< Ézéchiel 6 >

1 La parole du Seigneur me fut adressée en ces termes:
Yehova anandipatsa uthenga uwu kuti,
2 "Fils de l’homme, tourne ta face vers les montagnes d’Israël et prophétise sur elles.
“Iwe mwana wa munthu, yangʼana ku mapiri a Israeli; yankhula nawo modzudzula
3 Tu diras: Montagnes d’Israël, écoutez la parole du Seigneur Dieu! Ainsi parle le Seigneur Dieu aux montagnes et aux collines, aux torrents et aux vallées: Voici, je vais amener sur vous le glaive et je ruinerai vos hauts-lieux.
kuti, ‘Inu mapiri a ku Israeli, imvani mawu a Ambuye Yehova. Iye akuwuza mapiri, magomo, mitsinje ndi zigwa kuti: Ine ndizakuthirani nkhondo ndipo ndidzawononga nyumba zanu mʼmene mukupembedzeramo mafano.
4 Vos autels seront dévastés, vos statues solaires seront brisées, et je ferai tomber vos morts devant vos idoles.
Maguwa anu ansembe adzagumulidwa ndipo maguwa anu ofukizira lubani adzaphwanyidwa; ndipo ndidzapha anthu anu pamaso pa mafano anu.
5 Et je mettrai les cadavres des enfants d’Israël devant leurs idoles et je disperserai vos ossements autour de vos autels.
Ine ndidzagoneka mitembo ya Aisraeli pamaso pa mafano awo, ndipo ndidzamwaza mafupa anu mozungulira maguwa anu ansembe.
6 Dans tous vos établissements, les villes seront dévastées, et les hauts-lieux désolés, afin que soient ruinés et désolés vos autels, que soient brisées et anéanties vos idoles, que soient rasées vos statues solaires, et que soient effacées vos oeuvres.
Konse kumene mumakhala, mizinda yanu idzasanduka bwinja. Nyumba zanu zopembedzera mafano zidzagumulidwa kotero kuti maguwa anu adzawonongedwa ndi kusakazidwa, mafano anu adzaphwanyidwa ndi kuwonongedwa. Maguwa anu ofukizirapo lubani adzagwetsedwa pansi ndipo zonse zimene munapanga zidzatheratu.
7 Des morts tomberont au milieu de vous, et vous saurez que je suis le Seigneur.
Anthu anu adzaphedwa pakati panu, ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
8 Et si j’en épargne parmi vous qui échapperont au glaive parmi les nations, quand vous serez dispersés dans les pays,
“Komabe ndidzasiya ena pangʼono opulumuka ku nkhondo. Iwowa ndidzawamwazira ku mayiko ena pakati pa anthu a mitundu ina.
9 ces survivants parmi vous se souviendront de moi chez les nations où ils seront captifs, de moi qui aurai brisé leur coeur infidèle, qui s’est détourné de moi, et leurs yeux qui s’égaraient vers leurs idoles; et ils éprouveront le dégoût d’eux-mêmes à cause des méfaits qu’ils ont commis, par toutes leurs abominations.
Pamenepo opulumuka mwa inu adzandikumbukira ku mayiko kumene anatengedwa ukapolo. Ndidzawamvetsa chisoni chifukwa cha kusakhulupirika kwawo ndi kundipandukira kuja ndiponso chifukwa kuti anayika mtima wawo pa mafano. Choncho adzachita okha manyazi chifukwa cha zoyipa zimene ankachita ndi miyambo yonyansa imene ankatsata.
10 Ils sauront que je suis le Seigneur, que je n’ai pas parlé en vain en les menaçant de ce malheur."
Ndipo iwo adzadziwa kuti ndine Yehova ndi kuti sindinkawaopseza chabe pamene ndinanena kuti ndidzawawononga.
11 Ainsi a dit le Seigneur Dieu: "Frappe de la main et tape du pied et dis: "Hélas!" Au sujet de toutes les horreurs impies des gens de la maison d’Israël, qui tomberont par le glaive, par la famine et par la peste.
“Ambuye Yehova akuti: Womba mʼmanja mwako ndipo uponde mapazi ako pansi mwamphamvu ndipo ufuwule kuti, ‘Mayo!’ chifukwa cha zonyansa ndi zoyipa zonse zimene Aisraeli achita, pakuti adzaphedwa ndi lupanga, njala ndi mliri.
12 Celui qui est loin mourra par la peste, celui qui est proche tombera sous le glaive, survivants et assiégés périront par la famine, et j’épuiserai ma fureur sur eux.
Amene ali kutali adzafa ndi mliri, ndipo amene ali pafupi adzafa pa nkhondo, ndipo amene adzapulumuke ndi kusaphedwa adzafa ndi njala. Kotero ndidzakwaniritsa ukali wanga pa iwo.
13 Et vous saurez que je suis le Seigneur, quand leurs cadavres seront couchés au milieu de leurs idoles, autour de leurs autels, sur chaque haute colline, sur toutes les cimes des montagnes, sous chaque arbre verdoyant et sous chaque chêne touffu, en tout endroit où ils offraient une odeur agréable à toutes leurs idoles.
Ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene anthu awo adzagona atafa pakati pa mafano awo mozungulira maguwa awo ansembe, pamwamba pa magomo ndi mapiri onse, pansi pa mtengo uliwonse watambalala ndi wa thundu uliwonse wamasamba ambiri, kumalo kumene ankapereka nsembe zonunkhira kwa mafano awo onse.
14 J’Étendrai ma main sur eux et je ferai du pays une solitude et une ruine pire que le désert de Diblat, partout où ils seront établis, et ils sauront que je suis l’Eternel."
Choncho ndidzawalanga ndi mkono wanga ndi kusandutsa dziko kukhala bwinja. Dziko lonse kumene akukhala kuyambira ku chipululu mpaka ku mzinda wa Ribula ndidzalisandutsa bwinja. Pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

< Ézéchiel 6 >