< 2 Chroniques 30 >

1 Ezéchias envoya un message à tout Israël et Juda; il écrivit aussi des lettres à Ephraïm et Manassé, les invitant à venir au temple de l’Eternel à Jérusalem, pour célébrer la Pâque en l’honneur de l’Eternel, Dieu d’Israël.
Hezekiya anatumiza uthenga mʼdziko lonse la Israeli ndi ku Yuda ndiponso analemba makalata ku Efereimu ndi Manase, oyitana anthu kuti abwere ku Nyumba ya Yehova ku Yerusalemu kudzakondwerera Paska wa Yehova, Mulungu wa Israeli.
2 Le roi et ses chefs et toute la communauté de Jérusalem furent d’avis de célébrer la Pâque au second mois.
Mfumu ndi akuluakulu ake pamodzi ndi anthu onse a mu Yerusalemu anagwirizana kuti akondwerere Paska pa mwezi wachiwiri.
3 Car ils n’avaient pu la célébrer en ce temps-là, parce que les prêtres ne s’étaient pas sanctifiés en nombre suffisant et que le peuple ne s’était pas réuni à Jérusalem.
Iwo sanathe kukondwerera pa nthawi yake chifukwa si ansembe ambiri amene anadziyeretsa ndiponso anthu anali asanasonkhane mu Yerusalemu.
4 La chose plut aux yeux du roi et aux yeux de toute l’assemblée,
Chikonzerochi chinaoneka kuti chinali chabwino kwa mfumu pamodzi ndi anthu onse.
5 et ils décidèrent de proclamer par tout Israël, de Bersabée à Dan, qu’on eût à venir célébrer la Pâque en l’honneur de l’Eternel, Dieu d’Israël, à Jérusalem, car on ne l’avait pas de longtemps célébrée ainsi qu’il était écrit.
Iwo anagwirizana zoti alengeze mu Israeli monse kuyambira ku Beeriseba mpaka ku Dani, kuyitana anthu kuti abwere ku Yerusalemu ndi kudzakondwerera Paska wa Yehova, Mulungu wa Israeli. Si ambiri amene ankachita chikondwererochi monga momwe kunalembedwera.
6 Les courriers partirent, nantis des lettres de la main du roi et de ses chefs, dans tout Israël et Juda, pour dire, conformément à l’ordonnance du roi: "Enfants d’Israël, revenez à l’Eternel, Dieu d’Abraham, d’Isaac et d’Israël, afin qu’il revienne à ce reste de vous qui a pu échapper à la main des rois d’Assyrie.
Molamulidwa ndi mfumu, amithenga anapita mu Israeli yense ndi Yuda ndi makalata ochokera kwa mfumu ndi kwa akuluakulu ake, olembedwa kuti, “Aisraeli bwererani kwa Yehova, Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Israeli, kuti abwerere kwa inu amene mwatsala, amene mwapulumuka mʼdzanja la mafumu a ku Asiriya.
7 Ne soyez point semblables à vos pères et à vos frères, qui furent infidèles à l’Eternel, Dieu de leurs pères, de sorte qu’il les livra à la désolation, comme vous le voyez.
Musakhale ngati makolo anu ndi abale anu, amene anali osakhulupirika kwa Yehova Mulungu wa makolo awo kotero kuti anawachititsa kuti akhale chinthu chochititsa mantha, monga mukuoneramu.
8 A présent, ne roidissez pas votre nuque comme vos pères; tendez la main vers l’Eternel, venez dans son sanctuaire, qu’il a consacré à jamais, servez l’Eternel, votre Dieu, afin qu’il détourne de vous le feu de sa colère.
Musawumitse khosi monga anachitira makolo anu, Gonjerani Yehova. Bwerani ku malo opatulika, amene anawapatula kwamuyaya. Tumikirani Yehova Mulungu wanu kuti mkwiyo wake ukuchokereni.
