< Nombres 32 >

1 Et les troupeaux des fils de Ruben et des fils de Gad étaient en grand nombre, en très grande quantité. Et ils virent le pays de Jahzer et le pays de Galaad, et voici, le lieu était un lieu propre pour des troupeaux.
Arubeni ndi Agadi amene anali ndi ngʼombe zambiri ndi ziweto zina anaona dziko la Yazeri ndi la Giliyadi kuti linali labwino kwa ziwetozo.
2 Et les fils de Gad et les fils de Ruben vinrent, et parlèrent à Moïse et à Éléazar, le sacrificateur, et aux princes de l’assemblée, disant:
Choncho Arubeni ndi Agadi anapita kwa Mose ndi kwa wansembe Eliezara ndi kwa atsogoleri a anthu ndi kunena kuti,
3 Ataroth, et Dibon, et Jahzer, et Nimra, et Hesbon, et Elhalé, et Sebam, et Nebo, et Béon,
“Ataroti, Diboni, Yazeri, Nimira, Hesiboni, Eleali, Sebamu, Nebo ndi Beoni,
4 le pays que l’Éternel a frappé devant l’assemblée d’Israël, est un pays propre pour des troupeaux, et tes serviteurs ont des troupeaux.
dziko lomwe Yehova anagonjetsa pamaso pa Aisraeli, ndiwo malo woyenera ziweto, ndipo atumiki anufe tili ndi ziweto.
5 Et ils dirent: Si nous avons trouvé faveur à tes yeux, que ce pays soit donné en possession à tes serviteurs; ne nous fais pas passer le Jourdain.
Iwo anati, ‘Ngati tapeza ufulu pamaso panu atumiki anufe, mutipatse dziko limeneli kuti likhale lathu. Tisawoloke nanu Yorodani.’”
6 Et Moïse dit aux fils de Gad et aux fils de Ruben: Vos frères iront-ils à la guerre, et vous, vous habiterez ici?
Ndipo Mose anati kwa Agadi ndi Arubeni, “Kodi anthu a mtundu wanu apite ku nkhondo inu mutangokhala kuno?
7 Et pourquoi découragez-vous les fils d’Israël de passer dans le pays que l’Éternel leur a donné?
Chifukwa chiyani mukufowoketsa Aisraeli kupita mʼdziko limene Yehova wawapatsa?
8 Ainsi firent vos pères lorsque je les envoyai de Kadès-Barnéa pour voir le pays:
Izi ndi zimene makolo anu anachita pamene ndinawatuma kuchokera ku Kadesi kukaona dzikolo.
9 ils montèrent à la vallée d’Eshcol, et virent le pays; et ils découragèrent les fils d’Israël, afin qu’ils n’entrent pas dans le pays que l’Éternel leur avait donné.
Atapita ku chigwa cha Esikolo, ndi kuliona dzikolo, anafowoketsa Aisraeli kuti asalowe mʼdziko limene Yehova anawapatsa.
10 Et la colère de l’Éternel s’embrasa en ce jour-là, et il jura, disant:
Yehova anakwiya tsiku limenelo ndipo analumbira kuti,
11 Si les hommes qui sont montés d’Égypte, depuis l’âge de 20 ans et au-dessus, voient la terre que j’ai promise par serment à Abraham, à Isaac, et à Jacob! car ils ne m’ont pas pleinement suivi,
‘Chifukwa sananditsatire ndi mtima wonse, palibe ndi mmodzi yemwe mwa amuna a zaka makumi awiri kapena kuposa pamenepo, amene anachokera ku Igupto, amene adzaone dziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
12 – excepté Caleb, fils de Jephunné, le Kenizien, et Josué, fils de Nun, car ils ont pleinement suivi l’Éternel.
Palibe ndi mmodzi yemwe kupatula Kalebe mwana wa Yefune, Mkeni, ndi Yoswa mwana wa Nuni chifukwa anatsatira Yehova ndi mtima wonse.’
13 Et la colère de l’Éternel s’embrasa contre Israël, et il les a fait errer dans le désert 40 ans, jusqu’à ce qu’ait péri toute la génération qui avait fait ce qui est mauvais aux yeux de l’Éternel.
Yehova anakwiyira Aisraeli kwambiri ndipo anawachititsa kuyenda mʼchipululu zaka makumi anayi, mpaka mʼbado wonse wa anthu amene anachita choyipa pamaso pake unatha.
14 Et voici, vous vous êtes levés à la place de vos pères, une progéniture d’hommes pécheurs, pour ajouter encore à l’ardeur de la colère de l’Éternel contre Israël.
