< Psalms 76 >

1 To the victorie in orguns, `the salm of the song of Asaph. God is knowun in Judee; his name is greet in Israel.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo la Asafu. Mulungu amadziwika mu Yuda; dzina lake ndi lotchuka mu Israeli.
2 And his place is maad in pees; and his dwellyng is in Syon.
Tenti yake ili mu Salemu, malo ake okhalamo mu Ziyoni.
3 Ther he brak poweris; bowe, scheeld, swerd, and batel.
Kumeneko Iye anathyola mivi yowuluka, zishango ndi malupanga, zida zankhondo. (Sela)
4 And thou, God, liytnest wondirfuli fro euerlastynge hillis;
Wolemekezeka ndinu, wamphamvu kuposa mapiri amene ali ndi nyama zambiri.
5 alle vnwise men of herte weren troblid. Thei slepten her sleep; and alle men founden no thing of richessis in her hondis.
Anthu owuma mtima amagona atalandidwa chuma, Iwowo amagona tulo tawo totsiriza; palibe mmodzi wamphamvu amene angatukule manja ake.
6 Thei that stieden on horsis; slepten for thi blamyng, thou God of Jacob.
Pa kudzudzula kwanu, Inu Mulungu wa Yakobo, kavalo pamodzi ndi galeta zimakhala chete zitagona pansi.
7 Thou art feerful, and who schal ayenstonde thee? fro that tyme thin ire.
Inu nokha ndiye muyenera kuopedwa. Angathe kuyima pamaso panu ndani mukakwiya?
8 Fro heuene thou madist doom herd; the erthe tremblide, and restide.
Kuchokera kumwamba Inu munalengeza chiweruzo, ndipo dziko linaopa ndi kukhala chete,
9 Whanne God roos vp in to doom; to make saaf al the mylde men of erthe.
pamene Inu Mulungu munadzuka kuti muweruze, kupulumutsa onse osautsidwa mʼdziko. (Sela)
10 For the thouyt of man schal knouleche to thee; and the relifs of thouyt schulen make a feeste dai to thee.
Zoonadi, ukali wanu pa anthu umakubweretserani matamando ndipo opulumuka ku ukali wanu mumawasunga pafupi nanu.
11 Make ye a vow, and yelde ye to youre Lord God; alle that bringen yiftis in the cumpas of it.
Chitani malumbiro kwa Yehova Mulungu wanu ndipo muwakwaniritse; anthu onse omuzungulira abweretse mphatso kwa Iye amene ayenera kuopedwa.
12 To God ferdful, and to him that takith awei the spirit of prynces; to the ferdful at the kyngis of erthe.
Iye amaswa mzimu wa olamulira; amaopedwa ndi mafumu a dziko lapansi.

< Psalms 76 >