9 C’Est par votre retour à l’Eternel que vos frères et vos enfants trouveront de la pitié auprès de leurs ravisseurs, de façon à retourner dans ce pays, car clément et miséricordieux est l’Eternel, votre Dieu, et il ne détournera pas sa face de vous, si vous revenez à lui."
Ngati inu mubwerera kwa Yehova, pamenepo abale anu ndi ana anu adzachitiridwa chifundo ndi amene anawagwira ukapolo ndipo adzabwereranso ku dziko lino pakuti Yehova, Mulungu wanu ndi wokoma mtima ndi wachifundo. Iye sadzakufulatirani ngati inuyo mubwerera kwa Iye.”
10 Les courriers passèrent de ville en ville dans le pays d’Ephraïm et de Manassé jusqu’en Zabulon, mais on se railla d’eux et on les bafoua.
Amithenga aja anapita mzinda ndi mzinda wa ku Efereimu ndi Manase mpaka ku Zebuloni, koma anthu anawanyoza ndi kuwachita chipongwe.
11 Seuls des hommes d’Aser, de Manassé et de Zabulon s’humilièrent et vinrent à Jérusalem.
Komabe anthu ena a ku Aseri, Manase ndi Zebuloni anadzichepetsa ndipo anapita ku Yerusalemu.
12 En Juda aussi la main de Dieu agit pour leur donner un même cœur, afin d’accomplir l’ordre du roi et des chefs selon la prescription de l’Eternel.
Dzanja la Mulungu linalinso pa anthu a ku Yuda, kuwapatsa mtima umodzi wochita zimene mfumu ndi akuluakulu ake analamula potsata mawu a Yehova.
13 Une population nombreuse se réunit à Jérusalem pour célébrer la fête des azymes au second mois; ce fut une affluence énorme.
Gulu lalikulu la anthu linasonkhana mu Yerusalemu kudzachita chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti pa mwezi wachiwiri.
14 Ils se levèrent, ôtèrent les autels qui se trouvaient à Jérusalem; ils enlevèrent aussi les encensoirs et les jetèrent au torrent du Cédron.
Anachotsa mu Yerusalemu maguwa ofukizira lubani ndipo anakawaponya mʼchigwa cha Kidroni.
15 Puis ils immolèrent le sacrifice pascal le quatorze du second mois; les prêtres et les Lévites eurent honte, se sanctifièrent et apportèrent des holocaustes au temple de l’Eternel.
Iwo anapha mwana wankhosa wa Paska pa tsiku la 14 la mwezi wachiwiri. Ansembe ndi Alevi anachita manyazi ndipo anadziyeretsa ndi kubweretsa nsembe zopsereza ku Nyumba ya Yehova.
16 Ils se tinrent à leur place selon leur règle, conformément à la loi de Moïse, homme de Dieu; les prêtres versaient le sang que leur passaient les Lévites.
Ndipo anakhala mʼmalo awo a nthawi zonse potsatira zolembedwa mʼmalamulo a Mose munthu wa Mulungu. Ansembe anawaza magazi amene anawapatsa Alevi.
17 Car il y en avait beaucoup dans l’assemblée qui ne s’étaient point sanctifiés, et les Lévites étaient chargés d’immoler les sacrifices pascaux pour tous ceux qui n’étaient pas purs, afin de les consacrer à l’Eternel.
Popeza ambiri mʼgululo anali asanadziyeretse, Alevi anapha ana ankhosa a Paska a iwo amene, mwa mwambo, anali osayeretsedwa ndipo sakanatha kupereka ana ankhosa awo kwa Yehova.
