< Job 8 >

1 Bildad de Chouha prit la parole et dit:
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 Combien de temps encore tiendras-tu ces discours, et les paroles de ta bouche seront-elles comme un vent impétueux?
“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
3 Dieu fait-il fléchir le bon droit? Le Tout-Puissant fausse-t-il la justice?
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 Si tes fils lui ont manqué, il les aura laissés succomber sous 'le poids de leur faute.
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
5 Mais si toi, tu te mets à la recherche de Dieu, si tu te tournes en suppliant vers le Tout-Puissant,
Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 si tu es innocent et droit, ah! certes, sa bonté s’éveillera en ta faveur, il rendra la paix à la demeure qui abrite ta piété.
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
7 Humbles auront été tes débuts, mais combien brillant sera ton avenir!
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
8 Interroge, en effet, les générations primitives, fais appel à l’expérience de leurs ancêtres:
“Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 nous, nous ne sommes que d’hier et nous ne savons rien, car nos jours sur la terre ne sont qu’une ombre.
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 Eh bien! Ils t’instruiront, eux, ils te parleront et du fond de leur cœur ils tireront ce discours:
Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 "Le papyrus pousse-t-il en l’absence de marais, le jonc se développe-t-il sans eau?
Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 A peine monté en tige, alors qu’il ne peut être coupé, il devient sec avant toute autre herbe."
Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 Tel est le sort de ceux qui oublient Dieu: l’espoir de l’impie sera déçu.
Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 Sa confiance sera brisée et son assurance n’est qu’une toile d’araignée.
Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 Il s’appuiera sur sa maison, mais elle ne tiendra pas debout; il s’y cramponnera, mais elle ne résistera point.
Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 Qu’il maintienne même sa sève sous les rayons du soleil et étende ses rejetons à travers son jardin;
Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 que ses racines s’entrelacent autour du roc et percent jusqu’à la couche de pierres,
mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 dès qu’on l’arrache de sa place, celle-ci le reniera en disant: "Je ne t’ai jamais vu!"
Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 Vois, c’est là le triomphe de sa destinée; d’autres pousseront sur ce même sol.
Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 C’Est que Dieu ne repousse pas l’homme intègre, pas plus qu’il n’accorde l’appui de sa main aux malfaiteurs.
“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 Il finira pas remplir ta bouche de joie et tes lèvres de cris de victoire.
Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 Tes ennemis seront couverts de honte: la tente des méchants ne sera plus.
Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

< Job 8 >