“Ndipo onani tsopano, inu mʼbado wochimwa, mwalowa mʼmalo mwa makolo anu ndipo mwachititsa kuti Yehova akwiyire Israeli kwambiri.
15 Si vous vous détournez de lui, il le laissera encore dans le désert, et vous détruirez tout ce peuple.
Ngati muleka kumutsata, Iye adzawasiyiranso anthu onsewa mʼchipululu ndipo mudzawonongetsa anthu onsewa.”
16 Et ils s’approchèrent de lui, et dirent: Nous bâtirons ici des enclos pour nos troupeaux, et des villes pour nos petits enfants;
Ndipo iwo anabwera kwa Mose namuwuza kuti, “Ife tikufuna kumanga makola a ziweto zathu kuno ndi mizinda yokhalamo akazi athu ndi ana athu.
17 et nous nous équiperons promptement [pour marcher] devant les fils d’Israël, jusqu’à ce que nous les ayons introduits en leur lieu; et nos petits enfants habiteront dans les villes fortes, à cause des habitants du pays.
Koma ndife okonzeka kutenga zida za nkhondo ndi kupita pamodzi ndi Aisraeli mpaka titakawafikitsa ku malo awo. Panopa, akazi ndi ana athu akhala mʼmizinda yotetezedwa, kuwateteza kwa anthu okhala mʼdzikoli.
18 Nous ne reviendrons pas dans nos maisons, jusqu’à ce que les fils d’Israël aient pris possession chacun de son héritage;
Sitidzabwerera ku midzi yathu mpaka Mwisraeli aliyense atalandira cholowa chake.
19 car nous n’hériterons pas avec eux au-delà du Jourdain, ni plus loin, parce que notre héritage nous est échu, à nous, de ce côté du Jourdain, vers le levant.
Sitidzalandira cholowa chilichonse pamodzi nawo ku tsidya lina la Yorodani, chifukwa cholowa chathu tachipezera ku tsidya lino la kummawa kwa Yorodani.”
20 Et Moïse leur dit: Si vous faites cela, si vous vous équipez devant l’Éternel pour la guerre,
Tsono Mose anati kwa anthuwo, “Ngati inu mudzachita zimenezi, kutenga zida zankhondo pamaso pa Yehova kuti muchite nkhondo,
21 et que tous ceux d’entre vous qui sont équipés passent le Jourdain devant l’Éternel, jusqu’à ce qu’il ait dépossédé ses ennemis devant lui,
ndipo ngati nonsenu mudzapita ndi zida kuwoloka Yorodani pamaso pa Yehova mpaka atachotsa adani ake pamaso pake,
22 et que le pays soit subjugué devant l’Éternel, et qu’ensuite vous vous en retourniez, alors vous serez innocents envers l’Éternel et envers Israël; et ce pays-ci sera votre possession devant l’Éternel.
dzikolo nʼkugonja pamaso pa Yehova, mudzabwera ndi kukhala mfulu pamaso pa Yehova ndi Aisraeli. Ndipo dziko lino lidzakhala lanu pamaso pa Yehova.
23 Mais si vous ne faites pas ainsi, voici, vous pécherez contre l’Éternel; et sachez que votre péché vous trouvera.
“Koma mukalephera kuchita izi, mudzakhala mukuchimwira Yehova. Ndipo dziwani kuti tchimo lanu lidzakupezani.
24 Bâtissez-vous des villes pour vos petits enfants, et des enclos pour vos troupeaux; et ce qui est sorti de votre bouche, faites-le.
Amangireni akazi ndi ana anu mizinda, mangani makola a ziweto zanu, koma chitani zomwe mwalonjeza.”
25 Et les fils de Gad et les fils de Ruben parlèrent à Moïse, disant: Tes serviteurs feront comme mon seigneur l’a commandé.
Agadi ndi Arubeni anati kwa Mose, “Ife antchito anu tidzachita monga mbuye wathu mwalamulira.
26 Nos petits enfants, nos femmes, nos troupeaux et toutes nos bêtes seront là, dans les villes de Galaad;
Ana ndi akazi athu, ziweto zathu zina ndi ngʼombe zidzatsala kuno ku mizinda ya Giliyadi,
27 et tes serviteurs, tous équipés pour l’armée, passeront devant l’Éternel [pour aller] à la guerre, comme mon seigneur l’a dit.
koma antchito anufe, mwamuna aliyense amene ali ndi chida cha nkhondo, adzawoloka kukamenya nkhondo pamaso pa Yehova monga mbuye wathu wanenera.”