18 Une grande partie du peuple, beaucoup de gens d’Ephraïm et de Manassé, d’Issachar et de Zabulon, ne s’étaient pas purifiés; ils avaient mangé l’agneau pascal sans égard aux prescriptions; mais Ezéchias avait intercédé pour eux, disant: "L’Eternel, qui est bon, absoudra
Ngakhale kuti ambiri mwa anthu ochokera ku Efereimu, Manase, Isakara ndi Zebuloni sanadziyeretse okha, komabe anadya Paska motsutsana ndi zimene zinalembedwa. Koma Hezekiya anawapempherera, kunena kuti, “Yehova wabwino, khululukirani aliyense
19 quiconque aura disposé son cœur à rechercher l’Eternel, Dieu de ses pères, même sans la purification de sainteté."
amene wayika mtima wake kufunafuna Yehova, Mulungu wa makolo ake, ngakhale ali wosayeretsedwa molingana ndi malamulo a malo opatulika.”
20 L’Eternel exauça Ezéchias et pardonna au peuple.
Ndipo Yehova anamvera Hezekiya ndipo anachiritsa anthuwo.
21 Les enfants d’Israël se trouvant à Jérusalem célébrèrent donc la fête des Azymes sept jours, en grande joie, et les Lévites et les prêtres louèrent l’Eternel jour par jour, avec des instruments puissants en l’honneur de l’Eternel.
Aisraeli amene anali mu Yerusalemu anachita chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti kwa masiku asanu ndi awiri akusangalala kwambiri, pamene Alevi ndi ansembe amayimbira Yehova tsiku lililonse, akuyimbira zida zamatamando za Yehova.
22 Ezéchias adressa des encouragements à tous les Lévites qui se montraient très entendus au service de l’Eternel. Ils consommèrent les repas de la fête durant les sept jours, offrant des sacrifices d’actions de grâces et rendant hommage à l’Eternel, Dieu de leurs pères.
Hezekiya anayankhula molimbikitsa Alevi onse amene anaonetsa kumvetsa bwino za kutumikira Yehova. Kwa masiku asanu ndi awiri anadya gawo lawo ndi kupereka nsembe zachiyanjano ndi kutamanda Yehova, Mulungu wa makolo awo.
23 Toute l’assemblée fut d’accord pour célébrer sept autres jours, et ils célébrèrent sept jours de réjouissances.
Ndipo msonkhano wonse unagwirizana zopitiriza chikondwerero kwa masiku ena asanu ndi awiri. Kotero kwa masiku ena asanu ndi awiri anachita chikondwererocho mosangalala.
24 Car Ezéchias, roi de Juda, avait prélevé pour l’assemblée mille taureaux et sept mille moutons, les chefs avaient prélevé pour l’assemblée mille taureaux et dix mille moutons et des prêtres s’étaient sanctifiés en grand nombre.
Hezekiya mfumu ya Yuda anapereka ngʼombe zamphongo 1,000 ndi nkhosa ndi mbuzi 7,000 ku msonkhanoko ndipo akuluakulu ake anapereka ngʼombe zamphongo 1,000, nkhosa ndi mbuzi 10,000. Ansembe ambiri anadziyeretsa.
25 Toute l’assemblée de Juda se réjouit, ainsi que les prêtres, les Lévites, toute la foule venue du pays d’Israël et les étrangers, ceux qui étaient venus du pays d’Israël et ceux qui résidaient en Juda.
Gulu lonse la ku Yuda linasangalala, pamodzi ndi ansembe ndi Alevi ndi onse amene anasonkhana ochokera ku Israeli, kuphatikizanso alendo amene anachokera ku Israeli ndi amene amakhala ku Yuda.
26 Il y eut une grande joie à Jérusalem, car depuis le temps de Salomon, fils de David, roi d’Israël, il n’y avait rien eu de semblable à Jérusalem.
Munali chikondwerero chachikulu mu Yerusalemu, pakuti kuyambira masiku a Solomoni mwana wa Davide mfumu ya Israeli sizinachitikepo zotere mu Yerusalemu.
27 Les prêtres et les Lévites se levèrent et bénirent le peuple; leur voix fut entendue et leur prière parvint au séjour de Sa sainteté, aux cieux.
Ansembe ndi Alevi anayimirira kudalitsa anthu, ndipo Mulungu anawamvera pakuti pemphero lawo linafika kumwamba, malo ake oyera.

< 2 Chroniques 30 >