< Zephaniah 1 >

1 The word of the Lord, that was maad to Sofonye, sone of Chusi, sone of Godolie, sone of Amasie, sone of Ezechie, in the daies of Josie, the sone of Amon, king of Juda.
Yehova anayankhula ndi Zefaniya mwana wa Kusi, mwana wa Gedaliya, mwana wa Amariya, mwana wa Hezekiya pa nthawi ya Yosiya, mwana wa Amoni, mfumu ya Yuda.
2 Y gaderinge schal gadere alle thingis fro the face of erthe, seith the Lord;
“Ndidzawononga kotheratu zinthu zonse pa dziko lapansi,” akutero Yehova.
3 Y gaderynge man and beeste, Y gaderynge volatils of heuene, and fischis of the see; and fallyngis of vnpitouse men schulen be, and Y schal leese men fro face of erthe, seith the Lord.
“Ndidzawononga anthu pamodzi ndi nyama zomwe; ndidzawononga mbalame zamlengalenga ndi nsomba za mʼnyanja. Ndidzawononga anthu oyipa, ndipo ndidzafafaniza mtundu wa anthu pa dziko lonse lapansi,” akutero Yehova.
4 And Y schal stretche out myn hond on Juda, and on alle dwellers of Jerusalem; and Y schal lese fro this place the relifs of Baal, and the names of keperis of housis, with prestis;
Ndidzatambasula dzanja langa pa Yuda ndi onse okhala mu Yerusalemu. Ndidzawononga pamalo pano otsalira opembedza Baala, mayina a anthu osapembedza pamodzi ndi ansembe a mafano:
5 and hem that worschipen on roouys the knyythod of heuene, and worschipen, and sweren in the Lord, and sweren in Melchon;
amene amagwada pa madenga a nyumba zawo kupembedza zolengedwa zamumlengalenga, amene amagwada ndi kulumbira mʼdzina la Yehova, komanso mʼdzina la Moleki,
6 and whiche ben turned awei bihynde the bak of the Lord, and whiche `souyten not the Lord, nether enserchiden hym.
amene abwerera mʼmbuyo osatsata Yehova, osafunafuna kapena kupempha nzeru kwa Yehova.
7 Be ye stille fro the face of the Lord God, for niy is the dai of the Lord; for the Lord made redi a sacrifice, halewide hise clepid men.
Khalani chete pamaso pa Ambuye Yehova, chifukwa tsiku la Yehova layandikira. Yehova wakonzekera kupereka nsembe; wapatula iwo amene wawayitana.
8 And it schal be, in the dai of sacrifice of the Lord, Y schal visite on princes, and on sones of the kyng, and on alle that ben clothid with pilgrimys, ether straunge, clothing.
Pa tsiku la nsembe ya Yehova ndidzalanga akalonga ndi ana aamuna a mfumu ndi onse amene amavala zovala zachilendo.
9 And Y schal visite on ech that proudli entrith on the threisfold in that dai, whiche fillen the hous of her Lord God with wickidnesse and gile.
Pa tsiku limenelo ndidzalanga onse amene safuna kuponda pa chiwundo, amene amadzaza nyumba ya ambuye awo ndi chiwawa ndi chinyengo.
10 And ther schal be in that dai, seith the Lord, a vois of cry fro the yate of fischis, and yellynge fro the secounde yate, and greet defoulyng fro litle hillis.
“Pa tsiku limenelo,” akutero Yehova, “Kufuwula kwakukulu kudzamveka pa Chipata cha Nsomba, kulira kwa chisoni kuchokera mʼChigawo Chatsopano, ndi phokoso la kugumuka kochokera ku mapiri.
11 Yelle ye, dwelleris of Pila; al the puple of Canaan was stille togidere, alle men wlappid in siluer perischiden.
Lirani mwachisoni, inu amene mumakhala kumene kuli msika; a malonda anu onse adzapululidwa, ndiponso onse amene ali ndi siliva adzawonongedwa.
12 And it schal be, in that tyme Y schal seke Jerusalem with lanternes, and Y schal visite on alle men piyt in her darstis, whiche seien in her hertis, The Lord schal not do wel, and he schal not do yuele.
Pa nthawi imeneyo ndidzafufuzafufuza mu Yerusalemu ndi nyale ndi kulanga onse amene sakulabadira, amene ali ngati vinyo wosakhutchumulidwa, amene amaganiza kuti, ‘Yehova sadzachita chilichonse, chabwino kaya choyipa.’
13 And the strengthe of hem schal be in to rauyschyng, and the housis of hem in to desert; and thei schulen bilde housis, and schulen not enhabite; and thei schulen plaunte vyneyerdis, and thei schulen not drynke the wyn of hem.
Chuma chawo chidzafunkhidwa, nyumba zawo zidzagwetsedwa. Adzamanga nyumba, koma osakhalamo; adzadzala minda ya mpesa koma sadzamwako vinyo wake.”
14 Nyy is the greet dai of the Lord, niy and swift ful myche; the vois of the dai of the Lord is bittir, a strong man schal be in tribulacioun there.
Tsiku lalikulu la Yehova layandikira, layandikira ndipo lifika msanga. Tamverani! Kulira kwa pa tsiku la Yehova kudzakhala kowawa, ngakhale munthu wolimba mtima adzalira kwambiri.
15 `The ilke dai is a dai of wraththe, dai of tribulacioun and angwisch, dai of nedynesse and wretchidnesse, dai of derknessis and myist, dai of cloude and whirlewynd,
Tsiku limenelo lidzakhala la ukali, tsiku losautsa ndi lomvetsa chisoni, tsiku la mavuto ndi la chiwonongeko, tsiku la mdima ndi lachisoni, tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani.
16 dai of trumpe and noise on strong citees and on hiye corneris.
Tsiku loliza lipenga ndi la mfuwu wankhondo, tsiku la kugwa kwa mizinda yotetezedwa ndi nsanja za pa ngodya.
17 And Y schal troble men, and thei schulen walke as blynde, for thei han synned ayens the Lord; and the blood of hem schal be sched out as erthe, and the bodies of hem schulen be as tordis.
Ndidzabweretsa msautso pa anthu ndipo adzayenda ngati anthu osaona, chifukwa achimwira Yehova, magazi awo adzamwazika ngati fumbi ndi mnofu wawo ngati ndowe.
18 But and the siluer of hem, and gold of hem, schal not mowe delyuere hem in the dai of wraththe of the Lord; in fier of his feruour al erthe schal be deuourid, for he schal make ende with haastyng to alle men enhabitynge the erthe.
Ngakhale siliva wawo kapena golide wawo sadzatha kuwapulumutsa pa tsiku la ukali wa Yehova. Dziko lonse lapansi lidzanyeka mʼmoto wa nsanje yake chifukwa adzakantha modzidzimutsa onse okhala pa dziko lapansi.

< Zephaniah 1 >