< Job 8 >

1 Et Bildad, le Shuhite, prit la parole,
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 « Jusqu'à quand direz-vous ces choses? Les paroles de ta bouche seront-elles un vent puissant?
“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
3 Dieu pervertit-il la justice? Ou le Tout-Puissant pervertit-il la justice?
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 Si vos enfants ont péché contre lui, il les a livrés entre les mains de leur désobéissance.
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
5 Si vous voulez chercher Dieu avec diligence, faites vos supplications au Tout-Puissant.
Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 Si tu étais pur et droit, sûrement maintenant il se réveillerait pour vous, et faire prospérer la demeure de ta justice.
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
7 Bien que tes débuts aient été modestes, mais votre fin dernière augmenterait considérablement.
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
8 « Veuillez vous renseigner sur les générations passées. Découvrez l'apprentissage de leurs pères.
“Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 (Car nous ne sommes que d'hier, et nous ne savons rien, car nos jours sur terre ne sont qu'une ombre).
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 Ne vous apprendront-ils pas, ne vous diront-ils pas, et de prononcer des paroles venant de leur cœur?
Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 « Le papyrus peut-il pousser sans bourbe? Les joncs peuvent-ils pousser sans eau?
Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 Pendant qu'il est encore dans sa verdure, ne le coupez pas, il se fane avant tout autre roseau.
Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 Il en est de même des chemins de tous ceux qui oublient Dieu. L'espoir de l'homme impie périra,
Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 dont la confiance se brisera, dont la confiance est une toile d'araignée.
Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 Il s'appuie sur sa maison, mais elle ne tient pas debout. Il s'y accrochera, mais cela ne durera pas.
Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 Il est vert devant le soleil. Ses pousses sortent le long de son jardin.
Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 Ses racines s'enroulent autour de l'amas de pierres. Il voit la place des pierres.
mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 S'il est détruit de son lieu, alors il le reniera, en disant: « Je ne t'ai pas vu.
Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 Voici la joie de son chemin. De la terre, d'autres jailliront.
Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 « Voici, Dieu ne rejette pas un homme irréprochable, Il ne soutiendra pas non plus les malfaiteurs.
“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 Il remplira encore ta bouche de rires, tes lèvres en criant.
Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 Ceux qui te haïssent seront vêtus de honte. La tente des méchants ne sera plus. »
Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

< Job 8 >