< Jérémie 28 >

1 II arriva, en cette même année, au début du règne de Sédécias, roi de Juda, le cinquième mois de la quatrième année, que Hanania, fils d’Azzour, prophète natif de Gabaon, me tint ce discours dans le Temple de l’Eternel, en présence des prêtres et de tout le peuple:
Chaka chomwecho mwezi wachisanu wa chaka chachinayi, poyambirira pa ulamuliro wa Zedekiya mfumu ya Yuda, mneneri Hananiya mwana wa Azuri, amene amachokera ku Gibiyoni, anandiwuza ine mʼNyumba ya Yehova pamaso pa ansembe ndi anthu onse kuti,
2 "Ainsi parle l’Eternel-Cebaot, Dieu d’Israël: Je brise le joug du roi de Babylone.
“Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akuti, ‘Ndidzathyola goli la mfumu ya ku Babuloni.
3 Encore deux années, et je ferai réintégrer dans cette cité tous les vases du Temple de l’Eternel, que Nabuchodonosor, roi de Babylone, a enlevés d’ici et transportés à Babylone.
Pasanathe zaka ziwiri ndidzabweretsa pa malo ano ziwiya zonse za ku Nyumba ya Yehova zimene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni anazichotsa pa malo pano ndi kupita nazo ku Babuloni.
4 Et leconia aussi, fils de Joïakim, roi de Juda, avec tous les déportés de Juda, qui sont arrivés à Babylone, je les ramènerai en ces lieux, dit l’Eternel, car je vais briser le joug du roi de Babylone."
Ndidzabweretsanso pa malo pano Yekoniya mwana wa Yehoyakimu mfumu ya Yuda pamodzi ndi akapolo ena onse ochokera ku Yuda amene anapita ku Babuloni,’ akutero Yehova, ‘chifukwa ndidzathyola goli la mfumu ya ku Babuloni.’”
5 Alors le prophète Jérémie répliqua au prophète Hanania en présence des prêtres et en présence de tout le peuple qui se tenait dans la maison de l’Eternel,
Pamenepo mneneri Yeremiya anayankha mneneri Hananiya pamaso pa ansembe ndi anthu onse amene anasonkhana mʼNyumba ya Yehova.
6 et le prophète Jérémie dit: "Amen! Ainsi fasse l’Eternel! Puisse l’Eternel accomplir la prédiction que tu as énoncée, en faisant revenir de Babylone en cette cité les vases du Temple de l’Eternel!
Anati, “Ameni! Yehova achitedi zomwezo! Yehova akwaniritse mawu amene waloserawo. Iye abweretsenso pa malo pano ziwiya za mʼNyumba ya Yehova ndi akapolo onse kuchokera ku Babuloni.
7 Toutefois écoute, je t’en prie, la parole que je fais entendre à tes oreilles et aux oreilles de tout le peuple.
Komabe, tamvera zimene nditi ndikuwuze iweyo pamodzi ndi anthu onse:
8 Les prophètes qui nous ont précédés, moi et toi, de toute antiquité, ont prédit à de puissants pays et à de grands rois des guerres, des calamités et des pestes.
Kunali aneneri kalelo, ine ndi iwe tisanabadwe. Iwowa analosera za nkhondo, mavuto ndi mliri kuti zidzagwera mayiko ambiri ndi maufumu amphamvu.
9 Mais le prophète qui prédit un événement heureux n’est reconnu comme véritablement envoyé de Dieu qu’autant que sa prédiction s’accomplit."
Koma mneneri amene amalosera zamtendere adzadziwika kuti ndi woona ndi kuti watumidwa ndi Yehova ngati zimene wanenera zachitikadi.”
10 Alors le prophète Hanania saisit le joug posé sur le cou du prophète Jérémie et le brisa.
Pamenepo mneneri Hananiya anachotsa goli mʼkhosi mwa mneneri Yeremiya nalithyola,
11 Et Hanania prononça ces paroles en présence de tout le peuple: "Ainsi parle l’Eternel: C’Est de cette façon que, dans un délai de deux ans, je briserai le joug que Nabuchodonosor, roi de Babylone, fait peser sur le cou de tous les peuples." Le prophète Jérémie se retira, poursuivant son chemin.
ndipo anawuza anthu onse kuti, “Yehova akuti, ‘Umu ndi mmene ndidzathyolere goli la Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni mʼkhosi mwa anthu a mitundu yonse pasanathe zaka ziwiri.’” Zitatero, mneneri Yeremiya anachoka.
12 Puis la parole de l’Eternel fut adressée à Jérémie en ces termes, après que le prophète Hanania eût brisé le joug posé sur le cou de Jérémie:
Patapita nthawi pangʼono, mneneri Hananiya atathyola goli mʼkhosi mwa mneneri Yeremiya, Yehova anawuza Yeremiya kuti,
13 "Va et tiens à Hanania ce langage: Tu as brisé un joug de bois, tu le remplaceras par un joug de fer;
“Pita, kawuze mneneri Hananiya kuti, ‘Yehova akuti: Iwe wathyola goli lamtengo, mʼmalo mwake Ine ndidzayika goli lachitsulo.
14 car voici ce que dit l’Eternel-Cebaot, Dieu d’Israël: C’Est un joug de fer que je pose sur le cou de tous ces peuples, pour qu’ils soient soumis à Nabuchodonosor, roi de Babylone, et le servent; jusqu’aux animaux des champs, je les lui livre."
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Ndidzayika goli lachitsulo mʼkhosi mwa anthu a mitundu yonseyi kuti atumikire Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, ndipo iwo adzamutumikiradi. Ndipo ndamupatsanso ulamuliro ngakhale pa nyama zakuthengo.’”
15 Puis le prophète Jérémie dit au prophète Hanania: "Veuille écouter, Hanania! l’Eternel ne t’a pas envoyé et toi, tu as leurré ce peuple par des promesses mensongères.
Ndipo mneneri Yeremiya anawuza mneneri Hananiya kuti, “Tamvera, Hananiya! Iweyo Yehova sanakutume, koma iwe wanyenga anthuwa kuti akhulupirire zabodza.
16 C’Est pourquoi l’Eternel parle ainsi: Je vais te renvoyer de la surface de la terre; au cours de cette année tu mourras, parce que tu as prêché la révolte contre l’Eternel."
Nʼchifukwa chake Yehova akuti, ‘Ndatsala pangʼono kukuchotsa pa dziko lapansi. Iwe ufa chaka chino chisanathe, chifukwa wakhala ukulalikira zowukira Yehova.’”
17 En effet, le prophète Hanania mourut cette même année, dans le septième mois.
Mʼmwezi wachisanu ndi chiwiri wa chaka chomwecho, mneneri Hananiya anamwaliradi.

< Jérémie 28 >