< Psaumes 90 >

1 Prière de Moïse, homme de Dieu. Seigneur, tu as été pour nous un refuge d'âge en âge.
Pemphero la Mose munthu wa Mulungu. Ambuye, mwakhala muli malo athu okhalamo pa mibado yonse.
2 Avant que les montagnes fussent nées, et que tu eusses enfanté la terre et le monde, de l'éternité à l'éternité tu es, ô Dieu!
Mapiri asanabadwe, musanalenge nʼkomwe dziko lapansi ndi dziko lonse, kuyambira muyaya mpaka muyaya Inu ndinu Mulungu.
3 Tu réduis les mortels en poussière, et tu dis: " Retournez, fils de l'homme! "
Inu mumabwezera anthu ku fumbi, mumati, “Bwerera ku fumbi iwe mwana wa munthu.”
4 Car mille ans sont, à tes yeux, comme le jour d'hier, quand il passe, et comme une veille de la nuit.
Pakuti zaka 1,000 pamaso panu zili ngati tsiku limene lapita kapena ngati kamphindi ka usiku.
5 Tu les emportes, semblables à un songe; le matin, comme l'herbe, ils repoussent:
Inu mumasesa anthu mʼtulo ta imfa, iwo ali ngati udzu watsopano wa mmawa,
6 le matin, elle fleurit et pousse; le soir, elle se flétrit et se dessèche.
ngakhale kuti mmawa umaphuka watsopano, pofika madzulo wauma ndi kufota.
7 Ainsi nous sommes consumés par ta colère, et ta fureur nous terrifie.
Ife tathedwa ndi mkwiyo wanu; ndipo taopsezedwa ndi kuyipidwa kwanu.
8 Tu mets devant toi nos iniquités, nos fautes cachées à la lumière de ta face.
Mwayika mphulupulu zathu pamaso panu, machimo athu obisika poonekera pamaso panu.
9 Tous nos jours disparaissent par ton courroux, nous voyons nos années s'évanouir comme un son léger.
Masiku athu onse amatha ali pansi pa ukali wanu; timatsiriza zaka zathu ndi kubuwula.
10 Nos jours s'élèvent à soixante-dix ans, et dans leur pleine mesure à quatre-vingts ans; et leur splendeur n'est que peine et misère, car ils passent vite, et nous nous envolons!
Kuchuluka kwa masiku athu ndi 70, kapena 80 ngati tili ndi mphamvu; komabe zaka zonsezi ndi za mavuto ndi nkhawa, zimatha mofulumira ndipo ife timawulukira kutali.
11 Qui comprend la puissance de ta colère, et ton courroux, selon la crainte qui t'est due?
Kodi ndani amadziwa mphamvu ya mkwiyo wanu? Pakuti ukali wanu ndi waukulu ngati ulemu umene uyenera Inu.
12 Enseigne-nous à bien compter nos jours. afin que nous acquérions un cœur sage.
Tiphunzitseni kuwerenga masiku athu molondola, kuti tikhale ndi mtima wanzeru.
13 Reviens, Yahweh; jusques à quand? Aie pitié de tes serviteurs.
Lezani mtima Inu Yehova! Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Achitireni chifundo atumiki anu.
14 Rassasie-nous le matin de ta bonté, et nous serons tous nos jours dans la joie et l'allégresse.
Mutikhutitse mmawa ndi chikondi chanu chosatha, kuti tiyimbe ndi chimwemwe ndi kukhala okondwa masiku athu onse.
15 Réjouis-nous autant de jours que tu nous as humiliés, autant d'années que nous avons connu le malheur.
Tisangalatseni masiku ambiri monga masiku amene mwatisautsa, kwa zaka zambiri monga momwe tinaonera mavuto.
16 Que ton œuvre se manifeste à tes serviteurs, ainsi que ta gloire, pour leurs enfants!
Ntchito zanu zionetsedwe kwa atumiki anu, kukongola kwanu kwa ana awo.
17 Que la faveur de Yahweh, notre Dieu, soit sur nous! Affermis pour nous l'ouvrage de nos mains; oui, affermis l'ouvrage de nos mains!
Kukoma mtima kwa Ambuye Mulungu wathu kukhale pa ife; tikhazikitsireni ntchito ya manja athu; inde, khazikitsani ntchito ya manja athu.

< Psaumes 90 >