28 Et Moïse commanda à leur sujet à Éléazar, le sacrificateur, et à Josué, fils de Nun, et aux chefs des pères des tribus des fils d’Israël;
Choncho Mose anapereka malamulo awa kwa wansembe Eliezara, kwa Yoswa mwana wa Nuni ndi kwa akulu a mafuko a Aisraeli.
29 et Moïse leur dit: Si les fils de Gad et les fils de Ruben passent avec vous le Jourdain devant l’Éternel, tous équipés pour la guerre, et que le pays soit subjugué devant vous, vous leur donnerez le pays de Galaad en possession.
Mose anawawuza kuti, ngati Agadi ndi Arubeni, mwamuna aliyense wokonzekera nkhondo, awoloka Yorodani pamodzi ndi inu pamaso pa Yehova, ndipo dzikolo nʼkugonjetsedwa pamaso panu, mudzawapatse dziko la Giliyadi kukhala lawo.
30 Mais s’ils ne passent pas équipés avec vous, alors ils auront des possessions au milieu de vous dans le pays de Canaan.
Koma ngati sawoloka pamodzi nanu ndi zida zankhondo, ayenera kulandira cholowa chawo pamodzi ndi inu ku Kanaani.
31 Et les fils de Gad et les fils de Ruben répondirent, disant: Nous ferons ainsi que l’Éternel a dit à tes serviteurs;
Agadi ndi Arubeni anayankha kuti, “Antchito anu adzachita zimene Yehova wanena.
32 nous passerons équipés devant l’Éternel dans le pays de Canaan, et la possession de notre héritage en deçà du Jourdain sera à nous.
Tidzawoloka pamaso pa Yehova ndipo tidzalowa mu Kanaani ndi zida zankhondo, koma cholowa chathu chidzakhala ku tsidya lino la Yorodani.”
33 Et Moïse leur donna, – aux fils de Gad, et aux fils de Ruben, et à la demi-tribu de Manassé, fils de Joseph, – le royaume de Sihon, roi des Amoréens, et le royaume d’Og, roi de Basan, le pays, selon ses villes, dans leurs confins, les villes du pays à l’entour.
Choncho Mose anapatsa Agadi, Arubeni ndi theka la fuko la Manase mwana wa Yosefe dziko la Sihoni mfumu ya Aamori ndi dziko la Ogi, mfumu ya ku Basani, dziko lonse, mizinda yake ndi midzi yowazungulira.
34 – Et les fils de Gad bâtirent Dibon, et Ataroth, et Aroër,
Agadi anamanga Diboni, Ataroti, Aroeri,
35 et Atroth-Shophan, et Jahzer, et Jogbeha,
Atiroti-Sofani, Yazeri, Yogibeha,
36 et Beth-Nimra, et Beth-Haran, villes fortes, et des enclos pour le petit bétail.
Beti-Nimira ndi Beti-Harani mizinda ya malinga. Anamanganso makola a ziweto zawo.
37 – Et les fils de Ruben bâtirent Hesbon, et Elhalé, et Kiriathaïm,
Ndipo Arubeni anamanga Hesiboni, Eleali, Kiriataimu,
38 et Nebo, et Baal-Méon, dont les noms furent changés, et Sibma; et ils donnèrent d’autres noms aux villes qu’ils bâtirent.
Nebo ndi Baala-Meoni (mayina awa anasinthidwa) ndi Sibima. Anapereka mayina ku mizinda ina yomwe anamangayo.
39 – Et les fils de Makir, fils de Manassé, allèrent dans [le pays de] Galaad, et le prirent, et dépossédèrent les Amoréens qui y étaient.
Zidzukulu za Makiri mwana wa Manase zinapita ku Giliyadi kulanda mzindawo ndi kuthamangitsira kunja Aamori omwe anali kumeneko.
40 Et Moïse donna Galaad à Makir, fils de Manassé, et il y habita.
Tsono Mose anapereka Giliyadi kwa Amakiri, ana a Manase, ndipo anakhala kumeneko.
41 Et Jaïr, fils de Manassé, alla, et prit leurs bourgs, et les appela bourgs de Jaïr.
Yairi, mwana wa Manase analanda midzi yambiri ya Giliyadi ndi kuyitcha kuti Havoti-Yairi.
42 Et Nobakh alla, et prit Kenath et les villages de son ressort, et il l’appela Nobakh, d’après son nom.
Ndipo Noba analanda Kenati ndi midzi yozungulira ndi kuyitcha Noba, kutengera dzina la iye mwini.

< Nombres 32 >