< Job 26 >

1 Job reprit la parole et dit:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Comme tu sais secourir la faiblesse, soutenir les bras défaillants!
“Wamuthandizadi munthu wopanda mphamvu! Walimbitsadi dzanja la munthu wofowoka!
3 Comme tu sais conseiller l’ignorance et répandre la science à profusion!
Wapereka malangizo kwa munthu amene alibe nzeru! Ndipotu waonetsadi nzeru zochuluka!
4 A l’adresse de qui as-tu débité ton discours et de qui l’inspiration a-t-elle passé par ta bouche?
Kodi wakuthandiza ndani kuti uyankhule mawu awa? Ndipo ndi mzimu wa yani umene unayankhula pakamwa pako?
5 Les ombres des trépassés se prennent à trembler au-dessous des eaux et de leurs habitants.
“Mizimu ya anthu akufa ikunjenjemera pansi pa madzi, ndi zonse zokhala mʼmadzimo.
6 Le Cheol est à nu devant lui et l’abîme n’a pas de voile. (Sheol h7585)
Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu; chiwonongeko ndi chosaphimbidwa. (Sheol h7585)
7 Il étend le Septentrion sur le vide, il suspend la terre sur le néant.
Mulungu anayala thambo la kumpoto pa phompho; Iye anakoloweka dziko lapansi mʼmalo mwake pamene panali popanda nʼkanthu komwe.
8 Il emmagasine les eaux dans ses nuages, sans que la nuée crève sous leur poids.
Amasunga madzi ambiri mʼmitambo yake, koma mitamboyo siphulika chifukwa cha kulemera kwa madziwo.
9 Il dérobe la vue de son trône, en déroulant sur lui sa nuée.
Iye amaphimba mwezi wowala, amawuphimba ndi mitambo yake.
10 Il a tracé un cercle sur la surface des eaux, jusqu’au point où la lumière confine aux ténèbres.
Mulungu anawalembera madzi malire wonga uta, kukhala malire pakati pa kuwunika ndi mdima.
11 Les colonnes du ciel frémissent et s’effarent sous sa menace.
Mizati yochirikiza mitambo yakumwamba imanjenjemera, ndi kudabwa pa kudzudzula kwake.
12 Par sa force, il dompte la mer et, par sa sagesse, il en brise l’orgueil.
Ndi mphamvu zake anatontholetsa nyanja; ndi nzeru zake anakantha chirombo cha mʼmadzi chija chotchedwa Rahabe.
13 Par son souffle, le ciel s’éclaircit; sa main transperce le serpent aux replis tortueux.
Ndi mpweya wake anayeretsa zamumlengalenga, dzanja lake linapha chinjoka chothawa chija.
14 Eh bien! Ce n’est là qu’une partie de ses actes; quel faible écho nous en avons recueilli! Mais le tonnerre de ses exploits, qui pourrait le concevoir?
Zimenezi ndi pangʼono chabe mwa ntchito yake; tingomva pangʼono za Iye ngati kunongʼona! Kodi ndani angathe kudziwa kukula kwa mphamvu zake?”

< Job 26 >