< Psalms 80 >

1 To victorie; this salm is witnessing of Asaph for lilies. Thou that gouernest Israel, yyue tent; that leedist forth Joseph as a scheep. Thou that sittist on cherubym; be schewid bifore Effraym,
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Salimo la Asafu. Tcherani khutu Inu mʼbusa wa Israeli, Inu amene mumatsogolera Yosefe monga nkhosa; Inu amene mumakhala pa mpando waufumu pakati pa akerubi, walani
2 Beniamyn, and Manasses. Stire thi power, and come thou; that thou make vs saaf.
kwa Efereimu, Benjamini ndi Manase. Utsani mphamvu yanu; bwerani ndi kutipulumutsa.
3 God of vertues, turne thou vs; and schewe thi face, and we schulen be saaf.
Tibwezereni mwakale Inu Mulungu; nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
4 Lord God of vertues; hou longe schalt thou be wrooth on the preier of thi seruaunt?
Inu Mulungu Wamphamvuzonse, mpaka liti mkwiyo wanu udzanyeka kutsutsana ndi mapemphero a anthu anu?
5 Hou longe schalt thou feede vs with the breed of teeris; and schalt yyue drynke to vs with teeris in mesure?
Mwawadyetsa buledi wa misozi; mwachitisa iwo kumwa misozi yodzaza mbale.
6 Thou hast set vs in to ayenseiyng to oure neiyboris; and oure enemyes han scornyde vs.
Mwachititsa kuti tikhale gwero la mikangano pakati pa anansi athu, ndipo adani athu akutinyoza.
7 God of vertues, turne thou vs; and schewe thi face, and we schulen be saaf.
Tibwezereni mwakale Inu Mulungu Wamphamvuzonse, nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
8 Thou translatidist a vyne fro Egipt; thou castidist out hethene men, and plauntidist it.
Munatulutsa mpesa kuchoka ku Igupto; munathamangitsa anthu a mitundu ina ndi kuwudzala mpesawo.
9 Thou were leeder of the weie in the siyt therof; and thou plauntidist the rootis therof, and it fillide the lond.
Munawulimira munda wamphesawo, ndipo unamera ndi kudzaza dziko.
10 The schadewe therof hilide hillis; and the braunchis therof filliden the cedris of God.
Mapiri anaphimbidwa ndi mthunzi wake, mikungudza yamphamvu ndi nthambi zake.
11 It streiyte forth hise siouns til to the see, and the generacioun ther of `til to the flood.
Unatambalitsa nthambi zake mpaka ku nyanja, mphukira zake mpaka ku mtsinje.
12 Whi hast thou destried the wal therof; and alle men that goen forth bi the weie gaderiden awei the grapis therof?
Chifukwa chiyani mwagwetsa makoma ake kuti onse amene akudutsa athyole mphesa zake?
13 A boor of the wode distriede it; and a singuler wielde beeste deuouride it.
Nguluwe zochokera mʼnkhalango zikuwononga ndipo zirombo za mthengo zimawudya.
14 God of vertues, be thou turned; biholde thou fro heuene, and se, and visite this vyne.
Bweraninso kwa ife Inu Mulungu Wamphamvuzonse! Yangʼanani pansi muli kumwambako ndipo muone! Uyangʼanireni mpesa umenewu,
15 And make thou it perfit, which thi riythond plauntide; and biholde thou on the sone of man, which thou hast confermyd to thee.
muzu umene dzanja lanu lamanja ladzala, mwana amene inu munamukuza nokha.
16 Thingis brent with fier, and vndurmyned; schulen perische for the blamyng of thi cheer.
Mpesa wanu wadulidwa ndi kutenthedwa ndi moto; pakudzudzula kwanu anthu anu awonongeka.
17 Thin hond be maad on the man of thi riythond; and on the sone of man, whom thou hast confermed to thee.
Dzanja lanu likhale pa munthu amene ali ku dzanja lanu lamanja, mwana wa munthu amene mwalera nokha.
18 And we departiden not fro thee; thou schalt quykene vs, and we schulen inwardli clepe thi name.
Ndipo ife sitidzatembenukira kumbali kuchoka kwa Inu; titsitsimutseni ndipo tidzayitana pa dzina lanu.
19 Lord God of vertues, turne thou vs; and schewe thi face, and we schulen be saaf.
Tibwezereni mwakale Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.

< Psalms 80 >