
31 Les descendants de Benjamin occupaient, en partant de Ghéba, Mikhmach, Aïa, Béthel et ses dépendances;
Nazonso zidzukulu za Benjamini zinkakhala mʼdera lawo kuyambira ku Geba mpaka ku Mikimasi, Ayiya, Beteli ndi midzi yake,
32 Anatot, Nob, Anania;
ku Anatoti, Nobu ndi Ananiya,
33 Haçor, Rama, Ghittaïm;
ku Hazori, Rama ndi Gitaimu,
34 Hadid, Ceboïm, Neballat;
ku Hadidi, Zeboimu ndi Nebalati,
35 Lod, Ono, la vallée des artisans.
ku Lodi, Ono ndi ku chigwa cha Amisiri.
36 Quelques-uns des Lévites demeuraient dans des parties de Juda rattachées à Benjamin.
Magulu ena a Alevi a ku Yuda ankakhala ku Benjamini.

< Néhémie 11 >