< Jobin 12 >

1 Job vastasi ja sanoi:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 "Totisesti, te yksin olette kansa, ja teidän mukananne kuolee viisaus!
“Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
3 Onhan minullakin ymmärrystä yhtä hyvin kuin teillä; en ole minä teitä huonompi, ja kuka ei moisia tietäisi?
Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
4 Ystävänsä pilkkana on hän, jota Jumala kuuli, kun hän häntä huusi, hurskas, nuhteeton on pilkkana.
“Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
5 Turvassa olevan mielestä sopii onnettomuudelle ylenkatse; se on valmiina niille, joiden jalka horjuu.
Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
6 Ja rauhassa ovat väkivaltaisten majat, turvassa ne, jotka ärsyttävät Jumalaa, ne, jotka kantavat jumalansa kourassaan." -
Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
7 "Mutta kysypä eläimiltä, niin ne opettavat sinua, ja taivaan linnuilta, niin ne ilmoittavat sinulle;
“Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
8 tahi tutkistele maata, niin se opettaa sinua, ja meren kalat kertovat sinulle.
kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
9 Kuka kaikista näistä ei tietäisi, että Herran käsi on tämän tehnyt,
Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
10 hänen, jonka kädessä on kaiken elävän sielu ja kaikkien ihmisolentojen henki?" -
Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
11 "Eikö korva koettele sanoja ja suulaki maista ruuan makua?"
Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
12 "Vanhuksilla on viisautta, ja pitkä-ikäisillä ymmärrystä." -
Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
13 "Jumalalla on viisaus ja voima, hänellä neuvo ja ymmärrys.
“Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
14 Jos hän repii maahan, niin ei rakenneta jälleen; kenen hän telkeää sisälle, sille ei avata.
Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
15 Katso, hän salpaa vedet, ja syntyy kuivuus; hän laskee ne irti, ja ne mullistavat maan.
Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
16 Hänen on väkevyys ja ymmärrys; hänen on niin eksynyt kuin eksyttäjäkin.
Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
17 Hän vie neuvosmiehet pois paljaiksi riistettyinä ja tekee tuomarit tyhmiksi.
Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
18 Kuningasten kurituksesta hän kirvoittaa ja köyttää köyden heidän omiin vyötäisiinsä.
Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
19 Hän vie papit pois paljaiksi riistettyinä, ja ikimahtavat hän kukistaa.
Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
20 Hän hämmentää luotettavain puheen ja ottaa pois vanhoilta taidon.
Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
21 Hän vuodattaa ylenkatsetta ruhtinasten päälle ja aukaisee virtojen padot.
Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
22 Hän paljastaa syvyydet pimeyden peitosta ja tuo valoon pilkkopimeän.
Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
23 Hän korottaa kansat, ja hän hävittää ne, hän laajentaa kansakunnat, ja hän kuljettaa ne pois.
Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
24 Maan kansan päämiehiltä hän ottaa ymmärryksen ja panee heidät harhailemaan tiettömissä autioissa.
Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
25 He haparoivat pimeässä valoa vailla, ja hän panee heidät hoipertelemaan kuin juopuneet."
Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.

< Jobin 12 >