< Psalms 90 >

1 The preier of Moises, the man of God. Lord, thou art maad help to vs; fro generacioun in to generacioun.
Pemphero la Mose munthu wa Mulungu. Ambuye, mwakhala muli malo athu okhalamo pa mibado yonse.
2 Bifore that hillis weren maad, ether the erthe and the world was formed; fro the world and in to the world thou art God.
Mapiri asanabadwe, musanalenge nʼkomwe dziko lapansi ndi dziko lonse, kuyambira muyaya mpaka muyaya Inu ndinu Mulungu.
3 Turne thou not awei a man in to lownesse; and thou seidist, Ye sones of men, be conuertid.
Inu mumabwezera anthu ku fumbi, mumati, “Bwerera ku fumbi iwe mwana wa munthu.”
4 For a thousynde yeer ben bifore thin iyen; as yistirdai, which is passid, and as keping in the niyt.
Pakuti zaka 1,000 pamaso panu zili ngati tsiku limene lapita kapena ngati kamphindi ka usiku.
5 The yeeris of hem schulen be; that ben had for nouyt.
Inu mumasesa anthu mʼtulo ta imfa, iwo ali ngati udzu watsopano wa mmawa,
6 Eerli passe he, as an eerbe, eerli florische he, and passe; in the euentid falle he doun, be he hard, and wexe drie.
ngakhale kuti mmawa umaphuka watsopano, pofika madzulo wauma ndi kufota.
7 For we han failid in thin ire; and we ben disturblid in thi strong veniaunce.
Ife tathedwa ndi mkwiyo wanu; ndipo taopsezedwa ndi kuyipidwa kwanu.
8 Thou hast set oure wickidnessis in thi siyt; oure world in the liytning of thi cheer.
Mwayika mphulupulu zathu pamaso panu, machimo athu obisika poonekera pamaso panu.
9 For alle oure daies han failid; and we han failid in thin ire. Oure yeris schulen bithenke, as an yreyn;
Masiku athu onse amatha ali pansi pa ukali wanu; timatsiriza zaka zathu ndi kubuwula.
10 the daies of oure yeeris ben in tho seuenti yeeris. Forsothe, if fourescoor yeer ben in myyti men; and the more tyme of hem is trauel and sorewe. For myldenesse cam aboue; and we schulen be chastisid.
Kuchuluka kwa masiku athu ndi 70, kapena 80 ngati tili ndi mphamvu; komabe zaka zonsezi ndi za mavuto ndi nkhawa, zimatha mofulumira ndipo ife timawulukira kutali.
11 Who knew the power of thin ire; and durste noumbre thin ire for thi drede?
Kodi ndani amadziwa mphamvu ya mkwiyo wanu? Pakuti ukali wanu ndi waukulu ngati ulemu umene uyenera Inu.
12 Make thi riythond so knowun; and make men lerned in herte bi wisdom.
Tiphunzitseni kuwerenga masiku athu molondola, kuti tikhale ndi mtima wanzeru.
13 Lord, be thou conuertid sumdeel; and be thou able to be preied on thi seruauntis.
Lezani mtima Inu Yehova! Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Achitireni chifundo atumiki anu.
14 We weren fillid eerli with thi merci; we maden ful out ioye, and we delitiden in alle oure daies.
Mutikhutitse mmawa ndi chikondi chanu chosatha, kuti tiyimbe ndi chimwemwe ndi kukhala okondwa masiku athu onse.
15 We weren glad for the daies in whiche thou madist vs meke; for the yeeris in whiche we siyen yuels.
Tisangalatseni masiku ambiri monga masiku amene mwatisautsa, kwa zaka zambiri monga momwe tinaonera mavuto.
16 Lord, biholde thou into thi seruauntis, and in to thi werkis; and dresse thou the sones of hem.
Ntchito zanu zionetsedwe kwa atumiki anu, kukongola kwanu kwa ana awo.
17 And the schynyng of oure Lord God be on vs; and dresse thou the werkis of oure hondis on vs, and dresse thou the werk of oure hondis.
Kukoma mtima kwa Ambuye Mulungu wathu kukhale pa ife; tikhazikitsireni ntchito ya manja athu; inde, khazikitsani ntchito ya manja athu.

< Psalms 90 >