< Psalms 137 >

1 By rivers of Babylon — There we did sit, Yea, we wept when we remembered Zion.
Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira pamene tinakumbukira Ziyoni.
2 On willows in its midst we hung our harps.
Kumeneko, pa mitengo ya misondozi tinapachika apangwe athu,
3 For there our captors asked us the words of a song, And our spoilers — joy: 'Sing ye to us of a song of Zion.'
pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo. Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo; iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”
4 How do we sing the song of Jehovah, On the land of a stranger?
Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova mʼdziko lachilendo?
5 If I forget thee, O Jerusalem, my right hand forgetteth!
Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu, dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.
6 My tongue doth cleave to my palate, If I do not remember thee, If I do not exalt Jerusalem above my chief joy.
Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu, ngati sindiyesa iwe chimwemwe changa chachikulu.
7 Remember, Jehovah, for the sons of Edom, The day of Jerusalem, Those saying, 'Rase, rase to its foundation!'
Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita pa tsiku limene Yerusalemu anagonja. Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi mpaka pa maziko ake!”
8 O daughter of Babylon, O destroyed one, O the happiness of him who repayeth to thee thy deed, That thou hast done to us.
Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa, wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera pa zimene watichitira.
9 O the happiness of him who doth seize, And hath dashed thy sucklings on the rock!
Amene adzagwira makanda ako ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.

< Psalms 137 >