< Joshua 1 >

1 And it cometh to pass after the death of Moses, servant of Jehovah, that Jehovah speaketh unto Joshua son of Nun, minister of Moses, saying,
Atamwalira Mose mtumiki wa Mulungu, Yehova anati kwa Yoswa mwana wa Nuni mthandizi wa Mose:
2 'Moses my servant is dead, and now, rise, pass over this Jordan, thou, and all this people, unto the land which I am giving to them, to the sons of Israel.
“Mose mtumiki wanga wamwalira. Ndipo iwe ndi anthu onsewa, tsopano konzekani kuwoloka mtsinje wa Yorodani kupita ku dziko limene ndiwapatse Aisraeli onse.
3 'Every place on which the sole of your foot treadeth, to you I have given it, as I have spoken unto Moses.
Paliponse pamene phazi lanu liponde, ndikupatsani monga momwe ndinalonjezera Mose.
4 From this wilderness and Lebanon, and unto the great river, the river Phrath, all the land of the Hittites, and unto the great Sea — the going in of the sun — is your border.
Dziko lanu lidzayambira ku chipululu kummwera mpaka ku mapiri a Lebanoni kumpoto, kuchokeranso ku mtsinje waukulu wa Yufurate kummawa, mpaka dziko lonse la Ahiti, kukafika ku Nyanja Yayikulu ya kumadzulo.
5 'No man doth station himself before thee all days of thy life; as I have been with Moses, I am with thee, I do not fail thee, nor forsake thee;
Palibe munthu amene adzatha kukugonjetsa masiku onse a moyo wako. Monga Ine ndinakhalira ndi Mose, chomwechonso ndidzakhala nawe. Sindidzakusiya kapena kukataya.
6 be strong and courageous, for thou — thou dost cause this people to inherit the land which I have sworn to their fathers to give to them.
“Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima, chifukwa iwe udzatsogolera anthu awa kukalandira dziko limene Ine ndinalonjeza makolo awo kuti ndidzawapatsa.
7 'Only, be strong and very courageous, to observe to do according to all the law which Moses My servant commanded thee; thou dost not turn aside from it right or left, so that thou dost act wisely in every [place] whither thou goest;
Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima kwambiri. Usamale ndithu kuti umvere malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anakupatsa. Usachoke pa malamulo anga ndipo kulikonse kumene udzapite udzapambana.
8 the book of this law doth not depart out of thy mouth, and thou hast meditated in it by day and by night, so that thou dost observe to do according to all that is written in it, for then thou dost cause thy way to prosper, and then thou dost act wisely.
Uziwerenga Buku la Malamuloli, uzilingalira zolembedwa mʼmenemo usana ndi usiku, kuti uchite zonse zimene zinalembedwamo. Ukamatero udzapeza bwino ndi kupambana.
9 'Have not I commanded thee? be strong and courageous; be not terrified nor affrighted, for with thee [is] Jehovah thy God in every [place] whither thou goest.'
Paja ndinakulamula kuti ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima. Choncho usamachite mantha kapena kutaya mtima popeza Ine Yehova Mulungu wako ndidzakhala nawe kulikonse kumene udzapite.”
10 And Joshua commandeth the authorities of the people, saying,
Tsono Yoswa analamula atsogoleri a Aisraeli nawawuza kuti,
11 'Pass over into the midst of the camp, and command the people, saying, Prepare for yourselves provision, for within three days ye are passing over this Jordan, to go in to possess the land which Jehovah your God is giving to you to possess it.'
“Pitani ku misasa yonse ndipo muwuze anthu kuti, ‘Konzekani, mangani katundu wanu, popeza pakapita masiku atatu kuyambira lero mudzawoloka Yorodani kupita kukatenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.’”
12 And to the Reubenite, and to the Gadite, and to the half of the tribe of Manasseh, hath Joshua spoken, saying,
Koma Yoswa anawuza fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase kuti,
13 'Remember the word which Moses, servant of Jehovah, commanded you, saying, Jehovah your God is giving rest to you, and He hath given to you this land;
“Kumbukirani zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani kuti, ‘Yehova Mulungu wanu akukupatsani mpumulo, ndi dziko ili kuti likhale lanu.’
14 your wives, your infants, and your substance, abide in the land which Moses hath given to you beyond the Jordan, and ye — ye pass over by fifties, before your brethren, all the mighty ones of valour, and have helped them,
Tsono akazi anu, ana anu ndi ziweto zanu zitsale mʼdziko lino limene Mose anakupatsani kummawa kwa Yorodani. Koma ankhondo anu okha ndiwo awoloke atatenga zida zawo ndi kupita patsogolo pa abale anu kukawathandiza.
15 till that Jehovah giveth rest to your brethren as to yourselves, and they have possessed, even they, the land which Jehovah your God is giving to them; then ye have turned back to the land of your possession, and have possessed it, which Moses, servant of Jehovah, hath given to you beyond the Jordan, [at] the sun-rising.'
Abale anuwo akadzalandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akuwapatsa monga inu mwachitira, inu mudzabwerera kudzakhazikika mʼdziko lanu limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani tsidya la kummawa kwa Yorodani.”
16 And they answer Joshua, saying, 'All that thou hast commanded us we do; and unto every [place] whither thou dost send us, we go;
Kenaka iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife tidzachita chilichonse chimene mwatilamula, ndipo kulikonse kumene mudzatitume tidzapita.
17 according to all that we hearkened unto Moses [in], so we hearken unto thee; surely Jehovah thy God is with thee as He hath been with Moses.
Monga momwe tinamvera Mose kwathunthu, chomwechonso tidzakumvera iwe. Yehova Mulungu wanu akhale nanu monga momwe anachitira ndi Mose.
18 Any man who doth provoke thy mouth, and doth not hear thy words, in all that thou dost command him, is put to death; only, be strong and courageous.'
Aliyense wotsutsana ndi inu kapena wosamvera zimene mutilamula adzaphedwa. Inu mukhale wamphamvu ndi wolimba mtima!”

< Joshua 1 >