< Job 8 >

1 Et Bildad, le Shukhite, répondit et dit:
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 Jusques à quand diras-tu ces choses, et les paroles de ta bouche seront-elles un vent impétueux?
“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
3 Est-ce que Dieu pervertit le droit? Le Tout-puissant pervertira-t-il la justice?
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 Si tes fils ont péché contre lui, il les a aussi livrés en la main de leur transgression.
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
5 Si tu recherches Dieu et que tu supplies le Tout-puissant,
Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 Si tu es pur et droit, certainement il se réveillera maintenant en ta faveur, et rendra prospère la demeure de ta justice;
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
7 Et ton commencement aura été petit, mais ta fin sera très grande.
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
8 Car interroge, je te prie, la génération précédente, et sois attentif aux recherches de leurs pères;
“Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 Car nous sommes d’hier et nous n’avons pas de connaissance, car nos jours sont une ombre sur la terre.
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 Ceux-là ne t’enseigneront-ils pas, ne te parleront-ils pas, et de leurs cœurs ne tireront-ils pas des paroles?
Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 Le papyrus s’élève-t-il où il n’y a pas de marais? Le roseau croît-il sans eau?
Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 Encore dans sa verdeur, sans qu’on l’ait arraché, avant toute herbe il sèche.
Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 Tels sont les sentiers de tous ceux qui oublient Dieu; et l’attente de l’impie périra;
Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 Son assurance sera retranchée, et sa confiance sera une toile d’araignée:
Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 Il s’appuiera sur sa maison, et elle ne tiendra pas; il s’y cramponnera, et elle ne restera pas debout.
Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 Il est verdoyant devant le soleil, et son rameau s’étend sur son jardin;
Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 Ses racines s’entrelacent dans un tas de rocaille, il voit la demeure des pierres;
mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 S’Il l’ôte de sa place, celle-ci le désavouera: Je ne t’ai pas vu!
Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 Telles sont les délices de ses voies; et de la poussière, d’autres germeront.
Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 Voici, Dieu ne méprisera pas l’homme parfait, et ne soutiendra pas les mains des méchants:
“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 Tandis qu’il remplira ta bouche de rire et tes lèvres de chants de joie,
Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 Ceux qui te haïssent seront revêtus de honte, et la tente des méchants ne sera plus.
Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

< Job 8 >