< Jérémie 47 >

1 Telle est la communication que fit l’Eternel au prophète Jérémie concernant les Philistins, avant la défaite infligée par Pharaon à Gaza:
Uthenga umene Yehova anamupatsa mneneri Yeremiya wonena za Afilisti, Farao asanathire nkhondo Gaza ndi uwu:
2 "Ainsi parle l’Eternel: Voici que des flots s’avancent du Nord et deviennent un torrent impétueux, submergeant la terre et ce qu’elle renferme, les villes et ceux qui y demeurent. Les hommes poussent des cris et tous les habitants du pays se lamentent.
Yehova akuti, “Taonani mmene madzi akubwerera kuchokera kumpoto; adzasanduka mtsinje wosefukira ndi a mkokomo. Adzasefukira mʼdziko monse ndi kumiza chilichonse mʼmenemo, mizinda ndi onse okhala mʼmenemo. Anthu adzafuwula; anthu onse okhala mʼdzikomo adzalira
3 Au trot bruyant des sabots des fiers coursiers, au roulement des chars, au fracas de leurs roues, les pères n’ont plus de regard pour leurs enfants, tant ils sont abattus,
akadzamva mgugu wa ngʼombe zazimuna zothamanga, phokoso la magaleta ake ndi kulira kwa mikombero yake. Makolo sadzatembenuka kuti athandize ana awo; manja awo adzangoti khoba.
4 à cause de l’arrivée de ce jour qui verra ruiner tous les Philistins, enlever à Tyr et à Sidon leurs derniers auxiliaires, car l’Eternel veut perdre les Philistins, ces émigrés de l’île de Caphtor.
Pakuti tsiku lafika lowononga Afilisti onse ndi kupha onse otsala, onse amene akanatha kuthandiza Turo ndi Sidoni. Yehova ali pafupi kuwononga Afilisti, otsala ochokera ku zilumba za ku Kafitori.
5 Gaza est atteinte de calvitie, Ascalon est anéantie avec le reste de leur plaine jusqu’à quand te feras-tu des incisions?
Anthu a ku Gaza ameta mipala; anthu a ku Asikeloni akhala chete. Inu otsala a ku chigwa, mudzakhala mukudzichekacheka mpaka liti?
6 Holà! Glaive du Seigneur, quand donc te reposeras-tu enfin? Rentre dans ton fourreau, apaise-toi, fais trève!
“Mukulira kuti, ‘Aa, lupanga la Yehova, kodi udzapumula liti? Bwerera mʼmalo ako; ukhale momwemo ndipo ukhale chete.’
7 Mais comment se tiendrait-il coi, alors que l’Eternel lui a donné des ordres? A Ascalon et sur les bords de la mer, il lui a assigné un rendez-vous."
Koma lupangalo lidzapumula bwanji pamene Yehova walilamulira kuti lithire nkhondo Asikeloni ndi anthu a mʼmbali mwa nyanja?”

< Jérémie 47 >